Yobu 10 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 10:1-22

1“Ine ndatopa nawo moyo wanga;

choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka

ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.

2Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,

koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.

3Kodi mumakondwera mukamandizunza,

kunyoza ntchito ya manja anu,

chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?

4Kodi maso anu ali ngati a munthu?

Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?

5Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,

kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,

6kuti Inu mufufuze zolakwa zanga

ndi kulondola tchimo langa,

7ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa

ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?

8“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.

Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?

9Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,

kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?

10Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,

suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?

11Munandikuta ndi khungu ndi mnofu

ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?

12Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,

ndipo munasamalira bwino moyo wanga.

13“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,

ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:

14Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa

ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.

15Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!

Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga,

pakuti ndagwidwa ndi manyazi

ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.

16Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango

ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.

17Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane

ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi

magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.

18“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?

Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.

19Ndikanapanda kubadwa,

kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!

20Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?

Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha

21ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako

ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,

22ku dziko la mdima wandiweyani

ndi chisokonezo,

kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

Nueva Versión Internacional

Job 10:1-22

1»¡Ya estoy harto de esta vida!

Por eso doy rienda suelta a mi queja;

desahogo la amargura de mi alma.

2Le he dicho a Dios: No me condenes.

Dime qué es lo que tienes contra mí.

3¿Te parece bien el oprimirme

y despreciar la obra de tus manos

mientras te muestras complaciente ante los planes del malvado?

4¿Son tus ojos los de un simple mortal?

¿Ves las cosas como las vemos nosotros?

5¿Son tus días como los nuestros,

tus años como los de un mortal,

6para que andes investigando mis faltas

y averiguándolo todo acerca de mi pecado?

7¡Tú bien sabes que no soy culpable

y que de tus manos no tengo escapatoria!

8»Tú me hiciste con tus propias manos;

tú me diste forma.

¿Vas ahora a cambiar de parecer

y a ponerle fin a mi vida?

9Recuerda que tú me hiciste del barro;

¿vas ahora a devolverme al polvo?

10¿No fuiste tú quien me derramó como leche,

quien me hizo cuajar como queso?

11Fuiste tú quien me vistió de carne y piel,

quien me tejió con huesos y tendones.

12Me diste vida, me favoreciste con tu amor

y tu cuidado ha guardado mi espíritu.

13»Pero una cosa guardaste en tu corazón,10:13 corazón. En la Biblia se usa para designar el asiento de las emociones, pensamientos y voluntad, es decir, el proceso de toma de decisiones del ser humano.

y sé muy bien que la tuviste en mente:

14Que si yo peco, tú me vigilas

y no pasas por alto mi pecado.

15Si soy culpable, ¡ay de mí!

Si soy inocente, no puedo levantar mi cabeza.

¡Lleno estoy de vergüenza,

y consciente de mi aflicción!

16Si me levanto, me acechas como un león

y despliegas contra mí tu gran poder.

17Contra mí presentas nuevos testigos,

contra mí acrecientas tu enojo.

¡Una tras otra, tus tropas me atacan!

18»¿Por qué me hiciste salir del vientre?

¡Quisiera haber muerto sin que nadie me viera!

19¡Preferiría no haber existido

y haber pasado del vientre a la tumba!

20¿Acaso mis contados días no llegan ya a su fin?

¡Déjame disfrutar de un momento de alegría

21antes de mi partida sin regreso

a la tierra de las sombras y de la densa oscuridad,

22al país de la más profunda de las noches,

al país de las sombras y del caos,

donde aun la luz se asemeja a las tinieblas!».