Yesaya 9 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 9:1-21

Ufumu wa Mesiya

1Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.

2Anthu oyenda mu mdima

awona kuwala kwakukulu;

kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani

kuwunika kwawafikira.

3Inu mwauchulukitsa mtundu wanu

ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo.

Iwo akukondwa pamaso panu,

ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola,

ngatinso mmene anthu amakondwera

pamene akugawana zolanda ku nkhondo.

4Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani,

inu mwathyola goli

limene limawalemera,

ndodo zimene amamenyera mapewa awo,

ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.

5Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo,

ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi

zidzatenthedwa pa moto

ngati nkhuni.

6Chifukwa mwana watibadwira,

mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife,

ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake.

Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti

Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu,

Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.

7Ulamuliro ndi mtendere wake

zidzakhala zopanda malire.

Iye adzalamulira ufumu wake ali pa

mpando waufumu wa Davide,

ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza

mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo

kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya.

Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse

watsimikiza kuchita zimenezi.

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

8Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo;

ndipo mawuwo agwera pa Israeli.

9Anthu onse okhala mu

Efereimu ndi okhala mu Samariya,

adzadziwa zimenezi.

Iwo amayankhula modzikuza kuti,

10“Ngakhale njerwa zagumuka,

koma ife tidzamanga ndi miyala yosema.

Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa,

koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”

11Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo

ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.

12Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo

ayasama pakamwa kuti adye a Israeli.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

13Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja,

ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.

14Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe,

nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;

15mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka,

mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.

16Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa,

ndipo otsogoleredwa amatayika.

17Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata,

ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye,

pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo

aliyense amayankhula zopusa.

Komabe, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

18Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto;

moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga,

umayatsa nkhalango yowirira,

ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.

19Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse,

dziko lidzatenthedwa

ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto;

palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.

20Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya,

koma adzakhalabe ndi njala;

kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya,

koma sadzakhuta.

Aliyense azidzadya ana ake omwe.

21Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase;

onsewa pamodzi adzadya Yuda.

Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere,

mkono wake uli chitambasulire.

Hoffnung für Alle

Jesaja 9:1-20

1Das Volk, das in der Finsternis lebt, sieht ein großes Licht; hell strahlt es auf über denen, die ohne Hoffnung sind. 2Du, Herr, machst Israel wieder zu einem großen Volk und schenkst ihnen überströmende Freude. Sie sind fröhlich wie nach einer reichen Ernte; sie jubeln wie nach einem Sieg, wenn die Beute verteilt wird. 3So wie du Israel damals aus der Gewalt der Midianiter gerettet hast, so befreist du sie dann von der schweren Last der Fremdherrschaft. Du zerbrichst die Peitsche, mit der sie zur Zwangsarbeit getrieben werden. 4Die Soldatenstiefel, die beim Marschieren so laut dröhnen, und all die blutverschmierten Kampfgewänder werden ins Feuer geworfen und verbrannt.

5Denn uns ist ein Kind geboren! Ein Sohn ist uns geschenkt! Er wird die Herrschaft übernehmen. Man nennt ihn »Wunderbarer Ratgeber«, »Starker Gott«, »Ewiger Vater«, »Friedensfürst«. 6Er wird seine Herrschaft weit ausdehnen und dauerhaften Frieden bringen. Auf dem Thron Davids wird er regieren und sein Reich auf Recht und Gerechtigkeit gründen, jetzt und für alle Zeit. Der Herr, der allmächtige Gott, wird dies eintreffen lassen, leidenschaftlich verfolgt er sein Ziel.

Der Zorn des Herrn hat sich noch nicht gelegt

7Der Herr hat ein hartes Urteil über die Nachkommen von Jakob verhängt. Das Reich Israel wird es zu spüren bekommen, 8ja, es wird die Bewohner von Israel und die Einwohner Samarias treffen. Voller Hochmut prahlen sie: 9»Unsere Häuser aus Ziegelsteinen sind zwar zerstört, doch nun bauen wir uns neue aus Quadersteinen. Die knorrigen Maulbeerbäume wurden alle gefällt. Was soll’s, wir pflanzen Zedern dafür an!« 10Darum hat der Herr die Feinde von König Rezin stark gemacht und sie gegen Israel zum Krieg angestachelt. 11Die Syrer sind von Osten her ins Land eingefallen, und die Philister griffen von Westen an. Sie stürzten sich mit weit aufgerissenem Maul auf Israel und verschlangen ganze Stücke davon. Aber trotz allem hat sich Gottes Zorn nicht gelegt; noch ist seine strafende Hand erhoben.

12Der Herr, der allmächtige Gott, bestraft sein Volk hart, aber es kehrt nicht zu ihm zurück, ja, es fragt nicht einmal nach ihm. 13-14Darum wird der Herr an ein und demselben Tag Kopf und Schwanz von Israel abschlagen. Der Kopf, das sind die Führer des Volkes, die angesehenen Männer und Sippenoberhäupter; der Schwanz, das sind die angeblichen Propheten mit ihren falschen Weissagungen. Wie man die obersten Zweige der Palmen und die Binsen im Sumpf abschneidet, so wird Gott an einem Tag das ganze Volk vernichten. 15Denn die Führer dieses Volkes sind nichts als Verführer. Wer sich ihnen anvertraut, wird in die Irre geleitet. 16Darum verschont der Herr die jungen Männer nicht und hat kein Mitleid mit den Witwen und Waisen. Denn sie alle haben sich gegen ihn aufgelehnt, ihr ganzes Leben besteht aus Lug und Betrug. Aber noch hat sich Gottes Zorn nicht gelegt; noch ist seine strafende Hand erhoben.

17Durch ihre Gottlosigkeit sprechen sie sich selbst das Urteil. Ihre Bosheit gleicht einer lodernden Flamme, die Unkraut und Dornensträucher verzehrt und das dichte Unterholz im Wald in Brand steckt, bis schwarze Rauchsäulen aufsteigen. 18In seinem glühenden Zorn denkt der Herr, der allmächtige Gott, gar nicht daran, dieses Feuer einzudämmen. Zurück bleibt ein zerstörtes Land, ein Land, in dem jeder gegen jeden kämpft. Niemand kümmert sich um den anderen, 19jeder will nur seinen Hunger stillen. Gierig und rücksichtslos fällt man über alles Essbare her und wird trotzdem nicht satt. Am Ende zerfleischen sie sich gegenseitig: 20Die Leute vom Stamm Manasse stürzen sich auf den Stamm Ephraim, die von Ephraim gehen auf Manasse los, und zusammen fallen sie über Juda her. Und immer noch ist Gottes Zorn nicht gestillt; drohend schwebt seine Hand über diesem Volk.