Yobu 13 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 13:1-28

1“Ndaziona ndi maso anga zonsezi,

ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.

2Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

3Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse

ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.

4Koma inu mukundipaka mabodza;

nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!

5Achikhala munangokhala chete nonsenu!

Apo mukanachita zanzeru.

6Tsopano imvani kudzikanira kwanga;

imvani kudandaula kwa pakamwa panga.

7Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu?

Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?

8Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera?

Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?

9Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa?

Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?

10Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani

ngati muchita zokondera mseri.

11Kodi ulemerero wake sungakuopseni?

Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?

12Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo;

mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.

13“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule;

tsono zimene zindichitikire zichitike.

14Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe

ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?

15Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira;

ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.

16Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa

pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!

17Mvetserani mosamala mawu anga;

makutu anu amve zimene ndikunena.

18Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga,

ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.

19Kodi alipo wina amene angatsutsane nane?

ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.

20“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi,

ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:

21Muchotse dzanja lanu pa ine,

ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.

22Tsono muyitane ndipo ndidzayankha,

kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.

23Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati?

Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.

24Chifukwa chiyani mukundifulatira

ndi kundiyesa ine mdani wanu?

25Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo?

Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?

26Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo

ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.

27Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo.

Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse

poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.

28“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa,

ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

Luganda Contemporary Bible

Yobu 13:1-28

1“Laba, eriiso lyange lyalaba ebyo byonna,

n’okutu kwange ne kuwulira ne mbitegeera.

213:2 Yob 12:3Kye mumanyi nange kye mmanyi;

siri wa wansi ku mmwe.

313:3 Yob 23:3-4Naye neegomba okwogera n’oyo Ayinzabyonna,

era n’okuleeta ensonga zange mu maaso ga Katonda.

413:4 Zab 119:69; Yer 23:32Naye mmwe mumpayiriza;

muli basawo abatagasa mmwe mwenna!

513:5 Nge 17:28Kale singa musirika!

Olwo lwe mwandibadde n’amagezi.

6Muwulire kaakano endowooza yange,

muwulirize okwegayirira kw’emimwa gyange.

713:7 Yob 36:4Katonda munaamwogerera nga mwogera ebitali bya butuukirivu?

Munaamwogerera eby’obulimba?

813:8 Lv 19:15Munaamulaga ng’ataliiko luuyi,

munaamuwoleza ensonga ze.

913:9 Yob 12:16; Bag 6:7Singa akukebera, anaakusanga oli bulungi?

Oyinza okumulimba nga bw’oyinza okulimba abantu?

10Tayinza butakunenya,

singa osaliriza mu bubba.

1113:11 Yob 31:23Ekitiibwa kye ekisukiridde tekyandikutiisizza?

Entiisa ye teyandikuguddeko?

12Ebigambo byammwe ebijjukirwa ngero za vvu,

n’okwewolereza kwammwe kwa bbumba.

13Musirike nze njogere;

kyonna ekinantukako kale kintuukeko.

14Lwaki neeteeka mu mitawaana,

obulamu bwange ne mbutwalira mu mikono gyange?

1513:15 a Yob 7:6 b Zab 23:4; Nge 14:32 c Yob 27:5Ne bw’anzita, mu ye mwe nnina essuubi,

ddala ddala nditwala ensonga zange mu maaso ge.

1613:16 Is 12:1Ddala kino kinaavaamu okusumululwa kwange,

kubanga teri muntu atatya Katonda ayinza kwetantala kujja mu maaso ge!

1713:17 Yob 21:2Muwulirize ebigambo byange n’obwegendereza;

amatu gammwe gawulire bye ŋŋamba.

1813:18 Yob 23:4Kaakano nga bwe ntegese empoza yange,

mmanyi nti nzija kwejeerera.

1913:19 a Yob 40:4; Is 50:8 b Yob 10:8Waliwo ayinza okuleeta emisango gye nvunaanibwa?

Bwe kiba bwe kityo, nzija kusirika nfe.

20Ebintu ebyo ebibiri byokka by’oba ompa, Ayi Katonda,

awo sijja kukwekweka.

2113:21 Zab 39:10Nzigyako omukono gwo,

olekere awo okuntiisatiisa n’okunkangakanga.

2213:22 a Yob 14:15 b Yob 9:16Kale nno ompite nzija kukuddamu,

oba leka njogere ggwe onziremu.

2313:23 1Sa 26:18Nsobi meka era bibi bimeka bye nkoze?

Ndaga ekibi kyange era n’omusango gwange.

2413:24 a Ma 32:20; Zab 13:1; Is 8:17 b Yob 19:11; Kgb 2:5Lwaki okweka amaaso go,

n’onfuula omulabe wo?

2513:25 a Lv 26:36 b Yob 21:18; Is 42:3Onoobonyaabonya ekikoola ekifuuyiddwa omuyaga?

Onooyigga ebisasiro ebikaze?

2613:26 Zab 25:7Kubanga ompadiikako ebintu ebiruma,

n’ondeetera okuddamu okwetikka ebibi byange eby’omu buvubuka.

2713:27 Yob 33:11Oteeka ebigere byange mu nvuba,

era okuuma butiribiri amakubo gange mwe mpita

ng’oteeka obubonero ku bisinziiro by’ebigere byange.

2813:28 Is 50:9; Yak 5:2Bw’atyo omuntu bw’aggwaawo ng’ekintu ekivundu,

ng’olugoye oluliiriddwa ennyenje.”