Yobu 13 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 13:1-28

1“Ndaziona ndi maso anga zonsezi,

ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.

2Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

3Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse

ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.

4Koma inu mukundipaka mabodza;

nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!

5Achikhala munangokhala chete nonsenu!

Apo mukanachita zanzeru.

6Tsopano imvani kudzikanira kwanga;

imvani kudandaula kwa pakamwa panga.

7Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu?

Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?

8Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera?

Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?

9Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa?

Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?

10Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani

ngati muchita zokondera mseri.

11Kodi ulemerero wake sungakuopseni?

Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?

12Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo;

mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.

13“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule;

tsono zimene zindichitikire zichitike.

14Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe

ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?

15Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira;

ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.

16Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa

pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!

17Mvetserani mosamala mawu anga;

makutu anu amve zimene ndikunena.

18Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga,

ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.

19Kodi alipo wina amene angatsutsane nane?

ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.

20“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi,

ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:

21Muchotse dzanja lanu pa ine,

ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.

22Tsono muyitane ndipo ndidzayankha,

kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.

23Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati?

Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.

24Chifukwa chiyani mukundifulatira

ndi kundiyesa ine mdani wanu?

25Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo?

Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?

26Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo

ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.

27Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo.

Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse

poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.

28“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa,

ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 13:1-28

1“这一切,我亲眼见过,

亲耳听过,且已明白。

2你们知道的我也知道,

我不比你们逊色。

3我想和全能者对话,

我渴望跟上帝理论。

4而你们只会编造谎言,

都是无用的庸医。

5但愿你们闭口不言,

那样还算你们明智。

6请听我的申辩,

留心听我的争讼。

7你们要为上帝说谎,

为祂说诡诈的话吗?

8你们要偏袒上帝吗?

你们要替祂辩护吗?

9祂查问你们时岂会有好结果?

你们岂能像欺骗人一样欺骗祂?

10你们若暗中偏袒,

祂必责备你们。

11难道你们不怕祂的威严,

不对祂充满恐惧吗?

12你们的名言是无用的灰尘,

你们的雄辩是土筑的营垒。

13“你们住口,让我发言;

我愿承担一切后果。

14我已经豁出性命,

不惜冒生命危险。

15祂必杀我,我毫无指望,13:15 祂必杀我,我毫无指望”或译“即使祂杀我,我也信靠祂”。

但我仍要在祂面前申辩。

16这样我才能得救,

因为不信上帝的人无法到祂面前。

17请留心听我说话,

侧耳听我发言。

18看啊,我已准备好辩词,

我知道自己有理。

19若有人能指控我,

我就缄默,情愿死去。

20上帝啊,只要你应允两件事,

我就不躲避你的面,

21求你把手从我身上挪开,

不要用你的威严惊吓我。

22这样,你传唤我,我必回应;

或者让我陈述,你来回答。

23我究竟有什么过错和罪恶?

求你指出我的过犯和罪愆。

24你为何掩面不看我?

为何把我当作仇敌?

25你要恐吓一片风中的落叶吗?

你要追赶一根枯干的茅草吗?

26你记下指控我的罪状,

让我承担幼年的罪恶。

27你给我上了脚镣,

监视我的一举一动,

为我的脚掌设界限。

28我消逝如朽烂之物,

又如虫蛀的衣服。