Yobu 20 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 20:1-29

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe

chifukwa ndasautsidwa kwambiri.

3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,

ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,

kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,

5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,

chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.

6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba

ndipo mutu wake uli nengʼaa,

7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;

iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’

8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,

adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.

9Diso limene linamuona silidzamuonanso;

sadzapezekanso pamalo pake.

10Ana ake adzabwezera zonse

zimene iyeyo analanda anthu osauka;

11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake

zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake

ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,

13ngakhale salola kuzilavula,

ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,

14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;

chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.

15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;

Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.

16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo

ululu wa mphiri udzamupha.

17Sadzasangalala ndi timitsinje,

mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.

18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;

sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.

19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;

iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,

sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.

21Palibe chatsala kuti iye adye;

chuma chake sichidzachedwa kutha.

22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;

mavuto aakulu adzamugwera.

23Akadya nʼkukhuta,

Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto

ngati mvula yosalekeza.

24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,

muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.

25Muviwo adzawutulutsira ku msana,

songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.

Adzagwidwa ndi mantha aakulu;

26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.

Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza

ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.

27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;

dziko lapansi lidzamuwukira.

28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,

katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.

29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,

mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

La Bible du Semeur

Job 20:1-29

Deuxième discours de Tsophar

Le triomphe des méchants ne dure pas

1Tsophar de Naama prit la parole et dit :

2A présent, mes pensées ╵me pressent de répondre,

et mon agitation ╵ne peut se contenir.

3J’entends des remontrances ╵qui me sont une injure.

Mais mon esprit, ╵avec intelligence, ╵me donne la réponse.

4Ne le sais-tu donc pas : ╵depuis toujours,

depuis que l’homme ╵a été placé sur la terre,

5le triomphe des gens méchants ╵est de courte durée,

et la joie de l’impie ╵ne dure qu’un instant.

6Et quand bien même ╵il grandirait jusques au ciel,

quand de la tête ╵il toucherait les nues,

7il périra à tout jamais ╵tout comme son ordure20.7 L’ancienne version grecque a : sa grandeur, ce qui suppose une différence d’une consonne par rapport au texte hébreu traditionnel..

Et ceux qui le voyaient ╵diront : « Où donc est-il ? »

8Comme un songe, il s’évanouit, ╵on ne le trouve plus.

Comme un rêve nocturne, ╵il se dissipe.

9L’œil qui le contemplait ╵ne pourra plus le voir,

l’endroit qu’il habitait ╵ne l’apercevra plus.

10Ses fils devront indemniser ╵ceux qu’il a appauvris20.10 Autre traduction : ses fils seront assaillis par les pauvres.

et, de ses propres mains, ╵il restituera sa fortune.

11Ses os étaient remplis ╵d’une ardeur juvénile –

qui se couchera avec lui ╵dans la poussière.

12Si la méchanceté ╵est si douce à sa bouche,

et s’il l’abrite sous sa langue,

13s’il la savoure ╵sans jamais la lâcher,

s’il la retient encore ╵sous son palais,

14cet aliment se corrompra ╵en ses entrailles

et deviendra en lui ╵comme un venin d’aspic.

15Il a beau engloutir une fortune, ╵il devra la vomir :

Dieu la lui fera rendre.

16Il a sucé ╵un venin de serpent,

il sera mis à mort ╵par la langue de la vipère.

17Non, il ne verra plus ╵couler à flots

des fleuves, des torrents ╵de miel et de laitage ;

18il devra rendre ╵le fruit de son labeur, ╵et il ne l’avalera pas.

Tout ce qu’il s’est acquis ╵par ses affaires, ╵il n’en jouira pas.

19Puisqu’il a écrasé, ╵abandonné les pauvres,

et pillé des maisons ╵qu’il n’avait pas bâties,

20puisque son appétit ╵s’est montré insatiable,

il ne sauvera pas ╵ce qu’il a de plus cher.

21Personne n’échappait ╵à sa voracité,

c’est pourquoi son bonheur ╵ne subsistera pas.

22Au sein de l’abondance, ╵la détresse le frappera.

Tous les coups du malheur ╵viendront fondre sur lui.

23Quand il sera en train ╵de se remplir le ventre,

Dieu enverra sur lui ╵l’ardeur de sa colère,

elle pleuvra sur lui, ╵ce sera son repas.

24S’il échappe aux armes de fer,

un arc de bronze ╵viendra le transpercer20.24 Arc de bois renforcé par du bronze qui envoyait les flèches avec plus de force que les autres. La même pensée se retrouve en Es 24.18 ; Am 5.19. ;

25s’il arrache la flèche ╵et la sort de son corps,

s’il retire la pointe ╵qui a percé son foie,

les terreurs l’atteindront.

26L’obscurité totale ╵enveloppera ses trésors20.26 Autre traduction : enveloppera ses cachettes.,

un feu que nul n’attise ╵viendra le dévorer,

et consumera tout ╵ce qui reste dans sa demeure.

27Le ciel dévoilera sa faute

et, contre lui, la terre ╵se dressera.

28Au jour de la Colère,

tous les biens qu’il a amassés ╵dans sa maison ╵seront balayés, emportés.

29Tel est le sort que Dieu destine ╵à ceux qui font le mal, ╵voilà ce qu’il récoltera.

C’est ce que Dieu ╵a résolu pour lui20.29 voilà ce qu’il récoltera… pour lui: autre traduction : c’est là ce que Dieu lui fera récolter pour ses propos..