Yesaya 65 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

New International Reader’s Version

Isaiah 65:1-25

The Lord Judges and Saves

1The Lord says, “I made myself known to those who were not asking for me.

I was found by those who were not trying to find me.

I spoke to a nation that did not pray to me.

‘Here I am,’ I said. ‘Here I am.’

2All day long I have held out my hands

to welcome a stubborn nation.

They lead sinful lives.

They go where their evil thoughts take them.

3They are always making me very angry.

They do it right in front of me.

They offer sacrifices in the gardens of other gods.

They burn incense on altars that are made out of bricks.

4They sit among the graves.

They spend their nights talking to the spirits of the dead.

They eat the meat of pigs.

Their cooking pots hold soup that has ‘unclean’ meat in it.

5They say, ‘Keep away! Don’t come near us!

We are too sacred for you!’

Those people are like smoke in my nose.

They are like a fire that keeps burning all day.

6“I will judge them. I have even written it down.

I will not keep silent.

Instead, I will pay them back for all their sins.

7I will punish them for their sins.

I will also punish them for the sins of their people before them.”

This is what the Lord says.

“They burned sacrifices on the mountains.

They disobeyed me by worshiping other gods on the hills.

So I will make sure they are fully punished

for all the sins they have committed.”

8The Lord says,

“Sometimes juice is still left in grapes that have been crushed.

So people say, ‘Don’t destroy them.’

They are still of some benefit.”

That is what I will do for the good of those who serve me.

I will not destroy all my people.

9I will give children

to the families of Jacob and Judah.

They will possess my entire land.

My chosen people will be given all of it.

Those who serve me will live there.

10Their flocks will eat in the rich grasslands of Sharon.

Their herds will rest in the Valley of Achor.

That is what I will do for my people who follow me.

11“But some of you have deserted me.

You no longer worship on my holy mountain of Zion.

You spread a table for the god called Good Fortune.

You offer bowls of mixed wine to the god named Fate.

12So I will make it your fate to be killed by swords.

All of you will die in the battle.

That’s because I called out to you, but you did not answer me.

I spoke to you, but you did not listen.

You did what is evil in my sight.

You chose to do what does not please me.”

13So the Lord and King says,

“Those who serve me will have food to eat.

But you will be hungry.

My servants will have plenty to drink.

But you will be thirsty.

Those who serve me will be full of joy.

But you will be put to shame.

14My servants will sing

with joy in their hearts.

But you will cry out

because of the great pain in your hearts.

You will cry because your spirits are sad.

15My chosen ones will use your names

when they curse others.

I am your Lord and King.

I will put you to death.

But I will give new names to those who serve me.

16They will ask me to bless their land.

They will do it in my name.

I am the one true God.

They will make promises in their land.

They will do it in my name.

I am the one true God.

The troubles of the past will be forgotten.

They will be hidden from my eyes.

The Lord Will Create New Heavens and a New Earth

17“I will create new heavens and a new earth.

The things that have happened before will not be remembered.

They will not even enter your minds.

18So be glad and full of joy forever

because of what I will create.

I will cause others to take delight in Jerusalem.

They will be filled with joy

when they see its people.

19And I will be full of joy because of Jerusalem.

I will take delight in my people.

Weeping and crying

will not be heard there anymore.

20“Babies in Jerusalem will no longer

live only a few days.

Old people will not fail

to live for a very long time.

Those who live to the age of 100

will be thought of as mere children when they die.

Those who die before they are 100

will be considered as having been under God’s curse.

21My people will build houses and live in them.

They will plant vineyards and eat their fruit.

22They will no longer build houses

only to have others live in them.

They will no longer plant crops

only to have others eat them.

My people will live to be as old as trees.

My chosen ones will enjoy for a long time

the things they have worked for.

23Their work will not be worthless anymore.

They will not have children who are sure to face sudden terror.

Instead, I will bless them.

I will also bless their children after them.

24Even before they call out to me, I will answer them.

While they are still speaking, I will hear them.

25Wolves and lambs will eat together.

Lions will eat straw like oxen.

Serpents will eat nothing but dust.

None of those animals will harm or destroy

anything or anyone on my holy mountain of Zion,”

says the Lord.