Yobu 23 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

Nova Versão Internacional

Jó 23:1-17

1Então Jó respondeu:

2“Até agora me queixo com amargura;

a mão dele23.2 Conforme a Septuaginta e a Versão Siríaca. O Texto Massorético diz a mão sobre mim. é pesada, a despeito de meu gemido.

3Se tão somente eu soubesse

onde encontrá-lo e como ir à sua habitação!

4Eu lhe apresentaria a minha causa

e encheria a minha boca de argumentos.

5Estudaria o que ele me respondesse

e analisaria o que me dissesse.

6Será que ele se oporia a mim com grande poder?

Não, ele não me faria acusações.

7O homem íntegro poderia apresentar-lhe sua causa;

eu seria liberto para sempre de quem me julga.

8“Mas, se vou para o oriente, lá ele não está;

se vou para o ocidente, não o encontro.

9Quando ele está em ação no norte, não o enxergo;

quando vai para o sul, nem sombra dele eu vejo!

10Mas ele conhece o caminho por onde ando;

se me puser à prova, aparecerei como o ouro.

11Meus pés seguiram de perto as suas pegadas;

mantive-me no seu caminho sem desviar-me.

12Não me afastei dos mandamentos dos seus lábios;

dei mais valor às palavras de sua boca

do que ao meu pão de cada dia.

13“Mas ele é ele!

Quem poderá fazer-lhe oposição? Ele faz o que quer.

14Executa o seu decreto contra mim

e tem muitos outros planos semelhantes.

15Por isso fico apavorado diante dele;

pensar nisso me enche de medo.

16Deus fez desmaiar o meu coração;

o Todo-poderoso causou-me pavor.

17Contudo, não fui silenciado pelas trevas,

pelas densas trevas que cobrem o meu rosto.