Chiweruzo ndi Chipulumutso
1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;
ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.
Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,
ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga
anthu owukira aja,
amene amachita zoyipa,
natsatira zokhumba zawo.
3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa
mopanda manyazi.
Iwo amapereka nsembe mʼminda
ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4Amakatandala ku manda
ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.
Amadya nyama ya nkhumba,
ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,
chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’
Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,
ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;
sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu
chifukwa cha machimo awo
7ndi a makolo awo,”
akutero Yehova.
“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri
ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,
Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata
zimene anachita kale.”
8Yehova akuti,
“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa
ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,
popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’
Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;
sindidzawononga onse.
9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,
ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.
Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,
ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,
ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe
kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11“Koma inu amene mumasiya Yehova
ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,
amene munamukonzera Gadi chakudya
ndi kuthirira Meni chakumwa,
12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,
ndipo nonse mudzaphedwa;
chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,
ndinayankhula koma simunamvere.
Munachita zoyipa pamaso panga
ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,
“Atumiki anga adzadya,
koma inu mudzakhala ndi njala;
atumiki anga adzamwa,
koma inu mudzakhala ndi ludzu;
atumiki anga adzakondwa,
koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14Atumiki anga adzayimba
mosangalala,
koma inu mudzalira kwambiri
chifukwa chovutika mu mtima
ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15Anthu anga osankhidwa
adzatchula dzina lanu potemberera.
Ambuye Yehova adzakuphani,
koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo
adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;
ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo
adzalumbira mwa Mulungu woona.
Pakuti mavuto akale adzayiwalika
ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Chilengedwe Chatsopano
17“Taonani, ndikulenga
mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.
Zinthu zakale sizidzakumbukika,
zidzayiwalika kotheratu.
18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya
chifukwa cha zimene ndikulenga,
pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa
ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu
ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.
Kumeneko sikudzamvekanso kulira
ndi mfuwu wodandaula.
20“Ana sadzafa ali akhanda
ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.
Wamngʼono mwa iwo
adzafa ali ndi zaka 100.
Amene adzalephere kufika zaka 100
adzatengedwa kukhala
wotembereredwa.
21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,
adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,
kapena kudzala ndi ena nʼkudya.
Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo
wautali ngati mitengo.
Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito
ya manja awo nthawi yayitali.
23Sadzagwira ntchito pachabe
kapena kubereka ana kuti aone tsoka;
chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,
iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.
Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.
Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,
koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.
Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala
chinthu chopweteka kapena chowononga,”
akutero Yehova.
惩罚与拯救
1耶和华说:“我向没有求问我的人显现,
让没有寻找我的人寻见,
对没有求告我的国家说,
‘我在这里,我在这里!’
2我整天伸出双手招呼一群悖逆的百姓,
他们却任意妄为,
不走正路,
3不断地当面惹我发怒。
他们在园中献祭,
在砖台上烧香,
4坐在坟场里,
宿在隐秘处。
他们吃猪肉,
用不洁之物做汤,
5还对人说,‘站远点,
别挨近我,因为我比你圣洁!’
我被这些人气得鼻孔冒烟,
整天怒火难息。
6看啊,这些都记录在我面前,
我不会再保持缄默,
我要报应他们,
7按他们和他们祖先的罪报应他们。
我必按他们的所作所为报应他们,
因为他们在山上烧香,
在丘陵上亵渎我。
这是耶和华说的。”
8耶和华说:“人发现一串葡萄尚可酿造新酒时,
一定会说,‘不要毁坏它,
里面还有好葡萄。’
同样,因我仆人的缘故,
我也不会把他们全部毁灭。
9“我必使雅各的后裔兴起,
使犹大人兴起,
继承我的群山。
我拣选的子民必拥有那片土地,
我的仆人必在那里安居。
10沙仑必成为牧放羊群的草场,
亚割谷必成为牛群休憩的地方,
这些地方必属于寻求我的人。
11但至于你们这些背弃我、
忘记我的圣山、
摆宴供奉幸运之神、
调酒祭奠命运之神的人,
12我要使你们注定被杀,
丧身刀下。
因为我呼唤你们,你们不回应;
我讲话,你们不聆听。
你们做我视为恶的事,
专行令我不悦的事。”
13所以主耶和华说:
“看啊,我的仆人必有吃有喝,
你们却要饥渴交加;
我的仆人必欢喜,
你们却要受羞辱;
14我的仆人必欢喜快乐,
扬声歌唱,
你们却要伤心欲绝,
嚎啕大哭。
15我的选民必用你们的名字作咒诅,
主耶和华必杀死你们,
给祂的仆人另起名字。
16因此,在地上求福祉的人都必向信实的上帝祈求,
在地上起誓的人都必凭信实的上帝起誓。
因为过去的苦难已经被遗忘,
从我眼前消失了。
新天新地
17“看啊,我要创造新天新地,
过去的一切都要被遗忘,
从记忆中消失。
18你们要因我创造的一切而永远欢喜快乐。
看啊,我要创造一个充满喜乐的耶路撒冷,
其中的居民个个欢欣。
19我必因耶路撒冷而欢喜,
因我的子民而快乐。
城里再听不见哭泣和哀号声。
20再没有只活几天便夭折的婴儿,
也没有寿数未尽便死的老人,
因为满了百岁便死的人不过算是青年,
不足百岁便死的人被视为受了咒诅。
21他们要建造房屋,安然居住,
栽种葡萄园,吃园中的果子。
22他们建的房屋再不会被别人居住,
他们种的果实再不会被别人享用。
我的子民必像树木一样长寿,
我拣选的人必长享自己亲手劳碌的成果。
23他们不会徒劳,
他们的孩子也不会遇到灾祸,
因为他们及其子孙是蒙上帝赐福的人。
24他们还没有求告,
我就已经应允;
他们正要祷告,
我就已经垂听。
25豺狼和绵羊必一起吃草,
狮子必像牛一样吃草,
蛇必以尘土为食。
在我的整个圣山上,
它们都不伤人,不害物。
这是耶和华说的。”