Yesaya 66 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 66:1-24

Chiweruzo ndi Chiyembekezo

1Yehova akuti,

“Kumwamba ndi mpando wanga waufumu

ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga.

Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire,

ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?

2Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

motero zonsezi ndi zanga?”

Akutero Yehova.

“Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu:

amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima,

ndipo amamvera mawu anga.

3Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

amaphanso munthu,

ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa,

amaphanso galu.

Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya

amaperekanso magazi a nkhumba.

Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso

amapembedzanso fano.

Popeza iwo asankha njira zawozawo,

ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.

4Inenso ndawasankhira chilango chowawa

ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija.

Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha,

pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu.

Anachita zoyipa pamaso panga

ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”

5Imvani mawu a Yehova,

inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake:

“Abale anu amene amakudani,

ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti,

‘Yehova alemekezeke

kuti ife tione chimwemwe chanu!’

Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

6Imvani mfuwu mu mzinda,

imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu!

Limenelo ndi liwu la Yehova,

kulanga adani ake onse.

7“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

wachira kale;

asanayambe kumva ululu,

wabala kale mwana wamwamuna.

8Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

Ndani anazionapo zinthu zoterezi?

Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi,

kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi?

Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa

nthawi yomweyo anabereka ana ake.

9Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova.

“Kodi ndingatseke mimba

pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.

10“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

inu nonse amene mumakonda Yerusalemu,

kondwera nayeni kwambiri,

nonse amene mumamulira.

11Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri

wa mʼmawere

a chitonthozo chake.”

12Yehova akuti,

“Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi,

ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira.

Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa,

kapena kumufungata pa miyendo yake.

13Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

moteronso Ine ndidzakusangalatsani;

ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”

14Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu.

Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira

ndi kuti ndimakwiyira adani anga.

15Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu;

Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake

ndi malawi amoto.

16Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

ndi moto ndi lupanga,

Yehova adzapha anthu ambiri.

17Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina. 20Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo. 21Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova. 23“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova. 24“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

Nova Versão Internacional

Isaías 66:1-24

Julgamento e Esperança

1Assim diz o Senhor:

“O céu é o meu trono;

e a terra, o estrado dos meus pés.

Que espécie de casa vocês me edificarão?

É este o meu lugar de descanso?

2Não foram as minhas mãos que fizeram todas essas coisas,

e por isso vieram a existir?”, pergunta o Senhor.

“A este eu estimo:

ao humilde e contrito de espírito,

que treme diante da minha palavra.

3Mas aquele que sacrifica um boi

é como quem mata um homem;

aquele que sacrifica um cordeiro,

é como quem quebra o pescoço de um cachorro;

aquele que faz oferta de cereal

é como quem apresenta sangue de porco,

e aquele que queima incenso memorial,

é como quem adora um ídolo.

Eles escolheram os seus caminhos,

e suas almas têm prazer em suas práticas detestáveis.

4Por isso também escolherei um duro tratamento para eles

e trarei sobre eles o que eles temem.

Pois eu chamei, e ninguém respondeu;

falei, e ninguém deu ouvidos.

Fizeram o mal diante de mim

e escolheram o que me desagrada”.

5Ouçam a palavra do Senhor,

vocês que tremem diante da sua palavra:

“Seus irmãos que os odeiam e os excluem

por causa do meu nome, disseram:

‘Que o Senhor seja glorioso,

para que vejamos a alegria de vocês!’

Mas eles é que passarão vergonha.

6Ouçam o estrondo que vem da cidade,

o som que vem do templo!

É o Senhor

que está dando a devida retribuição aos seus inimigos.

7“Antes de entrar em trabalho de parto,

ela dá à luz;

antes de lhe sobrevirem as dores,

ela ganha um menino.

8Quem já ouviu uma coisa dessas?

Quem já viu tais coisas?

Pode uma nação nascer num só dia,

ou, pode-se dar à luz um povo num instante?

Pois Sião ainda estava em trabalho de parto,

e deu à luz seus filhos.

9Acaso faço chegar a hora do parto

e não faço nascer?”,

diz o Senhor.

“Acaso fecho o ventre,

sendo que eu faço dar à luz?”,

pergunta o seu Deus.

10“Regozijem-se com Jerusalém e alegrem-se por ela,

todos vocês que a amam;

regozijem-se muito com ela,

todos vocês que por ela pranteiam.

11Pois vocês irão mamar e saciar-se

em seus seios reconfortantes,

e beberão à vontade

e se deleitarão em sua fartura.”

12Pois assim diz o Senhor:

“Estenderei para ela a paz como um rio

e a riqueza das nações, como uma corrente avassaladora;

vocês serão amamentados nos braços dela

e acalentados em seus joelhos.

13Assim como uma mãe consola seu filho,

também eu os consolarei;

em Jerusalém vocês serão consolados”.

14Quando vocês virem isso, o seu coração se regozijará,

e vocês florescerão como a relva;

a mão do Senhor estará com os seus servos,

mas a sua ira será contra os seus adversários.

15Vejam! O Senhor vem num fogo,

e os seus carros são como um turbilhão!

Transformará em fúria a sua ira

e em labaredas de fogo, a sua repreensão.

16Pois com fogo e com a espada

o Senhor executará julgamento sobre todos os homens,

e muitos serão os mortos pela mão do Senhor.

17“Os que se consagram para entrar nos jardins indo atrás do sacerdote66.17 Ou da deusa que está no meio, comem66.17 Ou jardins atrás de um de seus templos, e aqueles que comem carne de porco, ratos e outras coisas repugnantes, todos eles perecerão”, declara o Senhor.

18“E, por causa dos seus atos e das suas conspirações, virei ajuntar todas as nações e línguas, e elas virão e verão a minha glória.

19“Estabelecerei um sinal entre elas, e enviarei alguns dos sobreviventes às nações: a Társis, aos líbios66.19 Conforme alguns manuscritos da Septuaginta. O Texto Massorético diz a Pul. e aos lídios, famosos flecheiros, a Tubal, à Grécia, e às ilhas distantes, que não ouviram falar de mim e não viram a minha glória. Eles proclamarão a minha glória entre as nações. 20Também dentre todas as nações trarão os irmãos de vocês ao meu santo monte, em Jerusalém, como oferta ao Senhor. Virão a cavalo, em carros e carroças, e montados em mulas e camelos”, diz o Senhor.

“Farão como fazem os israelitas quando apresentam as suas ofertas de cereal, trazendo-as em vasos cerimonialmente puros; 21também escolherei alguns deles para serem sacerdotes e levitas”, diz o Senhor.

22“Assim como os novos céus e a nova terra que vou criar serão duradouros diante de mim”, declara o Senhor, “assim serão duradouros os descendentes de vocês e o seu nome. 23De uma lua nova a outra e de um sábado a outro, toda a humanidade virá e se inclinará diante de mim”, diz o Senhor. 24“Sairão e verão os cadáveres dos que se rebelaram contra mim; o verme destes não morrerá, e o seu fogo não se apagará, e causarão repugnância a toda a humanidade.”