Yobu 11 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 11:1-20

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,

2“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa?

Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?

3Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku?

Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?

4Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika

ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’

5Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula

kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe

6ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake,

pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri.

Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.

7“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu?

Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?

8Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani?

Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani?

9Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi

ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.

10“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende

nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?

11Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo;

akaona choyipa, kodi sachizindikira?

12Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru

monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.

13“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye

ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,

14ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako

ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,

15udzatukula mutu wako wosachita manyazi;

udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.

16Udzayiwala ndithu zowawa zako,

zidzakhala ngati madzi amene apita kale.

17Moyo wako udzawala kupambana usana,

ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.

18Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo;

ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.

19Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza

ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.

20Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza,

ndipo adzasowa njira yothawirapo;

chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

Nueva Versión Internacional

Job 11:1-20

Primer discurso de Zofar

1A esto respondió Zofar de Namat:

2«¿Quedará sin respuesta toda esta palabrería?

¿Resultará inocente este hablador?

3¿Todo ese discurso nos dejará callados?

¿Te burlarás sin que nadie te reprenda?

4Tú afirmas: “Mi postura es la correcta;

soy puro a los ojos de Dios”.

5¡Cómo me gustaría que Dios interviniera

y abriera sus labios contra ti

6para mostrarte los secretos de la sabiduría,

pues esta tiene dos lados!11:6 esta tiene dos lados. Frase de difícil traducción.

Sabrías entonces que buena parte de tu pecado

Dios no lo ha tomado en cuenta.

7»¿Puedes adentrarte en los misterios de Dios

o alcanzar la perfección11:7 alcanzar la perfección. Alt. llegar hasta los límites. del Todopoderoso?

8Son más altos que los cielos;

¿qué puedes hacer?

Son más profundos que el abismo;11:8 abismo. Lit. Seol.

¿qué puedes saber?

9Son más extensos que toda la tierra;

¡son más anchos que todo el mar!

10»Si viene y te pone en un calabozo,

y luego te llama a cuentas,

¿quién lo hará desistir?

11Bien conoce Dios a la gente sin escrúpulos;

cuando percibe el mal, no lo pasa por alto.

12¡El necio llegará a ser sabio

cuando de un asno salvaje nazca un hombre!11:12 cuando … hombre. Alt. cuando los asnos salvajes nazcan domesticados.

13»Pero si le entregas tu corazón

y hacia él extiendes las manos,

14si te apartas del pecado que has cometido

y en tu morada no das cabida al mal,

15entonces podrás llevar la frente en alto

y mantenerte firme y libre de temor.

16Ciertamente olvidarás tus pesares

o los recordarás como el agua que pasó.

17Tu vida será más radiante que el sol de mediodía

y la oscuridad será como el amanecer.

18Vivirás tranquilo, porque hay esperanza;

estarás protegido11:18 estarás protegido. Alt. mirarás en torno tuyo (TM). y dormirás confiado.

19Descansarás sin temer a nadie

y muchos querrán ganarse tu favor.

20Pero los ojos de los malvados se apagarán;

no tendrán escapatoria.

¡Su esperanza es exhalar el último suspiro!».