Yesaya 65 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

La Bible du Semeur

Esaïe 65:1-25

La nouvelle création

Le jugement qui vient

1Je me suis laissé consulter

par des personnes ╵qui ne demandaient rien,

et je me suis laissé trouver

par des personnes ╵qui ne me cherchaient pas.

J’ai dit : « Je suis là, je suis là ! »

aux gens d’un peuple ╵qui n’était pas appelé par mon nom65.1 Autre traduction : qui n’étaient pas appelés par mon nom. Les v. 1-2 sont cités en Rm 10.20-21 d’après l’ancienne version grecque..

2Par contre, j’ai tendu les mains, ╵à longueur de journée, ╵vers un peuple rebelle

qui suivait un chemin ╵qui n’est pas bon,

au gré de ses pensées,

3un peuple qui, sans cesse, ╵provoque ma colère ╵ouvertement.

Ses habitants offrent des sacrifices ╵dans les jardins sacrés,

et brûlent des parfums ╵sur des autels de briques.

4Ils s’asseyent parmi les tombeaux ╵pour consulter les morts

et passent la nuit dans les grottes.

Ils consomment du porc

et remplissent leurs plats ╵de mets impurs.

5Ils crient : « Reste où tu es

et ne m’approche pas,

car je suis trop sacré pour toi65.5 Autre traduction : je te rendrais sacré.. »

Ces choses sont pour moi ╵comme de la fumée ╵qui me monte aux narines,

un feu qui brûle tout le jour.

6Mais tout cela ╵reste écrit devant moi ;

je ne me tairai plus, ╵je le leur ferai payer jusqu’au bout.

7Je leur ferai payer leurs crimes

dit l’Eternel,

en même temps ╵que ceux de leurs ancêtres,

car ils ont brûlé des parfums ╵sur les montagnes

et ils m’ont outragé ╵sur les collines !

Oui, je leur ferai payer jusqu’au bout

ce que mérite ╵leur conduite passée.

8Voici ce que dit l’Eternel :

De même que l’on dit, ╵quand on trouve une grappe bien juteuse ╵sur une vigne :

« Ne la détruisez pas

car il y a en elle ╵quelque chose de bon »,

moi, je ferai de même ╵à cause de mes serviteurs.

Pour ne pas tout détruire,

9je ferai sortir de Jacob ╵une postérité,

oui, de Juda, des gens ╵qui prendront possession ╵de mes montagnes.

Mes élus les posséderont,

mes serviteurs ╵y feront leur demeure.

10La plaine du Saron ╵sera un pâturage ╵pour le menu bétail,

et la vallée d’Akor65.10 La plaine du Saron, en bordure de la mer Méditerranée, était réputée pour sa fertilité. La vallée d’Akor se trouve au nord-ouest de la mer Morte. ╵un gîte pour les bœufs

au profit de mon peuple ╵qui se sera tourné vers moi.

11Mais quant à vous ╵qui abandonnez l’Eternel,

et qui négligez ma montagne sainte,

qui dressez une table ╵au dieu de la Fortune

et remplissez la coupe ╵pour le dieu du Destin,

12je vous destine au glaive,

et vous vous courberez ╵pour passer tous à l’abattoir,

puisque j’ai appelé

et que vous ne m’avez pas répondu,

et puisque j’ai parlé

et que vous ne m’avez pas écouté,

puisque vous avez fait ╵ce que je trouve mal,

et que vous vous êtes complu ╵dans ce qui me déplaît.

13C’est pourquoi, voici ce que dit ╵le Seigneur, l’Eternel :

Mes serviteurs ╵auront de quoi manger,

et vous, vous aurez faim.

Mes serviteurs boiront,

et vous, vous aurez soif.

Mes serviteurs ╵seront dans l’allégresse,

et vous, vous serez dans la honte !

14Mes serviteurs crieront de joie

car ils connaîtront le bonheur.

Quant à vous, vous crierez

le cœur plein de douleur,

vous vous lamenterez,

l’esprit tout abattu.

15Votre nom restera ╵dans les imprécations ╵de mes élus ;

le Seigneur, l’Eternel, ╵fera que vous mouriez,

mais à ses serviteurs ╵il donnera un nom nouveau.

16Et celui qui voudra ╵être béni sur terre

invoquera sur lui ╵une bénédiction ╵au nom du Dieu de vérité,

et sur la terre, ╵qui prêtera serment ╵jurera par le Dieu de vérité.

Nouveaux cieux, nouvelle terre

En effet, les maux du passé ╵seront tous oubliés,

ils disparaîtront de ma vue.

17Je vais créer ╵un ciel nouveau,

une nouvelle terre ;

on ne se rappellera plus ╵les choses d’autrefois,

on n’y pensera plus65.17 Voir Es 66.22 ; 2 P 3.13 ; Ap 21.1..

18Réjouissez-vous plutôt

et soyez à toujours ╵tout remplis d’allégresse

à cause de ce que je crée.

Oui, car je vais créer ╵une Jérusalem ╵remplie de joie

et son peuple plein d’allégresse.

19J’exulterai moi-même ╵à cause de Jérusalem

et je me réjouirai ╵au sujet de mon peuple.

On n’y entendra plus de pleurs

ni de cris de détresse65.19 Voir Ap 21.4..

20Là, plus de nourrisson

emporté en bas âge,

ni de vieillard qui meure ╵avant d’avoir atteint ╵le nombre de ses ans.

Ce sera mourir jeune ╵de mourir centenaire ;

si un pécheur ╵ne dépasse pas les cent ans65.20 Autre traduction : Si quelqu’un n’atteint pas l’âge de cent ans., ╵c’est qu’il aura été maudit.

21Ils se construiront des maisons

et les habiteront ;

ils planteront des vignes

et ils en mangeront les fruits ;

22ils ne bâtiront plus ╵des maisons pour qu’un autre ╵y habite à leur place,

ils ne planteront plus de vignes

pour qu’un autre en mange les fruits.

Car les gens de mon peuple ╵vivront aussi longtemps qu’un arbre.

Mes élus jouiront ╵du fruit de leur travail.

23Ils ne peineront plus pour rien

et les enfants ╵auxquels ils donneront naissance ╵ne seront plus destinés au malheur.

Ils seront une race ╵bénie par l’Eternel,

et leur postérité ╵le sera avec eux.

24Alors, avant qu’ils ne m’invoquent,

je les exaucerai ;

ils parleront encore,

que j’aurai déjà entendu.

25Les loups et les agneaux ╵paîtront ensemble,

le lion mangera du fourrage ╵tout comme le bétail ;

le serpent mordra la poussière.

Il ne se fera plus ╵ni mal, ni destruction,

sur toute ma montagne sainte,

dit l’Eternel65.25 Reprend Es 11.6-9. !