Yobu 15 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 15:1-35

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,

kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?

3Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,

kapena kuyankhula mawu opanda phindu?

4Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu

ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.

5Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;

ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.

6Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;

milomo yakoyo ikukutsutsa.

7“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?

Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?

8Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?

Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?

9Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?

Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?

10Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,

anthu amvulazakale kupambana abambo ako.

11Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,

mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?

12Chifukwa chiyani ukupsa mtima,

ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,

13moti ukupsera mtima Mulungu

ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?

14“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima

kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?

15Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,

ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,

16nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,

amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.

17“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;

ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,

18zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,

sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.

19(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa

pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).

20Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,

munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.

21Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,

pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.

22Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;

iyeyo ndi woyenera kuphedwa.

23Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;

amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.

24Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;

zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,

25chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu

ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.

26Amapita mwa mwano kukalimbana naye

atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.

27“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa

ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,

28munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka

ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu,

nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.

29Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,

ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.

30Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;

lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake,

ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.

31Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,

pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.

32Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,

ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.

33Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,

adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.

34Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala

ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.

35Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;

mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

Het Boek

Job 15:1-35

Het antwoord van Elifaz

1Op deze uitspraken antwoordde Elifaz:

2‘Je wordt beschouwd als een wijs man, maar je spreekt alleen maar nietszeggende woorden. Je bent gewoon een druktemaker!

3Het is niet goed zo te spreken, zulke woorden hebben geen enkele waarde.

4-5 Je vertekent de ware toewijding aan God en hebt geen ontzag voor Hem. Jouw zonden vertellen je mond wat hij moet zeggen. Je spreekt met de tong van een listig man.

6Daardoor veroordeel jij jezelf en niet ik, de woorden die je spreekt, getuigen tegen je.

7-8 Ben jij soms de eerste mens, werd jij geboren voordat de heuvels werden geschapen? Ken je de verborgen beslissingen van God? Heb jij soms de wijsheid in pacht?

9Weet je meer dan wij? Begrijp je meer dan wij kunnen begrijpen?

10Aan onze kant staan wijze bejaarde mannen die zelfs ouder zijn dan je vader.

11Is Gods troost niet genoeg voor jou? Zijn zijn woorden niet vriendelijk tegen jou gesproken?

12Waarom laat je je meeslepen door je zondige hart en vlammen je ogen zo?

13Je keert je tegen God en beschuldigt Hem in het wilde weg!

14Welk mens op aarde kan zo rein en rechtvaardig zijn als jij zegt?

15Als God zelfs de engelen niet volledig vertrouwt en zelfs de hemelen in zijn ogen niet volkomen rein zijn,

16waar blijft de mens dan met zijn verdorvenheid en zondigheid? De mens, die de zonde drinkt of het water is.

17-19Luister, ik zal je verklaren wat ik heb gezien en wat bevestigd wordt door de ervaringen van wijze mannen, die dit kregen overgeleverd van hun vaders (onze voorouders, die als enigen het land kregen toegewezen):

20een goddeloos mens heeft zijn hele leven met moeilijkheden te kampen. De geweldpleger heeft slechts enkele jaren de tijd.

21Hij wordt geplaagd door angstaanjagende geruchten en wanneer hij eindelijk rust heeft gevonden, wordt hij aangevallen door rovers.

22Hij gelooft niet dat hij nog ooit de duisternis kan ontvluchten en leeft voortdurend met de angst dat hij wordt vermoord.

23-24 Hij dwaalt rond, bedelend om voedsel. Zijn leven wordt beheerst door voortdurende angst, spanningen en vertwijfeling. Zijn vijanden overwinnen hem als een koning die klaarstaat voor de strijd.

25-26 Gewapend met zijn zwaarbeslagen schild balt hij zijn vuist tegen God. Hij daagt de Almachtige uit en valt Hem koppig aan.

27-28 Hoewel deze mens er vet en opgeblazen uitziet, zal hij in verwoeste steden moeten wonen, in verlaten huizen die tot puin zijn vervallen.

29Hij zal niet rijk blijven en er niet in slagen zijn bezittingen uit te breiden.

30Nee, hij zal voor altijd in duisternis leven en de adem van God zal hem vernietigen, de vlammen zullen alles wat hij heeft, verteren.

31Laat hij niet langer vertrouwen op zinloze bezigheden en zichzelf niet meer voor de gek houden, want zinloosheid zal zijn enige beloning zijn.

32Vroeger dan hij denkt, zal dit werkelijkheid worden. Spoedig zal de volle nutteloosheid ervan tot hem doordringen. Want alles waarop hij vertrouwde, zal vergaan.

33Hij zal lijken op een onvruchtbare wijnstok en op een olijfboom zonder bloesem.

34Want de plannen van de goddelozen zijn onvruchtbaar, Gods vuur verteert de huizen van de omkopers.

35Het enige dat zij ter wereld brengen, is zonde en hun innerlijk brengt alleen bedrog voort.’