Yesaya 63 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 63:1-19

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

1Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,

atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?

Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,

akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo

ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

2Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,

ngati za munthu wofinya mphesa?

3“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,

palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.

Ndinawapondereza ndili wokwiya

ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;

magazi awo anadothera pa zovala zanga,

ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.

4Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;

ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.

5Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.

Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;

choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,

ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.

6Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;

ndipo ndinawasakaza

ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

7Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,

ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.

Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.

Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake

Yehova wachitira nyumba ya Israeli

zinthu zabwino zambiri.

8Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,

ana anga amene sadzandinyenga Ine.”

Choncho anawapulumutsa.

9Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,

ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.

Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,

anawanyamula ndikuwatenga

kuyambira kale lomwe.

10Komabe iwo anawukira

ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.

Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo

ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,

masiku a Mose mtumiki wake;

ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,

pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?

Ali kuti Iye amene anayika

Mzimu Woyera pakati pawo?

12Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa

ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?

Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,

kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,

13amene anawayendetsa pa nyanja yozama?

Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,

iwo sanapunthwe;

14Mzimu Woyera unawapumulitsa

ngati mmene ngʼombe zimapumulira.

Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu

kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,

wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.

Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?

Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.

16Koma Inu ndinu Atate athu,

ngakhale Abrahamu satidziwa

kapena Israeli kutivomereza ife;

Inu Yehova, ndinu Atate athu,

kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.

17Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?

Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?

Bwererani chifukwa cha atumiki anu;

mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.

18Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,

adani athu anasakaza malo anu opatulika.

19Ife tili ngati anthu amene

simunawalamulirepo

ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

King James Version

Isaiah 63:1-19

1Who is this that cometh from Edom, with dyed garments from Bozrah? this that is glorious in his apparel, travelling in the greatness of his strength? I that speak in righteousness, mighty to save.63.1 glorious: Heb. decked 2Wherefore art thou red in thine apparel, and thy garments like him that treadeth in the winefat? 3I have trodden the winepress alone; and of the people there was none with me: for I will tread them in mine anger, and trample them in my fury; and their blood shall be sprinkled upon my garments, and I will stain all my raiment. 4For the day of vengeance is in mine heart, and the year of my redeemed is come. 5And I looked, and there was none to help; and I wondered that there was none to uphold: therefore mine own arm brought salvation unto me; and my fury, it upheld me. 6And I will tread down the people in mine anger, and make them drunk in my fury, and I will bring down their strength to the earth.

7¶ I will mention the lovingkindnesses of the LORD, and the praises of the LORD, according to all that the LORD hath bestowed on us, and the great goodness toward the house of Israel, which he hath bestowed on them according to his mercies, and according to the multitude of his lovingkindnesses. 8For he said, Surely they are my people, children that will not lie: so he was their Saviour. 9In all their affliction he was afflicted, and the angel of his presence saved them: in his love and in his pity he redeemed them; and he bare them, and carried them all the days of old.

10¶ But they rebelled, and vexed his holy Spirit: therefore he was turned to be their enemy, and he fought against them. 11Then he remembered the days of old, Moses, and his people, saying, Where is he that brought them up out of the sea with the shepherd of his flock? where is he that put his holy Spirit within him?63.11 shepherd: or, shepherds 12That led them by the right hand of Moses with his glorious arm, dividing the water before them, to make himself an everlasting name? 13That led them through the deep, as an horse in the wilderness, that they should not stumble? 14As a beast goeth down into the valley, the Spirit of the LORD caused him to rest: so didst thou lead thy people, to make thyself a glorious name.

15¶ Look down from heaven, and behold from the habitation of thy holiness and of thy glory: where is thy zeal and thy strength, the sounding of thy bowels and of thy mercies toward me? are they restrained?63.15 the sounding: or, the multitude 16Doubtless thou art our father, though Abraham be ignorant of us, and Israel acknowledge us not: thou, O LORD, art our father, our redeemer; thy name is from everlasting.63.16 our redeemer…: or, our redeemer from everlasting is thy name

17¶ O LORD, why hast thou made us to err from thy ways, and hardened our heart from thy fear? Return for thy servants’ sake, the tribes of thine inheritance. 18The people of thy holiness have possessed it but a little while: our adversaries have trodden down thy sanctuary. 19We are thine: thou never barest rule over them; they were not called by thy name.63.19 they…: Heb. thy name was not called upon them