Yobu 22 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 22:1-30

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?

Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?

3Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?

Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?

4“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,

kuti azifuna kukukokera ku mlandu?

5Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?

Kodi machimo ako si opanda malire?

6Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;

umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.

7Sunawapatse madzi anthu otopa,

ndipo unawamana chakudya anthu anjala,

8ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,

munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.

9Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,

ndipo unapondereza ana amasiye.

10Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,

nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,

11nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,

nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.

12“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?

Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!

13Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?

Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?

14Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona

pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’

15Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale

imene anthu oyipa ankayendamo?

16Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,

maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.

17Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!

Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’

18Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,

choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.

19“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;

anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.

20Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka

ndipo moto wawononga chuma chawo!’

21“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;

ukatero udzaona zabwino.

22Landira malangizo a pakamwa pake

ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.

23Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;

ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,

24ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,

golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.

25Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,

siliva wako wamtengowapatali.

26Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse

ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.

27Udzamupempha ndipo adzakumvera,

ndipo udzapereka zimene unalonjeza.

28Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,

kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.

29Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’

Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.

30Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,

ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 22:1-30

以利法再次回答

1提幔以利法回答说:

2“人对上帝能有何益处?

即使智者对祂又有何益?

3全能者岂会因你为人公义而喜悦,

因你行为纯全而获利?

4祂岂会因你敬虔而惩罚你、审判你?

5你岂不是罪恶深重,

过犯无数?

6你无故强取弟兄的物品作抵押,

剥去贫寒者的衣服。

7你不给口渴的人水喝,

不给饥饿的人食物。

8土地归了权贵,

只让显要占有。

9你让寡妇空手而去,

你打断孤儿的臂膀。

10因此你周围布满网罗,

恐惧突然笼罩你。

11黑暗遮掩你的视线,

洪水淹没你。

12“上帝岂不在高天之上吗?

看,天上的星宿何其高远!

13你却说,‘上帝知道什么?

祂怎能隔着幽暗施行审判?

14当祂在穹苍巡弋时,

密云挡住祂的视线。’

15难道你要走恶人的古道,

步他们的后尘?

16他们死期未到便已夭逝,

他们的根基被洪涛卷走。

17他们对上帝说,‘离开我们吧!

全能者能把我们怎么样?’

18然而,是上帝把美物充满他们的家;

因此,我决不苟同他们的想法。

19义人看见他们的结局便欢喜,

无辜者见了便嘲笑,

20说,‘我们的仇敌果然被铲除,

他们的财产已被火吞噬。’

21“你要顺从上帝,与祂和好,

福乐就会临到你。

22你要接受祂的教诲,

把祂的话谨记在心。

23你若归向全能者,就必得到恢复。

你若将罪恶从帐篷中远远赶走,

24将金子扔进尘土,

俄斐的金子丢在布满石头的溪谷,

25全能者必成为你的金子,

成为你珍贵的银子。

26那时,你必从全能者那里找到欢乐,

你必抬头仰望上帝。

27你向祂祷告,祂必垂听,

你必向祂还所许的愿。

28你想做的事都会成功,

必有光照亮你的道路。

29人遭贬抑时,你说,‘使他们升高吧。’

上帝就会拯救他们,

30祂甚至会解救有罪之人,

他们必因你的手清洁而获救。”