Yesaya 8 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 8:1-22

Asiriya, Chida cha Yehova

1Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira. 2Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”

3Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’ 4Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”

5Yehova anayankhulanso ndi Ine;

6“Popeza anthu a dziko ili akana

madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu,

ndipo akukondwerera Rezini

ndi mwana wa Remaliya,

7nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa

madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo;

mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo.

Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse

ndi mʼmagombe ake onse.

8Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira,

adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi.

Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse,

iwe Imanueli!”

9Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere!

Tamverani, inu mayiko onse akutali.

Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!

Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!

10Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu,

kambiranani zochita, koma zidzalephereka,

pakuti Mulungu ali nafe.

Yehova Achenjeza Mneneri

11Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:

12“Usamanene kuti ndi chiwembu,

chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu

usamaope zimene anthuwa amaziopa,

ndipo usamachite nazo mantha.

13Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera,

ndiye amene uyenera kumuopa,

ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,

14ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika;

koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala

mwala wopunthwitsa,

mwala umene umapunthwitsa anthu,

thanthwe limene limagwetsa anthu.

Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.

15Anthu ambiri adzapunthwapo

adzagwa ndi kuthyokathyoka,

adzakodwa ndi kugwidwa.”

16Manga umboniwu

ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.

17Ndidzayembekezera Yehova,

amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo.

Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.

18Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.

19Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo, 20kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala. 21Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo. 22Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

New International Reader’s Version

Isaiah 8:1-22

Isaiah and His Children Are Signs

1The Lord said to me, “Get a large sheet of paper. Write ‘Maher-Shalal-Hash-Baz’ on it with a pen.” 2So I sent for Zechariah and Uriah the priest. Zechariah is the son of Jeberekiah. Zechariah and Uriah were witnesses for me whom I could trust. 3Then I went and slept with my wife, who was a prophet. She became pregnant and had a baby boy. The Lord said to me, “Name him Maher-Shalal-Hash-Baz. 4The king of Assyria will carry off the wealth of Damascus. He will also carry away the goods that were taken from Samaria. That will happen before the boy knows how to say ‘My father’ or ‘My mother.’ ”

5The Lord continued,

6“I am like the gently flowing stream of Siloam.

But the people of Judah have turned their backs on me.

They are filled with joy because of the fall of Rezin

and the son of Remaliah.

7So I am about to bring against these people

the king of Assyria and his whole army.

The Assyrians will be like the mighty Euphrates River

when it is flooding.

They will run over everything in their path.

8They will sweep on into Judah like a flood.

They will pass through Judah and reach all the way to Jerusalem.

Immanuel, they will attack your land like an eagle.

Their wings will spread out and cover it.”

9Sound the battle cry, you nations!

But you will be torn apart.

Listen, all you lands far away!

Prepare for battle! But you will be torn apart.

Prepare for battle! But you will be torn apart.

10Make your battle plans! But you won’t succeed.

Give your orders! But they won’t be carried out.

That’s because God is with us.

11The Lord speaks to me while his powerful hand is on me. He is warning me not to live the way these people live. He says,

12“People of Judah, do not agree with those who say

Isaiah is guilty of treason.

Do not fear what they fear.

Do not be afraid.

13The Lord rules over all.

So you must think about him as holy.

You must have respect for him.

You must fear him.

14Then the Lord will be a holy place of safety for you.

But that’s not true for many people in Israel and Judah.

He will be a stone that causes them to trip.

He will be a rock that makes them fall.

And for the people of Jerusalem

he will be a trap and a snare.

15Many of them will trip.

They will fall and be broken.

They will be trapped and captured.”

16Tie up and seal this warning that the Lord said to you through me.

Preserve among my followers what he taught you through me.

17I will wait for the Lord.

He is turning his face away from Jacob’s people.

I will put my trust in him.

18Here I am. Here are the children the Lord has given me. We are signs and reminders to Israel from the Lord who rules over all. He lives on Mount Zion.

The Darkness Turns to Light

19There are people who get messages from those who have died. But these people only whisper words that are barely heard. Suppose someone tells you to ask for advice from these people. Shouldn’t you ask for advice from your God instead? Why should you get advice from dead people to help those who are alive? 20Follow what the Lord taught you and said to you through me. People who don’t speak in keeping with these words will have no hope in the morning. 21They will suffer and be hungry. They’ll wander through the land. When they are very hungry, they will become angry. They’ll look up toward heaven. They’ll ask for bad things to happen to their king and their God. 22Then they will look at the earth. They’ll see nothing but suffering and darkness. They’ll see terrible sadness. They’ll be driven into total darkness.