Yesaya 65 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 65:1-25

Omusango n’Obulokozi

165:1 a Kos 1:10; Bar 9:24-26; 10:20* b Bef 2:12Mukama n’alyoka agamba nti,

“Nze nnali mwetegefu okweyoleka eri abo abaali tebannoonya.

Neeraga abo abaali tebannoonya.

Eri eggwanga eryali litakoowoola linnya lyange nneyoleka gye bali ng’aŋŋamba nti, ‘Ndi wano, Ndi wano.’

265:2 a Is 1:2, 23; Bar 10:21* b Zab 81:11-12; Is 66:18Nagolola emikono gyange olunaku lwonna okutuusa obudde okuziba

eri abantu abeewagguzze,

abatambulira mu makubo amabi

abagoberera entegeka ezaabwe ku bwabwe;

365:3 a Yob 1:11 b Is 1:29abantu bulijjo

abansomooza mu maaso gange gennyini

nga bawaayo ebiweebwayo mu nnimiro

ne bookera n’ebiweebwayo ku byoto eby’amatoffaali;

465:4 Lv 11:7abatuula mu malaalo

ne bamalako ekiro kyonna mu bifo ebyekusifu,

abalya ennyama y’embizzi,

era n’amaseffuliya gaabwe gajjudde ennyama etali nnongoofu.

565:5 Mat 9:11; Luk 7:39; 18:9-12Bagamba nti, ‘Beera wala, tojja kumpi nange,

kubanga ndi mutuukirivu nnyo ggwe okunsaanira!’

Abantu bwe batyo mukka mu nnyindo zange,

omuliro ogwaka olunaku lwonna.

665:6 a Zab 50:3 b Yer 16:18 c Zab 79:12“Laba kiwandiikiddwa mu maaso gange.

Sijja kusirika naye nzija kusasula mu bujjuvu,

nzija kubasasula bibatuukireko ddala;

765:7 a Is 22:14 b Kuv 20:5 c Is 57:7olw’ebibi byammwe byonna era n’olw’ebibi bya bakitammwe,”

bw’ayogera Mukama Katonda.

“Kubanga baayokera ebiweebwayo byabwe ku lusozi

era ne bannyoomera ku busozi,

ndibalira mu mikono gyabwe empeera yennyini enzijuvu

ey’ebikolwa byabwe eby’edda.”

8Bw’atyo bw’ayogera Mukama:

“Ng’omubisi bwe gusangibwa mu kirimba ky’emizabbibu

abantu ne bagamba nti, ‘Togwonoona,

gukyalimu akalungi,’

bwe ntyo bwe ndikibakolera olw’obulungi bw’abaweereza bange.

Sijja kubasaanyaawo bonna.

965:9 a Is 45:19 b Am 9:11-15 c Is 32:18Ndiggya ezzadde okuva mu Yakobo

era ne mu Yuda abo abalitwala ensozi zange;

abantu bange abalonde balizigabana,

era eyo abaweereza bange gye balibeera.

1065:10 a Is 35:2 b Yos 7:26 c Is 51:1Awo Saloni kiribeera ddundiro lya bisibo,

era n’ekiwonvu kya Akoli kifo kya nte we zigalamira

olw’abantu bange abannoonya.

1165:11 Ma 29:24-25; Is 1:28“Naye mmwe abava ku Mukama

ne mwerabira olusozi lwange olutukuvu

ne muteekerateekera emmeeza katonda wammwe, Mukisa,

ne mujuliza katonda wammwe, Kusalawo, ebikopo eby’envinnyo,

1265:12 a Is 27:1 b Nge 1:24-25; Is 41:28; 66:4 c 2By 36:15-16; Yer 7:13ndibawaayo eri ekitala

era mwenna mukutaamirire musalibwe,

kubanga nabayita naye temwayitaba,

nayogera naye temwampuliriza.

Mwakola ebitasaana

era ne musalawo okukola ebitansanyusa.”

