Yesaya 66 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 66:1-24

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?”

Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

3Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

amaphanso munthu,

ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,

amaphanso galu.

Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya

amaperekanso magazi a nkhumba.

Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso

amapembedzanso fano.

Popeza iwo asankha njira zawozawo,

ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.

4Inenso ndawasankhira chilango chowawa

ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.

Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,

pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.

Anachita zoyipa pamaso panga

ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

5Imvani mawu a Yehova,

inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:

“Abale anu amene amakudani,

ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,

‘Yehova alemekezeke

kuti ife tione chimwemwe chanu!’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6Imvani mfuwu mu mzinda,

imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!

Limenelo ndi liwu la Yehova,

kulanga adani ake onse.

7“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

wachira kale;

asanayambe kumva ululu,

wabala kale mwana wamwamuna.

8Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

Ndani anazionapo zinthu zoterezi?

Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,

kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?

Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa

nthawi yomweyo anabereka ana ake.

9Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.

“Kodi ndingatseke mimba

pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,

kondwera nayeni kwambiri,

nonse amene mumamulira.

11Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri

wa mʼmawere

a chitonthozo chake.”

12Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,

ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,

kapena kumufungata pa miyendo yake.

13Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

moteronso Ine ndidzakusangalatsani;

ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

14Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira

ndi kuti ndimakwiyira adani anga.

15Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;

Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake

ndi malawi amoto.

16Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

ndi moto ndi lupanga,

Yehova adzapha anthu ambiri.

17Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

O Livro

Isaías 66:1-24

O juízo e a esperança

1Assim diz o Senhor: “O céu é o meu trono e a Terra é o estrado dos meus pés! Que casa me poderiam construir ou que lugar para o meu descanso? 2Foi a minha mão que fez todas essas coisas! Tudo é meu! Contudo, olharei com piedade para todo aquele que tiver um coração simples e arrependido, que trema perante a minha palavra.

3Mas aqueles que preferem escolher os seus próprios caminhos, deleitando-se nos seus pecados, serão amaldiçoados; as suas oferendas não serão aceites. Quando uma tal pessoa sacrificar um boi sobre o altar de Deus, isso terá para mim o mesmo significado e gravidade que assassinar um homem. Se sacrificarem um cordeiro, ou se trouxerem uma oferta de cereais, será tão repugnante como trazer um cão ou sangue de porco para o altar! Quando queimarem incenso será absolutamente o mesmo que prestar culto a abominações. 4Mandar-lhes-ei grandes tribulações; tudo aquilo que precisamente receiam, visto que quando chamei por eles recusaram responder-me e quando lhes dirigi a minha palavra não quiseram ouvir-me. Até fizeram o mal, na minha própria presença, e optaram por aquelas coisas que sabiam bem que eu abominava.”

5Ouçam a palavra do Senhor, todos os que o temem e tremam com a sua palavra: “Os vossos irmãos vos odeiam e aborrecem; expulsam-vos por serem leais ao meu nome; troçam de vocês dizendo: ‘Que o Senhor seja glorificado, para que vejamos a vossa alegria!’ Mas se dizem isso, agora na risota, o certo é que hão de ficar envergonhados.

6Que movimento, que rumor é este na cidade? Que ruído tremendo é este que se ouve no templo? É justamente a voz do Senhor dando a paga aos seus inimigos.

7Antes das contrações do parto, ela deu à luz; antes que as dores viessem, teve um menino. 8Quem alguma vez ouviu tal ou viu coisa semelhante? Porventura um povo nasce num só dia ou uma nação nasce duma só vez? Mas foi este o caso de Sião, que mal sentiu as contrações, deu à luz os seus filhos. 9Seria eu capaz de levar o parto até ao último momento sem que se desse o nascimento?, pergunta o Senhor, o vosso Deus. Não, nunca!

10Alegrem-se com Jerusalém! Regozijam-se com ela, todos os que a amam e que choraram por causa dela! Deleitem-se em Jerusalém! 11Saciem-se fartamente da sua glória, como se fosse um bebé sôfrego ao peito da mãe. 12A prosperidade encherá Jerusalém como se um rio a inundasse, diz o Senhor, pois sou eu quem a envia. Serão as riquezas dos gentios que se derramarão sobre ela. Os seus filhos alimentar-se-ão aos seus peitos, levados ao seu colo, embalados sobre os seus joelhos. 13Confortar-vos-ei ali, tal como um pequenino é consolado pela mãe.”

14Quando virem Jerusalém, o vosso coração vibrará de gozo; o vosso corpo retomará vigor como a erva na primavera. Todo o mundo verá a boa mão do Senhor sobre o seu povo e a sua cólera sobre os seus adversários.

15Reparem, o Senhor há de vir com fogo e com velozes carros, para condenar com severa cólera, para fazer justiça com chamas de fogo! 16Será precisamente com fogo e com a sua espada que o Senhor condenará o mundo e será grande a matança que terá de fazer!

17“Serão mortos todos aqueles que adoram ídolos atrás de qualquer árvore dum jardim, fazendo festins com carne de porco e de ratos, e com toda a espécie de coisas abomináveis. Sim, esses terão um fim maldito, diz o Senhor.

18Conheço muito bem as suas obras; sei perfeitamente o que pensam. Por isso, juntarei todas as nações e todos os povos contra Jerusalém, para ali verem a minha glória. 19Realizarei um poderoso milagre contra eles e aos que dali escaparem enviá-los-ei como missionários a Társis, a Pul e a Lude, povo exímio no uso do arco, a Tubal, à Grécia e às terras para além do mar, que nunca ouviram falar da minha fama, nem se deram conta da minha glória. Aí será anunciada a minha glória aos gentios. 20E trarão os vossos irmãos, vindos de todas as nações, como se fosse um presente oferecido ao Senhor, transportando-os cuidadosamente em carros e liteiras, em mulas e camelos, até ao meu santo monte, até Jerusalém, diz o Senhor. Será como quando se trazem as ofertas na época das colheitas, que enchem o templo do Senhor, transportadas em vasos limpos. 21E nomearei alguns desses para serem meus sacerdotes e levitas, diz o Senhor.

22Tão certo como os novos céus e a nova Terra que eu hei de criar permanecerão para sempre, assim também serão para sempre o meu povo, com um nome que nunca há de desaparecer. 23Toda a humanidade virá para me adorar, de sábado a sábado, de uma festa da lua nova a outra, diz o Senhor. 24Ao saírem verão os corpos mortos dos que se revoltaram contra mim, visto que os vermes que os comem nunca morrerão e o fogo que os consome nunca se apagará; serão um sinal de desprezo para todo o ser humano.”