Yesaya 64 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 64:1-12

1Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,

kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!

2Monga momwe moto umatenthera tchire

ndiponso kuwiritsa madzi,

tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,

ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.

3Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,

ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo

kapena kuona

Mulungu wina wonga Inu,

amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.

5Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,

amene amakumbukira njira zanu.

Koma Inu munakwiya,

ife tinapitiriza kuchimwa.

Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?

6Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,

ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;

tonse tafota ngati tsamba,

ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.

7Palibe amene amapemphera kwa Inu

kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;

pakuti mwatifulatira

ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

8Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.

Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;

ife tonse ndi ntchito ya manja anu.

9Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso

musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.

Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,

pakuti tonsefe ndi anthu anu.

10Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;

ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.

11Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,

yatenthedwa ndi moto

ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.

12Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?

Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

King James Version

Isaiah 64:1-12

1Oh that thou wouldest rend the heavens, that thou wouldest come down, that the mountains might flow down at thy presence, 2As when the melting fire burneth, the fire causeth the waters to boil, to make thy name known to thine adversaries, that the nations may tremble at thy presence!64.2 the melting…: Heb. the fire of meltings 3When thou didst terrible things which we looked not for, thou camest down, the mountains flowed down at thy presence. 4For since the beginning of the world men have not heard, nor perceived by the ear, neither hath the eye seen, O God, beside thee, what he hath prepared for him that waiteth for him.64.4 seen…: or, seen a God beside thee, which doeth so for him, etc 5Thou meetest him that rejoiceth and worketh righteousness, those that remember thee in thy ways: behold, thou art wroth; for we have sinned: in those is continuance, and we shall be saved.

6But we are all as an unclean thing, and all our righteousnesses are as filthy rags; and we all do fade as a leaf; and our iniquities, like the wind, have taken us away. 7And there is none that calleth upon thy name, that stirreth up himself to take hold of thee: for thou hast hid thy face from us, and hast consumed us, because of our iniquities.64.7 consumed: Heb. melted64.7 because: Heb. by the hand 8But now, O LORD, thou art our father; we are the clay, and thou our potter; and we all are the work of thy hand.

9¶ Be not wroth very sore, O LORD, neither remember iniquity for ever: behold, see, we beseech thee, we are all thy people. 10Thy holy cities are a wilderness, Zion is a wilderness, Jerusalem a desolation. 11Our holy and our beautiful house, where our fathers praised thee, is burned up with fire: and all our pleasant things are laid waste. 12Wilt thou refrain thyself for these things, O LORD? wilt thou hold thy peace, and afflict us very sore?