Yobu 18 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 18:1-21

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?

Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.

3Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe

ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?

4Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,

kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?

Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

5“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;

malawi a moto wake sakuwalanso.

6Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;

nyale ya pambali pake yazima.

7Mayendedwe ake amgugu azilala;

fundo zake zomwe zamugwetsa.

8Mapazi ake amulowetsa mu ukonde

ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.

9Msampha wamkola mwendo;

khwekhwe lamugwiritsitsa.

10Amutchera msampha pansi mobisika;

atchera diwa pa njira yake.

11Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,

zikutsatira mayendedwe ake onse.

12Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,

tsoka likumudikira.

13Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;

miyendo yake, manja ake, zonse zawola.

14Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,

ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.

15Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;

awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.

16Mizu yake ikuwuma pansi

ndipo nthambi zake zikufota

17Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;

sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.

18Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,

ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.

19Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,

kulibe wotsala kumene iye ankakhala.

20Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;

anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.

21Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;

amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

New International Version

Job 18:1-21

Bildad

1Then Bildad the Shuhite replied:

2“When will you end these speeches?

Be sensible, and then we can talk.

3Why are we regarded as cattle

and considered stupid in your sight?

4You who tear yourself to pieces in your anger,

is the earth to be abandoned for your sake?

Or must the rocks be moved from their place?

5“The lamp of a wicked man is snuffed out;

the flame of his fire stops burning.

6The light in his tent becomes dark;

the lamp beside him goes out.

7The vigor of his step is weakened;

his own schemes throw him down.

8His feet thrust him into a net;

he wanders into its mesh.

9A trap seizes him by the heel;

a snare holds him fast.

10A noose is hidden for him on the ground;

a trap lies in his path.

11Terrors startle him on every side

and dog his every step.

12Calamity is hungry for him;

disaster is ready for him when he falls.

13It eats away parts of his skin;

death’s firstborn devours his limbs.

14He is torn from the security of his tent

and marched off to the king of terrors.

15Fire resides18:15 Or Nothing he had remains in his tent;

burning sulfur is scattered over his dwelling.

16His roots dry up below

and his branches wither above.

17The memory of him perishes from the earth;

he has no name in the land.

18He is driven from light into the realm of darkness

and is banished from the world.

19He has no offspring or descendants among his people,

no survivor where once he lived.

20People of the west are appalled at his fate;

those of the east are seized with horror.

21Surely such is the dwelling of an evil man;

such is the place of one who does not know God.”