Yobu 13 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 13:1-28

1“Ndaziona ndi maso anga zonsezi,

ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.

2Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

3Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse

ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.

4Koma inu mukundipaka mabodza;

nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!

5Achikhala munangokhala chete nonsenu!

Apo mukanachita zanzeru.

6Tsopano imvani kudzikanira kwanga;

imvani kudandaula kwa pakamwa panga.

7Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu?

Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?

8Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera?

Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?

9Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa?

Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?

10Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani

ngati muchita zokondera mseri.

11Kodi ulemerero wake sungakuopseni?

Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?

12Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo;

mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.

13“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule;

tsono zimene zindichitikire zichitike.

14Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe

ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?

15Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira;

ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.

16Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa

pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!

17Mvetserani mosamala mawu anga;

makutu anu amve zimene ndikunena.

18Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga,

ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.

19Kodi alipo wina amene angatsutsane nane?

ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.

20“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi,

ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:

21Muchotse dzanja lanu pa ine,

ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.

22Tsono muyitane ndipo ndidzayankha,

kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.

23Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati?

Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.

24Chifukwa chiyani mukundifulatira

ndi kundiyesa ine mdani wanu?

25Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo?

Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?

26Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo

ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.

27Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo.

Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse

poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.

28“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa,

ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

Nova Versão Internacional

Jó 13:1-28

1“Meus olhos viram tudo isso,

meus ouvidos o ouviram e entenderam.

2O que vocês sabem, eu também sei;

não sou inferior a vocês.

3Mas desejo falar ao Todo-poderoso

e defender a minha causa diante de Deus.

4Vocês, porém, me difamam com mentiras;

todos vocês são médicos que de nada valem!

5Se tão somente ficassem calados,

mostrariam sabedoria.

6Escutem agora o meu argumento;

prestem atenção à réplica de meus lábios.

7Vocês vão falar com maldade em nome de Deus?

Vão falar enganosamente a favor dele?

8Vão revelar parcialidade por ele?

Vão defender a causa a favor de Deus?

9Tudo iria bem se ele os examinasse?

Vocês conseguiriam enganá-lo

como podem enganar os homens?

10Com certeza ele os repreenderia

se, no íntimo, vocês fossem parciais.

11O esplendor dele não os aterrorizaria?

O pavor dele não cairia sobre vocês?

12As máximas que vocês citam são provérbios de cinza;

suas defesas não passam de barro.

13“Aquietem-se e deixem-me falar,

e aconteça comigo o que acontecer.

14Por que me ponho em perigo

e tomo a minha vida em minhas mãos?

15Embora ele me mate, ainda assim esperarei nele;

certo é que defenderei13.15 Ou Certamente ele me matará; não tenho esperança; ainda assim defenderei os meus caminhos diante dele.

16Aliás, será essa a minha libertação,

pois nenhum ímpio ousaria apresentar-se a ele!

17Escutem atentamente as minhas palavras;

que os seus ouvidos acolham o que eu digo.

18Agora que preparei a minha defesa,

sei que serei justificado.

19Haverá quem me acuse?

Se houver, ficarei calado e morrerei.

20“Concede-me só estas duas coisas, ó Deus,

e não me esconderei de ti:

21Afasta de mim a tua mão

e não mais me assustes com os teus terrores.

22Chama-me, e eu responderei,

ou deixa-me falar, e tu responderás.

23Quantos erros e pecados cometi?

Mostra-me a minha falta e o meu pecado.

24Por que escondes o teu rosto

e me consideras teu inimigo?

25Atormentarás uma folha levada pelo vento?

Perseguirás a palha?

26Pois fazes constar contra mim coisas amargas

e me fazes herdar os pecados da minha juventude.

27Acorrentas os meus pés

e vigias todos os meus caminhos,

pondo limites aos meus passos.

28“Assim o homem se consome como coisa podre,

como a roupa que a traça vai roendo.