1365:13 a Is 1:19 b Is 41:17 c Is 44:9Noolwekyo kino Mukama Ayinzabyonna ky’agamba:

“Abaweereza bange bajja kulya,

naye mmwe mujja kulumwa enjala,

abaweereza bange bajja kunywa,

naye mmwe mulumwe ennyonta;

abaweereza bange bajja kujaguza,

naye mmwe mukwatibwe ensonyi.

1465:14 Mat 8:12; Luk 13:28Abaweereza bange bajja kuyimba

olw’essanyu erinaaba mu mitima gyabwe,

naye mmwe muli ba kukaaba olw’okulumwa okunaabeera mu mitima gyammwe

era mukaabe olw’okulumwa emyoyo.

1565:15 Zek 8:13Ekikolimo kiryoke kibagwire,

Nze Mukama Katonda ow’Eggye mbatte

amannya gammwe geerabirwe,

naye mpe amannya amaggya abo abaŋŋondera.

1665:16 a Zab 31:5 b Is 19:18Kiryoke kibeere nti buli muntu ananoonya okufuna omukisa

anaagunoonya kuva eri Katonda Ow’amazima

buli anaalayiranga mu ggwanga

anaalayiranga Katonda ow’amazima.

Kubanga emitawaana egyayita gya kwerabirwa

gikwekebwe okuva mu maaso gange.

Eggulu Epya n’Ensi Empya

1765:17 a Is 66:22; 2Pe 3:13 b Is 43:18; Yer 3:16“Laba nditonda eggulu eriggya

n’ensi empya.

Ebintu eby’edda tebijja kujjukirwa

wadde okulowoozebwako mu mutima.

1865:18 Zab 98:1-9; Is 25:9Naye musanyukire ekyo kye ntonda

mujaguze emirembe n’emirembe,

kubanga nditonda Yerusaalemi okuba essanyu

n’abantu baamu okuba okujaguza.

1965:19 a Is 35:10; 62:5 b Is 25:8; Kub 7:17Ndijaguza olwa Yerusaalemi

era nsanyukire abantu bange;

amaloboozi ag’okukaaba

tegaliddayo kuwulirwamu.

2065:20 Mub 8:13“Teriddayo kuba mu kyo mwana muwere

anaaberawo ennaku obunaku,

oba omusajja omukulu ataamalengayo myaka gye;

oyo alifiira ku myaka ekikumi

alitwalibwa ng’omuvubuka obuvubuka.

Oyo atalituusa kikumi

abalibwe ng’eyakolimirwa.

2165:21 a Is 32:18 b Is 37:30; Am 9:14Balizimba ennyumba bazisulemu,

balisimba emizabbibu balye ebibala byagyo.

2265:22 a Zab 92:12-14 b Zab 21:4; 91:16Tebalizimba nnyumba ate omulala agisulemu,

tebalisimba ate omulala abirye.

Kubanga emyaka gy’emiti nga bwe giba

bwe gityo bwe giribeera emyaka gy’abantu bange.

Abalonde bange balirwawo nga bawoomerwa

emirimu gy’emikono gyabwe.

2365:23 a Ma 28:3-12; Is 61:9 b Bik 2:39Tebalikolera bwereere

oba okuzaala abaana ab’okugwa mu katyabaga,

kubanga balibeera abantu abaweebwa Mukama Katonda omukisa,

bo awamu n’ab’enda yaabwe.

2465:24 a Is 55:6 b Dan 9:20-23; 10:12Nga tebanakoowoola ndibaddamu,

nga bakyayogera bati mbaddemu.

2565:25 a Is 11:6 b Lub 3:14; Mi 7:17Omusege n’omwana gw’endiga biriire wamu,

era empologoma erye omuddo ng’ennume,

era ettaka libeere emmere y’omusota.

Tewaliba kulumya

wadde kuzikiriza ku lusozi lwange olutukuvu,”

bw’ayogera Mukama Katonda.