Yobu 10 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 10:1-22

1“Ine ndatopa nawo moyo wanga;

choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka

ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.

2Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,

koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.

3Kodi mumakondwera mukamandizunza,

kunyoza ntchito ya manja anu,

chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?

4Kodi maso anu ali ngati a munthu?

Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?

5Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,

kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,

6kuti Inu mufufuze zolakwa zanga

ndi kulondola tchimo langa,

7ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa

ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?

8“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.

Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?

9Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,

kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?

10Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,

suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?

11Munandikuta ndi khungu ndi mnofu

ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?

12Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,

ndipo munasamalira bwino moyo wanga.

13“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,

ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:

14Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa

ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.

15Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!

Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga,

pakuti ndagwidwa ndi manyazi

ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.

16Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango

ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.

17Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane

ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi

magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.

18“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?

Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.

19Ndikanapanda kubadwa,

kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!

20Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?

Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha

21ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako

ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,

22ku dziko la mdima wandiweyani

ndi chisokonezo,

kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

Hoffnung für Alle

Hiob 10:1-22

Stell mich nicht als schuldig hin!

1»Mein Leben ekelt mich an!

Darum will ich der Klage freien Lauf lassen

und mir die Bitterkeit von der Seele reden.

2Gott, stell mich nicht als schuldig hin!

Erklär mir doch, warum du mich anklagst!

3Gefällt es dir, dass du mich unterdrückst?

Warum verachtest du mich,

den du selbst so kunstvoll gebildet hast?

Die Pläne gewissenloser Menschen aber führst du zum Erfolg.

4Hast du denn Menschenaugen?

Siehst du die Dinge nur von außen, so wie wir?

5Sind deine Lebenstage auch begrenzt,

deine Jahre rasch vergangen so wie unsere?

6Warum suchst du dann nach meiner Schuld

und hast es eilig, jede Sünde aufzuspüren?

7Du weißt doch genau, dass ich unschuldig bin

und dass es keinen gibt, der mich aus deiner Hand befreit.

8Deine Hände haben mich gebildet und geformt.

Willst du dich jetzt von mir abwenden und mich zerstören?

9Bedenke doch, dass du mich wie Ton gestaltet hast!

Lässt du mich jetzt wieder zu Staub zerfallen?

10Dir verdanke ich mein Leben:

dass mein Vater mich zeugte

und ich im Mutterleib Gestalt annahm.10,10 Wörtlich: Hast du mich nicht wie Milch ausgegossen und wie Käse gerinnen lassen?

11Mit Knochen und Sehnen hast du mich durchwoben,

mit Muskeln und Haut mich bekleidet.

12Ja, du hast mir das Leben geschenkt

und mir deine Güte erwiesen;

deine Fürsorge hat mich stets bewahrt.

13Aber tief in deinem Herzen denkst du anders;

in Wirklichkeit hast du dies beschlossen:

14Auf jedes Vergehen willst du mich festnageln

und mich von meiner Schuld nicht mehr freisprechen.

15Habe ich mich schuldig gemacht,

dann bin ich verloren!

Doch auch wenn ich im Recht bin,

kann ich nicht zuversichtlich sein,

denn man überhäuft mich mit Schande,

und mein Elend steht mir ständig vor Augen.

16Will ich mich behaupten, jagst du mich wie ein Löwe

und richtest mich wieder schrecklich zu.

17Einen Zeugen nach dem anderen lässt du gegen mich auftreten,

dein Zorn wird nur noch größer,

auf immer neue Art greifst du mich an.

18Warum hast du zugelassen,

dass ich geboren wurde?

Wäre ich doch gleich gestorben –

kein Mensch hätte mich je gesehen!

19Vom Mutterleib direkt ins Grab!

Ich wäre wie einer, den es nie gegeben hat.

20Wie kurz ist mein Leben! Schon fast vergangen!

Lass mich jetzt in Frieden, damit ich noch ein wenig Freude habe!

21Bald muss ich gehen und komme nie mehr wieder.

Ich gehe in ein Land, wo alles schwarz und düster ist,

22ins Land der Dunkelheit und tiefen Nacht,

ein Land, in dem es keine Ordnungen mehr gibt,

wo selbst das Licht nur schwarz ist wie die Nacht.«