Yobu 10 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 10:1-22

1“Ine ndatopa nawo moyo wanga;

choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka

ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.

2Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,

koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.

3Kodi mumakondwera mukamandizunza,

kunyoza ntchito ya manja anu,

chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?

4Kodi maso anu ali ngati a munthu?

Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?

5Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,

kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,

6kuti Inu mufufuze zolakwa zanga

ndi kulondola tchimo langa,

7ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa

ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?

8“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.

Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?

9Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,

kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?

10Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,

suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?

11Munandikuta ndi khungu ndi mnofu

ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?

12Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,

ndipo munasamalira bwino moyo wanga.

13“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,

ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:

14Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa

ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.

15Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!

Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga,

pakuti ndagwidwa ndi manyazi

ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.

16Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango

ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.

17Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane

ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi

magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.

18“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?

Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.

19Ndikanapanda kubadwa,

kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!

20Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?

Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha

21ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako

ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,

22ku dziko la mdima wandiweyani

ndi chisokonezo,

kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

Het Boek

Job 10:1-22

Job betreurt zijn geboortedag

1‘Ik ben het leven moe. Laat mij maar rustig klagen en mijn bitterheid en bedroefdheid onder woorden brengen.

2Ik zal tegen God zeggen: “Veroordeel mij niet zomaar, vertel mij tenminste waarom U het doet!

3Heeft U er wat aan dat U mij veracht en onder druk zet, een mens dat U Zelf hebt gemaakt, terwijl U tegelijkertijd vreugde en voorspoed geeft aan de goddelozen?

4-7Hebt U menselijke ogen en ziet U zoals stervelingen zien? Bent U net zo onrechtvaardig als mensen kunnen zijn? Is uw leven even kort als het onze? Waarom speurt U naar mijn fouten, terwijl U weet dat ik onschuldig ben? Doet U dat omdat U weet dat toch niemand mij uit uw hand kan redden?

8U hebt mij gemaakt, maar toch vernietigt U mij.

9Ach, denk er toch alstublieft aan dat ik maar van stof ben gemaakt, wilt U mij al zo snel weer in stof veranderen?

10Als melk hebt U mij uitgegoten, als kaas hebt U mij laten stremmen.

11U gaf mij een huid en vlees en doorweefde mij met beenderen en spieren.

12U gaf mij het leven, was goed en vriendelijk voor mij en uw goede zorgen hebben mij bewaard.

13-14 Toen U mij maakte, was U al van plan mij te straffen, als ik zou zondigen.

15Als ik schuldig ben, wee mij! En als ik onschuldig ben, dan loop ik met mijn hoofd gebogen, want ik schaam mij en ben overspoeld door verdriet.

16Als ik met opgeheven hoofd zou rondlopen, springt U als een leeuw op mij en toont uw geweldige overmacht.

17Telkens weer getuigt U tegen mij, treft U mij met een steeds groter wordende toorn, steeds vijandiger stelt u zich tegen mij op.

18Maar waarom liet U mij dan toch geboren worden? Waarom liet U mij bij mijn geboorte niet sterven?

19Dan zou ik niets geweten hebben van dit ellendige bestaan! Ik zou direct vanuit de baarmoeder naar het graf zijn gebracht.

20-21 Ziet U niet hoe weinig tijd ik nog heb? Och, laat mij toch met rust, zodat ik nog een korte tijd van vreugde heb, voordat ik naar het land van duisternis en de schaduwen van de dood ga om nooit meer terug te keren,

22een land dat zo donker is als de diepste duisternis van de nacht, een land van de schaduw van de dood, waar verwarring heerst en waar het helderste licht nog zo donker is als de nacht.” ’