Yobu 24 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 24:1-25

1“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze?

Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?

2Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo;

amadyetsa ziweto zimene aba.

3Amalanda abulu a ana amasiye

ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.

4Amachotsa mʼmisewu anthu osauka,

ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.

5Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu,

amayendayenda kufuna chakudya;

dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.

6Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake,

ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.

7Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala;

pa nthawi yozizira amasowa chofunda.

8Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri

ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.

9Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere;

ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.

10Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala;

amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.

11Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa;

amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.

12Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda,

anthu ovulala akulirira chithandizo.

Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.

13“Pali ena amene amakana kuwala,

amene safuna kuyenda mʼkuwalako

kapena kukhala mʼnjira zake.

14Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka

ndipo amakapha osauka ndi amphawi;

nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.

15Munthu wachigololo amadikira chisisira;

iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’

ndipo amaphimba nkhope yake.

16Mbala zimathyola nyumba usiku,

koma masana zimadzitsekera;

izo zimathawa kuwala.

17Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera.

Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.

18“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi;

minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo

kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.

19Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana

ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa.

20Mayi wowabereka amawayiwala,

mphutsi zimasangalala powadya;

anthu oyipa sakumbukiridwanso

koma amathyoka ngati mtengo.

21Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana,

ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.

22Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake;

ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.

23Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka,

koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.

24Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso;

amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse;

amadulidwa ngati ngala za tirigu.

25“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza

ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

Nova Versão Internacional

Jó 24:1-25

1“Por que o Todo-poderoso não marca as datas de julgamento?

Por que aqueles que o conhecem não chegam a vê-las?

2Há os que mudam os marcos dos limites

e apascentam rebanhos que eles roubaram.

3Levam o jumento que pertence ao órfão

e tomam o boi da viúva como penhor.

4Forçam os necessitados a sair do caminho

e os pobres da terra a esconder-se.

5Como jumentos selvagens no deserto,

os pobres vão em busca de comida;

da terra deserta a obtêm para os seus filhos.

6Juntam forragem nos campos

e respigam nas vinhas dos ímpios.

7Pela falta de roupas, passam a noite nus;

não têm com que cobrir-se no frio.

8Encharcados pelas chuvas das montanhas,

abraçam-se às rochas por falta de abrigo.

9A criança órfã é arrancada do seio de sua mãe;

o recém-nascido do pobre é tomado para pagar uma dívida.

10Por falta de roupas, andam nus;

carregam os feixes, mas continuam famintos.

11Espremem azeitonas dentro dos seus muros24.11 Ou entre as pedras de moinho;

pisam uvas nos lagares, mas assim mesmo sofrem sede.

12Sobem da cidade os gemidos dos que estão para morrer,

e as almas dos feridos clamam por socorro.

Mas Deus não vê mal nisso.

13“Há os que se revoltam contra a luz,

não conhecem os caminhos dela

e não permanecem em suas veredas.

14De manhã o assassino se levanta

e mata os pobres e os necessitados;

de noite age como ladrão.

15Os olhos do adúltero ficam à espera do crepúsculo;

‘Nenhum olho me verá’, pensa ele;

e mantém oculto o rosto.

16No escuro os homens invadem casas,

mas de dia se enclausuram;

não querem saber da luz.

17Para eles a manhã é tremenda escuridão;24.17 Ou A manhã deles é como a sombra da morte;

eles são amigos dos pavores das trevas.

18“São, porém, como espuma sobre as águas;

sua parte da terra foi amaldiçoada,

e por isso ninguém vai às vinhas.

19Assim como o calor e a seca depressa consomem a neve derretida,

assim a sepultura24.19 Hebraico: Sheol. Essa palavra também pode ser traduzida por profundezas, ou morte. consome os que pecaram.

20Sua mãe os esquece, os vermes se banqueteiam neles.

Ninguém se lembra dos maus;

quebram-se como árvores.

21Devoram a estéril e sem filhos

e não mostram bondade para com a viúva.

22Mas Deus, por seu poder, os arranca;

embora firmemente estabelecidos,

a vida deles não tem segurança.

23Ele poderá deixá-los descansar, sentindo-se seguros,

mas atento os vigia nos caminhos que seguem.

24Por um breve instante são exaltados e depois se vão,

colhidos como todos os demais,

ceifados como espigas de cereal.

25“Se não é assim, quem poderá provar que minto

e reduzir a nada as minhas palavras?”