Yobu 23 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 23:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri;

Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.

3Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu;

ndikanangopita kumene amakhalako!

4Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake

ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.

5Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha,

ndi kulingalira bwino zimene akananena!

6Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu?

Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.

7Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake,

ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.

8“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko,

ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.

9Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko

akapita kummwera, sindimuona.

10Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera;

Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.

11Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake;

ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.

12Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake;

ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.

13“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye?

Iye amachita chilichonse chimene wafuna.

14Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire,

ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.

15Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake;

ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.

16Mulungu walefula mtima wanga;

Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.

17Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima,

ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 23:1-17

约伯的回答

1约伯回答说:

2“我的哀诉至今充满苦楚,

祂的责罚使我呻吟不止。

3但愿我知道何处能寻见上帝,

知道怎样去祂的居所。

4我好在祂面前陈明案情,

滔滔不绝地为自己申辩;

5我好知道祂的答复,

看看祂对我说什么。

6祂会用大能与我争辩吗?

不会的,祂会垂听我的申诉,

7允许正直的人与祂理论,

审判者会让我永远脱罪。

8“然而,我去东边,祂不在那里;

我到西边,也找不到祂。

9祂在北边工作,我看不见祂;

祂转到南边,我也看不见祂。

10但祂知道我的一举一动,

我被祂试炼后必如纯金。

11我紧随祂的脚步,

持守祂的道,没有偏离。

12我没有违背祂的诫命,

我珍视祂的话语胜过我日用的饮食。

13祂独行其事,谁能阻挡祂?

祂按自己的意愿行事。

14祂在我身上的计划必然实现,

祂还有许多这样的计划。

15所以,我在祂面前惊恐不安。

我想起这事,便对祂充满恐惧。

16上帝使我心惊胆战,

全能者使我惊恐不安。

17然而,我不会因为置身黑暗,

被幽暗笼罩而缄默不言。