Yobu 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 18:1-21

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?

Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.

3Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe

ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?

4Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,

kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?

Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

5“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;

malawi a moto wake sakuwalanso.

6Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;

nyale ya pambali pake yazima.

7Mayendedwe ake amgugu azilala;

fundo zake zomwe zamugwetsa.

8Mapazi ake amulowetsa mu ukonde

ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.

9Msampha wamkola mwendo;

khwekhwe lamugwiritsitsa.

10Amutchera msampha pansi mobisika;

atchera diwa pa njira yake.

11Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,

zikutsatira mayendedwe ake onse.

12Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,

tsoka likumudikira.

13Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;

miyendo yake, manja ake, zonse zawola.

14Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,

ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.

15Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;

awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.

16Mizu yake ikuwuma pansi

ndipo nthambi zake zikufota

17Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;

sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.

18Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,

ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.

19Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,

kulibe wotsala kumene iye ankakhala.

20Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;

anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.

21Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;

amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

New Russian Translation

Иов 18:1-21

Вторая речь Билдада

Билдад ругает Иова за его речи

1Тогда ответил Билдад из Шуаха:

2– Когда ты положишь конец речам?

Подумай, потом будем говорить.

3Почему мы считаемся за скотов?

Почему в глазах твоих мы глупцы?

4О ты, кто в гневе себя терзает,

опустеть ли ради тебя земле?

Скалам ли с мест своих сдвинуться?

Наказание нечестивого Богом

5Истинно, свет у нечестивого погаснет,

даже искры не останется.

6Померкнет огонь у него в шатре,

и угаснет над ним светильник.

7Сократится мощь его шагов,

и падет он жертвой своих же замыслов.

8Ноги его сами шагнут в силки,

запутаются в сетях ловца.

9Поймает его за пяту петля,

крепко схватит его ловушка.

10Силки для него раскинуты по земле,

и ждет на пути западня.

11Страшат его ужасы отовсюду,

следуют за ним по пятам.

12Истощается сила его от голода,

и беда на страже, ждет, когда он споткнется.

13Съест его кожу болезнь18:13 Вероятный текст; в еврейском тексте: «Съест члены его кожи».,

съест первенец смерти члены его.

14Выволокут его из шатра, где он был в безопасности,

и приведут его к Царю ужасов18:14 Царь ужасов – олицетворение смерти..

15В шатре его поселится пламя;

горящая сера изольется на его жилище.

16Корни его засохнут внизу,

а ветви его наверху увянут.

17Память о нем исчезнет с земли,

и не будут о нем вспоминать на улицах.

18Изгонят его из света во мрак,

из мира живых прогонят.

19Ни детей, ни внуков

не останется после него в народе;

никого не останется после него

там, где он жил когда-то.

20На западе ужаснутся его судьбе,

и на востоке будут объяты страхом.

21Да, таков беззаконного дом,

место того, кто не знает Бога.