Yobu 13 – CCL & KSS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 13:1-28

1“Ndaziona ndi maso anga zonsezi,

ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.

2Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

3Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse

ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.

4Koma inu mukundipaka mabodza;

nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!

5Achikhala munangokhala chete nonsenu!

Apo mukanachita zanzeru.

6Tsopano imvani kudzikanira kwanga;

imvani kudandaula kwa pakamwa panga.

7Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu?

Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?

8Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera?

Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?

9Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa?

Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?

10Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani

ngati muchita zokondera mseri.

11Kodi ulemerero wake sungakuopseni?

Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?

12Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo;

mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.

13“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule;

tsono zimene zindichitikire zichitike.

14Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe

ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?

15Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira;

ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.

16Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa

pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!

17Mvetserani mosamala mawu anga;

makutu anu amve zimene ndikunena.

18Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga,

ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.

19Kodi alipo wina amene angatsutsane nane?

ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.

20“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi,

ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:

21Muchotse dzanja lanu pa ine,

ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.

22Tsono muyitane ndipo ndidzayankha,

kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.

23Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati?

Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.

24Chifukwa chiyani mukundifulatira

ndi kundiyesa ine mdani wanu?

25Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo?

Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?

26Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo

ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.

27Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo.

Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse

poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.

28“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa,

ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

Kurdi Sorani Standard

ئەیوب 13:1-28

1«چاوەکانم هەموو ئەمانەی بینیوە،

گوێیەکانم بیستوویانە و تێیان گەیشتووم.

2وەک زانینی ئێوە منیش زانیومە؛

من لە ئێوە کەمتر نیم.

3بەڵام من لەگەڵ توانادارەکە قسە دەکەم،

دەمەوێت لەلای خودا دادگایی بکرێم.

4بەڵام ئێوە درۆم بۆ هەڵدەبەستن،

هەمووتان پزیشکی بێ کەڵکن.

5خۆزگە بە تەواوی بێدەنگ دەبوون!

ئەوە بۆتان دەبوو بە دانایی.

6ئێستا گوێ لە بەهانەم بگرن و

بۆ سکاڵای لێوەکانم گوێ شل بکەن.

7ئایا بە درۆ بەرگری لە خودا دەکەن؟

ئایا بە دەم خوداوە درۆ دەکەن؟

8ئایا لایەنگری دەکەن،

یان بۆ خودا مشتومڕ دەکەن؟

9ئەگەر تاقیتان بکاتەوە، ئایا دەردەچن

یان دەتانەوێت وەک مرۆڤ هەڵیبخەڵەتێنن؟

10بێگومان سەرزەنشتتان دەکات

ئەگەر بە نهێنی لایەنگری بکەن.

11ئایا شکۆمەندییەکەی ناتانترسێنێت و

ترسی ئەو دەستتان بەسەردا ناکێشێت؟

12یادەوەری و پەندەکانتان تەنها خۆڵەمێشە و

بەرگرییەکانتان بەرگرییە لە قوڕ.

13«لێم بێدەنگ بن، من قسە دەکەم و

ئەوەی بەسەرم دێت با بێت!

14بۆچی من کێشە بۆ خۆم دروستبکەم،

ژیانی خۆم بخەمە مەترسییەوە؟

15ئەگەر بشمکوژێت هەر پشتی پێ دەبەستم،

لەبەردەمیدا تەنها مشتومڕ لەسەر هەڵسوکەوتم دەکەم.

16هەروەها ئەمە بۆ ڕزگاریمە،

کە خوانەناس نایەتە بەردەمی.

17بە تەواوی گوێ لە قسەکانم بگرن و

ئەوەی ڕایدەگەیەنم با گوێتان لێی بێت.

18ئەوەتا من بە باشی سکاڵای خۆمم خستووەتە ڕوو،

دەزانم ئەستۆپاک دەردەچم.

19کێیە ئەوەی مشتومڕم لەگەڵ دەکات،

تاکو هەر ئێستا بێدەنگ بم و ڕۆح بەدەستەوە بدەم؟

20«ئەی خودا، تەنها بەم دوو کارە پشتگیریم بکە،

ئیتر لەبەردەمت ون نابم.

21دەستت لێم دووربخەوە و

با سامی تۆ نەمترسێنێت.

22ئینجا بانگم بکە و من وەڵام دەدەمەوە،

یان من قسە دەکەم و تۆ وەڵامم بدەوە.

23چەند تاوان و گوناهم هەیە؟

یاخیبوون و گوناهەکەی خۆمم پێ بناسێنە.

24بۆچی ڕووی خۆت دەشاریتەوە و

بە دوژمنی خۆت دامدەنێیت؟

25ئایا گەڵایەکی هەڵوەریو پان دەکەیتەوە؟

ئایا بەدوای پووشی وشکدا ڕادەکەیت؟

26تۆ بە تاڵی لە دژم دەنووسیت و

لەسەر تاوانەکانی لاویێتیم سزام دەدەیت.

27جا پێیەکانی منت خستووەتە ناو کۆتەوە و

چاوت بڕیوەتە هەموو ڕێڕەوەکانم و

شوێن پێیەکانم دەپشکنیت.

28«وەک دارێکی کلۆر لەناو دەچم،

وەک جلێک کە مۆرانە لێی دابێت.