Yobu 18 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 18:1-21

Mawu a Bilidadi

1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,

2“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?

Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.

3Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe

ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?

4Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,

kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo?

Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?

5“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;

malawi a moto wake sakuwalanso.

6Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;

nyale ya pambali pake yazima.

7Mayendedwe ake amgugu azilala;

fundo zake zomwe zamugwetsa.

8Mapazi ake amulowetsa mu ukonde

ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.

9Msampha wamkola mwendo;

khwekhwe lamugwiritsitsa.

10Amutchera msampha pansi mobisika;

atchera diwa pa njira yake.

11Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,

zikutsatira mayendedwe ake onse.

12Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,

tsoka likumudikira.

13Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;

miyendo yake, manja ake, zonse zawola.

14Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,

ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.

15Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;

awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.

16Mizu yake ikuwuma pansi

ndipo nthambi zake zikufota

17Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;

sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.

18Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,

ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.

19Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,

kulibe wotsala kumene iye ankakhala.

20Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;

anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.

21Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;

amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 18:1-21

比勒达发言

1书亚比勒达回答说:

2“你要狡辩到何时呢?

你先想清楚,然后我们再谈。

3为何你把我们当作牲畜,

把我们视为蠢货?

4你这气得要撕碎自己的人,

大地会因你而荒凉吗?

磐石会因你而挪移吗?

5“恶人的光必熄灭。

他的火焰不再闪耀。

6他帐篷中一片黑暗,

他上面的灯光熄灭。

7恶人强劲的步伐变得蹒跚,

他必被自己的阴谋所害。

8他自陷网罗,

步入圈套。

9套索缠住他的脚跟,

网罗紧紧地罩住他。

10土里埋着绊他的绳索,

路上有陷阱等待着他。

11恐惧四面笼罩着他,

步步紧追着他。

12他饿得气力衰竭,

灾祸随时临到他。

13疾病侵蚀他的皮肉,

死亡吞噬他的肢体。

14他被拖出安稳的帐篷,

被押到冥王18:14 冥王”希伯来文是“恐怖之王”。那里。

15他的帐篷燃烧着烈焰,

他的居所撒满了硫磺。

16他下面的根茎枯干,

上面的枝子枯萎。

17他从世上销声匿迹,

无人记得他的名字。

18他从光明中被赶入黑暗,

他被逐出这个世界。

19他在本族中无子无孙,

他所居之地无人生还。

20他的下场令西方的人震惊,

令东方的人战栗。

21这就是不义之人的结局,

不认识上帝之人的下场。”