Yobu 16 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 16:1-22

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi;

nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.

3Kodi mawu anu ochulukawo adzatha?

Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?

4Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu,

inuyo mukanakhala monga ndilili inemu;

Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu

ndi kukupukusirani mutu wanga.

5Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani;

chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.

6“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa;

ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.

7Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu;

mwawononga banja langa lonse.

8Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni;

kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.

9Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane,

amachita kulumira mano;

mdani wanga amandituzulira maso.

10Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza;

amandimenya pa tsaya mwachipongwe

ndipo amagwirizana polimbana nane.

11Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa

ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.

12Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya;

anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya.

Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;

13anthu ake oponya mauta andizungulira.

Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga

ndipo akutayira pansi ndulu yanga.

14Akundivulaza kawirikawiri,

akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.

15“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa

ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.

16Maso anga afiira ndi kulira,

ndipo zikope zanga zatupa;

17komatu manja anga sanachite zachiwawa

ndipo pemphero langa ndi lolungama.

18“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga;

kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!

19Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba;

wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.

20Wondipembedzera ndi bwenzi langa,

pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;

21iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu

monga munthu amadandaulira bwenzi lake.

22“Pakuti sipapita zaka zambiri

ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 16:1-22

约伯的回答

1约伯回答说:

2“这些话,我听过很多,

你们安慰人,反让人愁烦。

3你们的空谈无休无止吗?

是什么惹你们说个不停?

4倘若你我易地而处,

我也能说你们那样的话,

滔滔不绝地攻击你们,

向你们摇头。

5我会对你们讲鼓励的话,

用劝慰之言减轻你们的痛苦。

6“我若申辩,痛苦不减;

我若缄默,痛苦犹在。

7上帝啊,你使我精疲力竭,

家破人亡,

8你榨干了我,

使我骨瘦如柴,

这成了我的罪证。

9上帝在愤怒中撕裂我,迫害我,

向我咬牙切齿;

仇敌恶狠狠地盯着我。

10他们嘲笑我,

轻蔑地掴我的脸,

联合起来攻击我。

11上帝把我交给罪人,

把我扔到恶人手中。

12我本来平顺,祂击垮了我,

祂抓住我的颈项将我摔碎,

把我当祂的箭靶。

13祂的弓箭手四面围住我,

祂毫不留情地刺透我的肾脏,

使我肝胆涂地。

14祂一次次地击伤我,

像勇士一样扑向我。

15我缝制麻衣,披在身上,

把我的荣耀埋在尘土中。

16我哭得脸颊红肿,

眼皮发黑。

17但我未行残暴之事,

我的祷告纯真。

18“大地啊!不要掩盖我的血,

不要拦阻我的呼求。

19此时,我的见证人在天上,

我的辩护者在高天上。

20我的朋友讥笑我,

我在上帝面前流泪。

21但愿人与上帝之间有仲裁者,

如同人与人之间。

22因为我的年日不多,

我快要踏上不归路。