Yobu 23 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

New International Version

Job 23:1-17

Job

1Then Job replied:

2“Even today my complaint is bitter;

his hand23:2 Septuagint and Syriac; Hebrew / the hand on me is heavy in spite of23:2 Or heavy on me in my groaning.

3If only I knew where to find him;

if only I could go to his dwelling!

4I would state my case before him

and fill my mouth with arguments.

5I would find out what he would answer me,

and consider what he would say to me.

6Would he vigorously oppose me?

No, he would not press charges against me.

7There the upright can establish their innocence before him,

and there I would be delivered forever from my judge.

8“But if I go to the east, he is not there;

if I go to the west, I do not find him.

9When he is at work in the north, I do not see him;

when he turns to the south, I catch no glimpse of him.

10But he knows the way that I take;

when he has tested me, I will come forth as gold.

11My feet have closely followed his steps;

I have kept to his way without turning aside.

12I have not departed from the commands of his lips;

I have treasured the words of his mouth more than my daily bread.

13“But he stands alone, and who can oppose him?

He does whatever he pleases.

14He carries out his decree against me,

and many such plans he still has in store.

15That is why I am terrified before him;

when I think of all this, I fear him.

16God has made my heart faint;

the Almighty has terrified me.

17Yet I am not silenced by the darkness,

by the thick darkness that covers my face.