Yobu 12 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 12:1-25

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Ndithudi inuyo ndinu anthu

ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!

3Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu;

ineyo sindine munthu wamba kwa inu.

Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?

4“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga,

ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha.

Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!

5Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka.

Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.

6Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere,

ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino,

amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.

7“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa,

kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;

8kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa,

kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.

9Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa

kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?

10Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse,

ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.

11Kodi khutu sindiye limene limamva mawu

monga mmene lilime limalawira chakudya?

12Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba?

Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?

13“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu;

uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.

14Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso.

Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.

15Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma;

akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.

16Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana;

munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.

17Iye amalanda aphungu nzeru zawo

ndipo amapusitsa oweruza.

18Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo

ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.

19Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo

ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.

20Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika

ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.

21Iye amanyoza anthu otchuka

ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.

22Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima

ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.

23Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso;

amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.

24Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi;

amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.

25Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira;

Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

New International Reader’s Version

Job 12:1-25

Job’s Reply

1Job replied,

2“You people think you are the only ones who matter!

You are sure that wisdom will die with you!

3But I have a brain, just like you.

I’m as clever as you are.

In fact, everyone knows as much as you do.

4“My friends laugh at me all the time,

even though I called out to God and he answered.

My friends laugh at me,

even though I’m honest and right.

5People who have an easy life look down on those who have problems.

They think trouble comes only to those whose feet are slipping.

6Why doesn’t anyone bother the tents of robbers?

Why do those who make God angry remain secure?

They are in God’s hands!

7“But ask the animals what God does.

They will teach you.

Or ask the birds in the sky.

They will tell you.

8Or speak to the earth. It will teach you.

Or let the fish in the ocean educate you.

9Are there any of these creatures that don’t know

what the powerful hand of the Lord has done?

10He holds the life of every creature in his hand.

He controls the breath of every human being.

11Our tongues tell us what tastes good and what doesn’t.

And our ears tell us what’s true and what isn’t.

12Old people are wise.

Those who live a long time have understanding.

13“Wisdom and power belong to God.

Advice and understanding also belong to him.

14What he tears down can’t be rebuilt.

The people he puts in prison can’t be set free.

15If he holds back the water, everything dries up.

If he lets the water loose, it floods the land.

16Strength and understanding belong to him.

Those who tell lies and those who believe them also belong to him.

17He removes the wisdom of rulers and leads them away.

He makes judges look foolish.

18He sets people free from the chains that kings put on them.

Then he dresses the kings in the clothes of slaves.

19He removes the authority of priests and leads them away.

He removes from their positions

officials who have been in control for a long time.

20He shuts the mouths of trusted advisers.

He takes away the understanding of elders.

21He looks down on proud leaders.

He takes away the strength of those who are mighty.

22He tells people the secrets of darkness.

He brings total darkness out into the light.

23He makes nations great, and then he destroys them.

He makes nations grow, and then he scatters them.

24He takes away the understanding of the leaders of the earth.

He makes them wander in a desert where no one lives.

25Without any light, they feel their way along in darkness.

God makes them unsteady like those who get drunk.