Yesaya 63 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 63:1-19

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

1Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,

atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?

Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,

akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo

ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

2Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,

ngati za munthu wofinya mphesa?

3“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,

palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.

Ndinawapondereza ndili wokwiya

ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;

magazi awo anadothera pa zovala zanga,

ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.

4Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;

ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.

5Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.

Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;

choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,

ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.

6Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;

ndipo ndinawasakaza

ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

7Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,

ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.

Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.

Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake

Yehova wachitira nyumba ya Israeli

zinthu zabwino zambiri.

8Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,

ana anga amene sadzandinyenga Ine.”

Choncho anawapulumutsa.

9Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,

ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.

Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,

anawanyamula ndikuwatenga

kuyambira kale lomwe.

10Komabe iwo anawukira

ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.

Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo

ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,

masiku a Mose mtumiki wake;

ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,

pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?

Ali kuti Iye amene anayika

Mzimu Woyera pakati pawo?

12Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa

ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?

Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,

kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,

13amene anawayendetsa pa nyanja yozama?

Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,

iwo sanapunthwe;

14Mzimu Woyera unawapumulitsa

ngati mmene ngʼombe zimapumulira.

Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu

kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,

wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.

Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?

Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.

16Koma Inu ndinu Atate athu,

ngakhale Abrahamu satidziwa

kapena Israeli kutivomereza ife;

Inu Yehova, ndinu Atate athu,

kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.

17Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?

Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?

Bwererani chifukwa cha atumiki anu;

mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.

18Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,

adani athu anasakaza malo anu opatulika.

19Ife tili ngati anthu amene

simunawalamulirepo

ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

Hoffnung für Alle

Jesaja 63:1-19

Gott richtet die Völker

1»Wer kommt in roten Kleidern von Bozra her, aus dem Land der Edomiter? Prächtig sieht er aus in seinem Gewand. Stolz schreitet er daher, mit ungebrochener Kraft.« »Ich bin es, der für Recht sorgt«, antwortet der Herr. »Ich kann euch helfen, es steht in meiner Macht.« 2»Warum sind deine Kleider so rot? Hast du Trauben in der Kelter zerstampft?«

3»Ja, ich habe in einer Kelter gestanden. Ganz allein habe ich sie getreten, niemand half mir dabei. In meinem Zorn habe ich die Völker wie Trauben zerstampft. Ihr Blut spritzte auf meine Kleider, alles ist damit besudelt. 4Denn die Zeit war reif, um mit den Völkern abzurechnen und mein Volk von ihrer Unterdrückung zu befreien. 5Ich schaute mich suchend um, aber weit und breit war niemand, der mir helfen wollte. Ich war erstaunt, dass keiner mir beistand. Darum half ich mir selbst, mein Zorn trieb mich an. 6Ja, ich ließ meinem Zorn freien Lauf und brachte die Völker zum Taumeln. Wütend zertrampelte ich sie und tränkte die Erde mit ihrem Blut.«

Wie wunderbar hat der Herr sein Volk geführt!

7Ich will bekennen, wie der Herr uns seine Gnade erwiesen hat; immer wieder erzähle ich von seinen ruhmvollen Taten – wie er mit Liebe und Güte das Volk Israel umsorgte und es mit Wohltaten überschüttete.

8Er dachte: »Sie sind mein Volk, meine Kinder, sicher werden sie mich nicht enttäuschen!« Und so half er ihnen aus ihrer Not. 9Denn wenn sie in Bedrängnis waren, litt auch er. Immer wieder ist er durch seinen Engel zu ihnen gekommen und hat sie gerettet. Er befreite sie damals vor langer Zeit, weil er sie liebte und Mitleid mit ihnen hatte. Er nahm sie auf die Arme und trug sie Tag für Tag.

10Sie aber lehnten sich auf und beleidigten immer wieder seinen Heiligen Geist. Darum wurde er ihr Feind und kämpfte nun selbst gegen sie.

11Da erst dachten sie wieder an die früheren Zeiten, an Mose und sein Volk: »Wo ist der Gott, der damals Mose und die Israeliten durch das Meer führte wie einen Hirten mitsamt seiner Herde? Wo ist er, der sie mit seinem Heiligen Geist beschenkte?63,11 Oder: Wo ist der Gott, der damals Mose aus dem Wasser zog, den Hirten seiner Herde? Wo ist er, der ihn mit seinem Heiligen Geist beschenkte? 12-13Wo ist der mächtige Gott, der Mose beistand?

Damals teilte er das Wasser des Schilfmeers und ließ sein Volk hindurchziehen. Keiner glitt aus; alle liefen so sicher wie Wildpferde in der Steppe. Tat Gott diese Wunder nicht, damit sein Name für alle Zeiten gerühmt würde? 14Der Geist des Herrn führte das Volk und brachte sie schließlich ins Land Kanaan. Hier konnten sie sich niederlassen und Ruhe finden wie eine Herde, die von den Berghängen hinunter in ein grünes Tal kommt.«

So hast du, o Gott, dein Volk damals geführt, damit dein herrlicher Name geehrt wird.

Herr, wende dich uns wieder zu!

15Herr, schau doch herab vom Himmel, von deinem heiligen und majestätischen Thron! Warum setzt du dich nicht mehr mit ganzer Kraft für uns ein? Wo sind deine großen Taten? Warum hältst du dich zurück? Schlägt dein Herz nicht mehr für uns? Ist deine Liebe erloschen? 16Du bist doch unser Vater! Abraham weiß nichts von uns, und auch Jakob kennt uns nicht. Du, Herr, du bist unser Vater. »Unser Erlöser« – so hast du von jeher geheißen. 17Warum lässt du uns vom richtigen Weg abirren? Warum hast du uns so eigensinnig werden lassen, dass wir keine Ehrfurcht mehr vor dir haben? Bitte, wende dich uns wieder zu! Wir sind doch immer noch deine Diener, das Volk, das dir gehört. 18Für kurze Zeit haben die Feinde dein heiliges Volk vertrieben und dein Heiligtum zertreten. 19Es geht uns so, als hättest du nie über uns geherrscht, als wären wir nie das »Volk des Herrn« gewesen!

Ach, Herr, reiß doch den Himmel auf und komm zu uns herab! Lass vor deiner Erscheinung die Berge ins Wanken geraten!