Yobu 24 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 24:1-25

1“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze?

Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?

2Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo;

amadyetsa ziweto zimene aba.

3Amalanda abulu a ana amasiye

ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.

4Amachotsa mʼmisewu anthu osauka,

ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.

5Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu,

amayendayenda kufuna chakudya;

dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.

6Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake,

ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.

7Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala;

pa nthawi yozizira amasowa chofunda.

8Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri

ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.

9Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere;

ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.

10Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala;

amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.

11Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa;

amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.

12Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda,

anthu ovulala akulirira chithandizo.

Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.

13“Pali ena amene amakana kuwala,

amene safuna kuyenda mʼkuwalako

kapena kukhala mʼnjira zake.

14Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka

ndipo amakapha osauka ndi amphawi;

nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.

15Munthu wachigololo amadikira chisisira;

iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’

ndipo amaphimba nkhope yake.

16Mbala zimathyola nyumba usiku,

koma masana zimadzitsekera;

izo zimathawa kuwala.

17Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera.

Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.

18“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi;

minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo

kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.

19Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana

ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa.

20Mayi wowabereka amawayiwala,

mphutsi zimasangalala powadya;

anthu oyipa sakumbukiridwanso

koma amathyoka ngati mtengo.

21Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana,

ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.

22Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake;

ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.

23Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka,

koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.

24Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso;

amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse;

amadulidwa ngati ngala za tirigu.

25“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza

ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 24:1-25

1“全能者为何不定下审判的日期?

为何信靠祂的人要空等一场?

2恶人挪移界石,

抢夺羊群去牧养。

3他们牵走孤儿的驴,

强取寡妇的牛作抵押。

4他们把贫民赶离正路,

地上的穷人被迫东躲西藏。

5贫穷的人如荒漠中的野驴,

殷勤觅食,给儿女糊口。

6他们割田间的草料,

摘恶人剩余的葡萄。

7他们整夜赤身露体,

没有被子可以御寒。

8他们被山雨浇透,

只能在岩石下栖身。

9恶人夺去寡母怀中的孤儿,

强取穷人的孩子作抵押,

10使他们赤身露体地流浪,

饿着肚子扛禾捆。

11他们在恶人的橄榄林中榨油,

口干舌燥地在酒池踩踏。

12城中传来垂死之人的呻吟,

受伤者不断呼救,

上帝却置之不理。

13“有人与光明为敌,

不认识光明之道,

也不走光明之路。

14凶手黎明起来,

杀害贫苦的人,

夜晚又去做贼。

15奸夫的眼睛盼着黄昏,

心想,‘没人会看见我’,

并把脸蒙起来。

16盗贼夜间挖墙行窃,

日间躲藏起来,

不想认识光明。

17他们以昼作夜,

熟知黑夜的恐怖。

18“恶人如水上的泡沫。

他们的产业遭咒诅,

他们的葡萄园荒芜。

19阴间吞噬犯罪之人,

如同干热吞噬融雪。

20他们的生母忘记他们,

虫子在他们身上饱餐。

没有人再记得他们,

恶人像树木一样折断。

21他们恶待不育的妇人,

毫不善待寡妇。

22但上帝用大能掳走权贵,

他们再强大也难保性命。

23上帝让他们暂享安逸,

但他们逃不过祂的眼睛。

24他们一时得势,转瞬消逝;

他们沦为卑贱,像其他人一样灭亡,

像麦穗一样被割掉。

25我说的都是实情,谁能否认?

谁能证明我的话是空谈?”