Yesaya 65 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

New International Version

Isaiah 65:1-25

Judgment and Salvation

1“I revealed myself to those who did not ask for me;

I was found by those who did not seek me.

To a nation that did not call on my name,

I said, ‘Here am I, here am I.’

2All day long I have held out my hands

to an obstinate people,

who walk in ways not good,

pursuing their own imaginations—

3a people who continually provoke me

to my very face,

offering sacrifices in gardens

and burning incense on altars of brick;

4who sit among the graves

and spend their nights keeping secret vigil;

who eat the flesh of pigs,

and whose pots hold broth of impure meat;

5who say, ‘Keep away; don’t come near me,

for I am too sacred for you!’

Such people are smoke in my nostrils,

a fire that keeps burning all day.

6“See, it stands written before me:

I will not keep silent but will pay back in full;

I will pay it back into their laps—

7both your sins and the sins of your ancestors,”

says the Lord.

“Because they burned sacrifices on the mountains

and defied me on the hills,

I will measure into their laps

the full payment for their former deeds.”

8This is what the Lord says:

“As when juice is still found in a cluster of grapes

and people say, ‘Don’t destroy it,

there is still a blessing in it,’

so will I do in behalf of my servants;

I will not destroy them all.

9I will bring forth descendants from Jacob,

and from Judah those who will possess my mountains;

my chosen people will inherit them,

and there will my servants live.

10Sharon will become a pasture for flocks,

and the Valley of Achor a resting place for herds,

for my people who seek me.

11“But as for you who forsake the Lord

and forget my holy mountain,

who spread a table for Fortune

and fill bowls of mixed wine for Destiny,

12I will destine you for the sword,

and all of you will fall in the slaughter;

for I called but you did not answer,

I spoke but you did not listen.

You did evil in my sight

and chose what displeases me.”

13Therefore this is what the Sovereign Lord says:

“My servants will eat,

but you will go hungry;

my servants will drink,

but you will go thirsty;

my servants will rejoice,

but you will be put to shame.

14My servants will sing

out of the joy of their hearts,

but you will cry out

from anguish of heart

and wail in brokenness of spirit.

15You will leave your name

for my chosen ones to use in their curses;

the Sovereign Lord will put you to death,

but to his servants he will give another name.

16Whoever invokes a blessing in the land

will do so by the one true God;

whoever takes an oath in the land

will swear by the one true God.

For the past troubles will be forgotten

and hidden from my eyes.

New Heavens and a New Earth

17“See, I will create

new heavens and a new earth.

The former things will not be remembered,

nor will they come to mind.

18But be glad and rejoice forever

in what I will create,

for I will create Jerusalem to be a delight

and its people a joy.

19I will rejoice over Jerusalem

and take delight in my people;

the sound of weeping and of crying

will be heard in it no more.

20“Never again will there be in it

an infant who lives but a few days,

or an old man who does not live out his years;

the one who dies at a hundred

will be thought a mere child;

the one who fails to reach65:20 Or the sinner who reaches a hundred

will be considered accursed.

21They will build houses and dwell in them;

they will plant vineyards and eat their fruit.

22No longer will they build houses and others live in them,

or plant and others eat.

For as the days of a tree,

so will be the days of my people;

my chosen ones will long enjoy

the work of their hands.

23They will not labor in vain,

nor will they bear children doomed to misfortune;

for they will be a people blessed by the Lord,

they and their descendants with them.

24Before they call I will answer;

while they are still speaking I will hear.

25The wolf and the lamb will feed together,

and the lion will eat straw like the ox,

and dust will be the serpent’s food.

They will neither harm nor destroy

on all my holy mountain,”

says the Lord.