Yesaya 64 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 64:1-12

1Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,

kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!

2Monga momwe moto umatenthera tchire

ndiponso kuwiritsa madzi,

tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,

ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.

3Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,

ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo

kapena kuona

Mulungu wina wonga Inu,

amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.

5Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,

amene amakumbukira njira zanu.

Koma Inu munakwiya,

ife tinapitiriza kuchimwa.

Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?

6Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,

ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;

tonse tafota ngati tsamba,

ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.

7Palibe amene amapemphera kwa Inu

kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;

pakuti mwatifulatira

ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.

8Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.

Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;

ife tonse ndi ntchito ya manja anu.

9Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso

musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.

Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,

pakuti tonsefe ndi anthu anu.

10Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;

ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.

11Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,

yatenthedwa ndi moto

ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.

12Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?

Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?

Hoffnung für Alle

Jesaja 64:1-11

1Komm mit Macht – so wie ein Feuer, das im Nu einen Reisighaufen verzehrt und Wasser zum Sieden bringt! Lass deine Gegner erfahren, wer du bist. Die Völker sollen vor dir zittern. 2Denn du vollbringst so furchterregende Taten, wie wir sie uns nicht vorstellen können. Ja, komm doch herab, lass vor deiner Erscheinung die Berge ins Wanken geraten! 3Denn noch nie ist einem so etwas zu Ohren gekommen. Seit die Erde besteht, hat noch niemand von einem Gott wie dir gehört oder einen Gott gesehen, der es mit dir aufnehmen könnte. Nur du kannst den Menschen, die auf dich vertrauen, wirklich helfen.

4Du stehst dem bei, der mit Freude das Rechte tut, der sich nach deinen Geboten richtet und mit dir lebt. Aber auf uns, Herr, bist du zornig, und das mit Recht: Wir haben gesündigt und uns völlig in unsere Irrwege verrannt.64,4 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: Wir haben seit jeher gesündigt und wurden gerettet. 5In deinen Augen sind wir alle unrein geworden, selbst unsere guten Werke sind bloß ein schmutziges Kleid. Wegen unserer Sünden sind wir wie verdorrtes Laub, das zu Boden fällt und vom Wind weggeblasen wird.

6Doch niemand sucht bei dir Hilfe, Herr. Keiner will an dir festhalten. Denn du selbst hast dich von uns abgewandt. Du lässt uns die Folgen unserer Sünden tragen und daran zerbrechen.

7Dennoch bist du, Herr, unser Vater! Wir sind der Ton, und du bist der Töpfer! Wir alle sind Gefäße aus deiner Hand. 8Ach, Herr, sei nicht für immer zornig auf uns! Trag es uns nicht ewig nach, dass wir gegen dich gesündigt haben! Sieh uns an, wir sind doch immer noch dein Volk. 9Die Städte deines Heiligen Landes liegen verwüstet da. Jerusalem ist zerstört; von der einst prächtigen Stadt auf dem Berg Zion stehen nur noch Ruinen. 10Und unser heiliger Tempel, dieser wunderbare Bau, in dem schon unsere Vorfahren dich angebetet haben – er ist ein Raub der Flammen geworden. Die vielen Stätten, an denen unser Herz hing, liegen unter den Trümmern begraben.

11Herr, wie lange willst du noch warten? Wie lange schaust du noch schweigend zu? Willst du uns ganz im Elend versinken lassen?