Yesaya 61 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 61:1-11

Uthenga Wabwino wa Yehova

1Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine,

chifukwa Yehova wandidzoza

kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka.

Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima,

ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu

ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.

2Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake;

za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake.

Wandituma kuti ndikatonthoze olira.

3Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni,

nkhata ya maluwa yokongola

mʼmalo mwa phulusa,

ndiwapatse mafuta achikondwerero

mʼmalo mwa kulira.

Ndiwapatse chovala cha matamando

mʼmalo mwa mtima wopsinjika.

Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo,

yoyidzala Yehova

kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.

4Adzamanganso mabwinja akale a mzinda

ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso.

Adzakonzanso mizinda imene inapasuka,

imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.

5Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu;

iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.

6Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova,

adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu.

Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu,

ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.

7Chifukwa manyazi awo anali owirikiza;

ndi kuti munalandira

chitonzo ndi kutukwana,

adzakondwera ndi cholowa chawo,

tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza,

ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.

8“Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo;

ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa.

Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika

ndikupangana nawo pangano losatha.

9Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu

ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina.

Aliyense wowaona adzazindikira

kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”

10Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova;

moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga.

Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso,

ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo.

Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake,

ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.

11Monga momwe nthaka imameretsa mbewu

ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala,

momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando

pamaso pa mitundu yonse ya anthu.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 61:1-11

Amawulire Amalungi ag’Obulokozi

161:1 a Is 11:2 b Zab 45:7 c Mat 11:5; Luk 7:22 d Is 57:15 e Is 42:7; 49:9Omwoyo wa Mukama Katonda ali ku nze,

kubanga Mukama anfuseeko amafuta okubuulira abaavu n’abali obubi ebigambo ebirungi,

antumye okuyimusa abalina emitima egimenyese.

Okulangirira eddembe eri abawambe,

n’abasibe bateebwe

bave mu makomera.

261:2 a Is 49:8; Luk 4:18-19* b Is 34:8 c Is 57:18; Mat 5:4Okulangirira omwaka gwa Mukama

ogw’okulabiramu obulungi bwe;

olunaku lwa Mukama olw’okuwalanirako eggwanga

era n’okuzzaamu amaanyi abo bonna abakungubaga.

361:3 Is 60:20-21Okugabirira abo bonna abali mu Sayuuni abakungubaga,

okubawa engule ey’obubalagavu mu kifo ky’evvu,

n’amafuta ag’essanyu mu kifo ky’ennaku.

Ekyambalo ky’okutendereza

mu kifo ky’omwoyo w’okukeŋŋeentererwa

balyoke bayitibwe miti gy’abutuukirivu, ebisimbe bya Mukama,

balyoke baweebwe ekitiibwa.

461:4 Is 49:8; Ez 36:33; Am 9:14Baliddamu

bazimbe ebyali bizise,

balirongoosa ebibuga

ebyali byerabirwa edda.

561:5 Is 14:1-2Abaamawanga balibalundira ebisibo byammwe,

abagwira babakolere mu nnimiro zammwe ne mu nnimiro z’emizabbibu.

661:6 a Kuv 19:6; 1Pe 2:5 b Is 60:11Era muyitibwe bakabona ba Mukama,

abantu baliboogerako ng’abaweereza ba Mukama,

mulirya obugagga bw’amawanga,

era mu bugagga bwabwe mwe mulyenyumiririza.

761:7 Is 40:2; Zek 9:12Mu kifo ky’ensonyi,

abantu bange baliddizibwawo emirundi ebiri.

Mu kifo ky’okuswala

basanyuke olw’ebyo bye balifuna

era balifuna omugabo gwa mirundi ebiri,

essanyu lyabwe liribeerera emirembe gyonna.

861:8 a Zab 11:7; Is 5:16 b Is 55:3“Kubanga nze, Mukama, njagala obwenkanya,

nkyawa okunyaga era n’obutali butuukirivu.

Mu bwesigwa bwange ndibasasula

era nkole nabo endagaano ey’emirembe n’emirembe.

9N’ezzadde lyabwe liritutumuka nnyo mu mawanga

n’abaana baabwe eri abantu.

Abo bonna abalibalaba balibamanya,

nti bantu Mukama be yawa omukisa.”

1061:10 a Is 25:9; Kbk 3:18 b Zab 132:9; Is 52:1 c Is 49:18; Kub 21:2Nsanyukira nnyo mu Mukama,

emmeeme yange esanyukira mu Katonda wange.

Kubanga annyambazizza ebyambalo eby’obulokozi

era n’anteekako n’omunagiro ogw’obutuukirivu,

ng’omugole omusajja bw’ayambala engule nga kabona,

ng’omugole omukazi bw’ayambala amayinja ge ag’omuwendo.

1161:11 Zab 85:11Kuba nga ettaka bwe livaamu ebimera,

era ng’ennimiro bwereetera ensigo okumeruka,

bw’atyo Mukama Katonda bwalireeta obutuukirivu n’ettendo okumeruka,

ensi zonna zikirabe.