Yobu 1 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 1:1-22

Mawu Oyamba

1Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. 2Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu, 3ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.

4Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo. 5Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.

Yobu Ayesedwa Koyamba

6Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi. 7Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

8Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”

9Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?” 10“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo. 11Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

12Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.”

Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.

13Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo, 14wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo, 15tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

16Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

17Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

18Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo, 19mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

20Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu, 21nati,

“Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga,

namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche.

Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga;

litamandike dzina la Yehova.”

22Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Аюб 1:1-22

Пролог

1В земле Уц жил человек по имени Аюб. Этот человек был непорочен и праведен, жил в страхе перед Аллахом и сторонился зла. 2У него было семеро сыновей и три дочери. 3Он владел семью тысячами овец, тремя тысячами верблюдов, пятьюстами парами волов и пятьюстами ослицами, а ещё великим множеством слуг. Он был самым знатным и самым уважаемым человеком среди всех жителей Востока.

4Его сыновья сходились, чтобы пировать по очереди в домах друг у друга, и приглашали трёх своих сестёр, чтобы есть и пить вместе с ними. 5Когда время пиров истекало, Аюб посылал за ними и совершал ритуал очищения. Рано утром он возносил за каждого из них всесожжение, думая: «Быть может, мои сыновья согрешили и в сердце своём оскорбили Аллаха». Так Аюб поступал постоянно.

Шайтан клевещет на Аюба

6Однажды ангелы1:6 Букв.: «сыны Всевышнего»; также в 2:1. Ангелы не являются сыновьями Всевышнего в буквальном смысле. Это образное выражение лишь указывает на их сверхъестественную природу и подчинённость Аллаху. пришли, чтобы предстать перед Вечным1:6 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., и с ними пришёл Шайтан1:6 Шайтан – это имя переводится как «противник», «обвинитель»..

7Вечный спросил Шайтана:

– Откуда ты пришёл?

Шайтан ответил Вечному:

– Я скитался по земле и обошёл её всю.

8Вечный сказал Шайтану:

– Приметил ли ты Моего раба Аюба? Нет на земле такого человека, как он: непорочного и праведного, кто живёт в страхе перед Аллахом и сторонится зла.

9– Разве даром Аюб боится Аллаха? – ответил Вечному Шайтан. – 10Разве не Ты оградил его самого, его домашних и всё его добро? Ты благословил дело его рук, и его стада и отары заполонили землю. 11Но протяни руку и порази всё, что у него есть, и он проклянёт Тебя прямо в лицо.

12Вечный сказал Шайтану:

– Хорошо. Всё, что у него есть, в твоих руках, но на него самого руки не поднимай.

И Шайтан ушёл от Вечного.

Первое испытание Аюба

13Однажды, когда сыновья и дочери Аюба пировали и пили вино в доме у старшего из братьев, 14к Аюбу пришёл вестник и сказал:

15– Волы пахали и ослицы паслись неподалёку, когда напали севеяне и угнали их. Они предали всех слуг мечу, и я – единственный, кто спасся, чтобы рассказать тебе об этом!

16Он ещё говорил, когда пришёл другой вестник и сказал:

– Огонь Аллаха пал с небес и сжёг овец и слуг, и я – единственный, кто спасся, чтобы рассказать тебе об этом!

17Он ещё говорил, когда пришёл третий вестник и сказал:

– Халдеи собрались в три отряда, набросились на стадо твоих верблюдов и угнали их. Они предали всех слуг мечу, и я – единственный, кто спасся, чтобы рассказать тебе об этом!

18Он ещё говорил, когда пришёл ещё один вестник и сказал:

– Твои сыновья и дочери пировали и пили вино в доме у старшего брата, 19как вдруг страшный вихрь примчался из пустыни и сотряс дом. Дом рухнул на них, и все они погибли, а я – единственный, кто спасся, чтобы рассказать тебе об этом.

20Тогда Аюб встал и в скорби разорвал на себе одежду и обрил голову. Он поклонился, пав лицом на землю, 21и сказал:

– Нагим я пришёл в этот мир,

нагим из него и уйду.

Вечный даровал, Вечный и отнял –

да будет имя Вечного прославлено.

22Во всём этом Аюб не согрешил и не обвинил Аллаха в несправедливости к нему.