Yesaya 61 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 61:1-11

Uthenga Wabwino wa Yehova

1Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,

chifukwa Yehova wandidzoza

kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.

Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,

ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu

ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.

2Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;

za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.

Wandituma kuti ndikatonthoze olira.

3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,

nkhata ya maluwa yokongola

mʼmalo mwa phulusa,

ndiwapatse mafuta achikondwerero

mʼmalo mwa kulira.

Ndiwapatse chovala cha matamando

mʼmalo mwa mtima wopsinjika.

Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,

yoyidzala Yehova

kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

4Adzamanganso mabwinja akale a mzinda

ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.

Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,

imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.

5Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;

iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.

6Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,

adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.

Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,

ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

7Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;

ndi kuti munalandira

chitonzo ndi kutukwana,

adzakondwera ndi cholowa chawo,

tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,

ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

8“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;

ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.

Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika

ndikupangana nawo pangano losatha.

9Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu

ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.

Aliyense wowaona adzazindikira

kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;

moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.

Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,

ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.

Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,

ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.

11Monga momwe nthaka imameretsa mbewu

ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,

momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando

pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

New International Version – UK

Isaiah 61:1-11

The year of the Lord’s favour

1The Spirit of the Sovereign Lord is on me,

because the Lord has anointed me

to proclaim good news to the poor.

He has sent me to bind up the broken-hearted,

to proclaim freedom for the captives

and release from darkness for the prisoners,61:1 Hebrew; Septuagint the blind

2to proclaim the year of the Lord’s favour

and the day of vengeance of our God,

to comfort all who mourn,

3and provide for those who grieve in Zion –

to bestow on them a crown of beauty

instead of ashes,

the oil of joy

instead of mourning,

and a garment of praise

instead of a spirit of despair.

They will be called oaks of righteousness,

a planting of the Lord

for the display of his splendour.

4They will rebuild the ancient ruins

and restore the places long devastated;

they will renew the ruined cities

that have been devastated for generations.

5Strangers will shepherd your flocks;

foreigners will work your fields and vineyards.

6And you will be called priests of the Lord,

you will be named ministers of our God.

You will feed on the wealth of nations,

and in their riches you will boast.

7Instead of your shame

you will receive a double portion,

and instead of disgrace

you will rejoice in your inheritance.

And so you will inherit a double portion in your land,

and everlasting joy will be yours.

8‘For I, the Lord, love justice;

I hate robbery and wrongdoing.

In my faithfulness I will reward my people

and make an everlasting covenant with them.

9Their descendants will be known among the nations

and their offspring among the peoples.

All who see them will acknowledge

that they are a people the Lord has blessed.’

10I delight greatly in the Lord;

my soul rejoices in my God.

For he has clothed me with garments of salvation

and arrayed me in a robe of his righteousness,

as a bridegroom adorns his head like a priest,

and as a bride adorns herself with her jewels.

11For as the soil makes the young plant come up

and a garden causes seeds to grow,

so the Sovereign Lord will make righteousness

and praise spring up before all nations.