Yesaya 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 7:1-25

Yesaya Achenjeza Ahazi

1Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.

2Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.

3Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu. 4Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya. 5Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti, 6‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’ 7Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi:

“ ‘Zimenezo sizidzatheka,

sizidzachitika konse,

8pakuti Siriya amadalira Damasiko,

ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi.

Zisanathe zaka 65

Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.

9Dziko la Efereimu limadalira Samariya

ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi.

Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu,

ndithu simudzalimba konse.’ ”

10Yehova anayankhulanso ndi Ahazi, 11“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.”

12Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”

13Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga? 14Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli. 15Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino. 16Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja. 17Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”

18Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya. 19Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto. 20Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe. 21Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri. 22Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi. 23Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga. 24Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga. 25Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

New Russian Translation

Исаия 7:1-25

Знамение Еммануила

1Когда Ахаз, сын Иотама, внук Уззии, был царем Иудеи, Рецин, царь Арама, и Пеках, сын Ремалии, царя Израиля, пошли войной на Иерусалим, но не смогли его одолеть.

2Дому Давида возвестили: «Арам вступил в союз с Ефремом»7:2 Или: «разбил стан на земле Ефрема»., и сердца у7:2 Букв.: «его сердце». Ахаза и у его народа затрепетали, как деревья в лесу трепещут от ветра.

3Господь сказал Исаии:

– Выйди навстречу Ахазу со своим сыном Шеар-Иашувом7:3 Шеар-Иашув – это имя означает «остаток вернется». к концу водопровода Верхнего пруда, на дорогу к Сукновальному полю. 4Скажи ему: «Смотри, будь спокоен, не бойся. Не падай духом из-за двух концов этих тлеющих головней – из-за неистового гнева Рецина с Арамом и из-за сына Ремалии. 5Арам, Ефрем и сын Ремалии замышляют против тебя зло, говоря: 6„Пойдем на Иудею и запугаем ее, завоюем ее и поставим в ней царем сына Тавеела“. 7Но так говорит Владыка Господь:

Это не сбудется,

этого не случится,

8ведь глава Арама – Дамаск,

а глава Дамаска – Рецин.

Через шестьдесят пять лет

Ефрем будет рассеян и перестанет быть народом.

9Глава Ефрема – Самария,

а глава Самарии – сын Ремалии.

Если не будете твердо стоять в своей вере,

не устоите вовсе».

10И снова Господь сказал Ахазу:

11– Проси у Господа, своего Бога, знамения, все равно – в глубинах мира мертвых7:11 Мира мертвых – евр.: «шаала». Это слово может означать «в мире мертвых» и «проси». или на высотах небес.

12Но Ахаз сказал:

– Я не стану просить, не буду испытывать Господа.

13Тогда Исаия сказал:

– Слушайте, дом Давида! Разве не довольно вам испытывать человеческое терпение? Вы хотите испытать и терпение моего Бога? 14Итак, Владыка Сам даст вам знамение: вот, дева забеременеет и родит Сына, и назовет Его Еммануил7:14 Имя Еммануил (евр.: «Имману Эль») означает «с нами Бог». Эти слова являются пророчеством о рождении Иисуса Христа (см. Мат. 1:22-25).. 15Он будет питаться творогом и медом, пока не научится отвергать злое и избирать доброе. 16Но прежде чем мальчик научится отвергать злое и избирать доброе, земли двух царей, от которых ты в ужасе, будут опустошены. 17Но Господь наведет на тебя, на твой народ и на дом твоего отца такие дни, каких не бывало с тех пор, как Ефрем отделился от Иуды7:17 См. 3 Цар. 12:1-20., – Он наведет царя Ассирии.

18В тот день Господь свистнет мухе, что у истоков рек Египта, и пчеле, что в ассирийской земле. 19Они прилетят и опустятся в крутые ущелья и в расщелины скал, на все колючие кусты и на все пастбища.

20В тот день Владыка обреет ваши головы, волосы на ногах и отрежет бороды бритвой, нанятой по ту сторону Евфрата, – царем Ассирии7:20 В древние времена военнопленному сбривали волосы для того, чтобы сделать его объектом всеобщего поругания, унижения и осуждения..

21В тот день если кто сможет оставить в живых молодую корову и двух овец, 22то по изобилию молока, которое они станут давать, он будет есть творог. Все, кто останется в стране, будут есть творог и мед.

23В тот день там, где некогда росла тысяча виноградных лоз стоимостью в тысячу серебряных шекелей7:23 Около 11,5 кг., будут лишь терновник и колючки. 24Люди будут ходить туда с луком и стрелами, потому что земля будет покрыта терновником и колючками.

25Что же до холмов, которые некогда возделывали мотыгой, то вы больше не пойдете туда, боясь терновника и колючек. Туда будут выгонять крупный скот, и мелкий скот будет топтать их.