Yesaya 60 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 60:1-22

Ulemerero wa Ziyoni

1“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,

ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.

2Taona, mdima waphimba dziko lapansi

ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,

koma Yehova adzakuwalira iwe,

ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

3Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako

ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.

4“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.

Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;

ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali

ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.

5Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,

mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;

chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe

chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.

6Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,

ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.

Ndipo onse a ku Seba adzabwera

atanyamula golide ndi lubani

uku akutamanda Yehova.

7Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,

nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;

zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,

ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.

8“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,

ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?

9Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;

patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,

zikubweretsa ana ako ochokera kutali,

pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,

kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,

Woyerayo wa Israeli,

pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.

10“Alendo adzamanganso malinga ako,

ndipo mafumu awo adzakutumikira.

Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,

koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.

11Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,

sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,

kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,

akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.

12Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;

adzawonongeka kotheratu.

13“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,

mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni

kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;

ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.

14Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;

onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.

Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;

Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.

15“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,

koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,

ndipo udzakhala malo a chimwemwe

cha anthu amibado yonse.

16Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu

ndi kuleredwa pa maere aufumu,

motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,

Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.

17Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,

ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.

Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa

ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.

Olamulira ako adzakhala a mtendere.

Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.

18Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,

bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,

ndidzakhala malinga ako okuteteza

ndipo udzanditamanda.

19Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,

kapena mwezi kuti uwunikire usiku,

pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,

ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20Dzuwa lako silidzalowanso,

ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;

Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,

ndipo masiku a mavuto ako adzatha.

21Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama

ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.

Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,

ntchito ya manja anga,

kuti aonetse ulemerero wanga.

22Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,

kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.

Ine ndine Yehova,

nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

La Bible du Semeur

Esaïe 60:1-22

L’éclat de la Jérusalem future

Lumière et gloire

1Lève-toi, resplendis, ╵car voici ta lumière,

car sur toi s’est levée ╵la gloire du Seigneur.

2Voici que les ténèbres ╵couvrent la terre

et une nuée sombre60.2 Autre traduction : un épais brouillard. ╵couvre les peuples,

mais, sur toi, l’Eternel ╵se lèvera lui-même ╵comme un soleil

et l’on verra sa gloire ╵apparaître sur toi.

3Des peuples marcheront ╵à ta lumière60.3 Cité en Ap 21.24.,

et des rois à cette clarté ╵qui s’est levée sur toi.

4Regarde autour de toi et vois :

ils se rassemblent tous,

ils viennent jusqu’à toi.

Tes fils viennent de loin,

tes filles sont portées ╵comme des enfants sur la hanche.

5Tu le verras alors, ╵tu brilleras de joie,

ton cœur tressaillira ╵et se dilatera

car, les richesses que transportent ╵les vaisseaux sillonnant la mer ╵seront dirigées vers tes ports.

Les trésors des nations60.5 Cité en Ap 21.24. ╵arriveront chez toi.

6Tu seras submergée ╵par le flot des chameaux.

Les dromadaires ╵de Madian et d’Epha60.6 Madian: tribu nomade du sud-est du Jourdain, aux nombreux éleveurs de chameaux, dont l’origine remonte à Abraham. Epha: un fils de Madian (Gn 25.1-2, 4). ╵couvriront ton pays.

Tous les habitants de Saba60.6 Saba: région opulente du sud de l’Arabie. viendront

et ils apporteront ╵de l’or et de l’encens,

et ils proclameront ╵les louanges de l’Eternel.

7Les moutons et les chèvres de Qédar ╵s’assembleront chez toi,

tous les béliers de Nebayoth60.7 Qédar désigne le désert Arabique avec ses tribus de Bédouins. Nebayoth: autre tribu arabe (Gn 25.13). ╵seront à ton service,

ils monteront sur mon autel ╵en offrande agréée,

et je rendrai splendide ╵le Temple où ma splendeur réside.

8Qui sont ceux-là qui viennent ╵volant comme un nuage,

ou comme des colombes ╵qui regagnent leur colombier ?

9Les habitants des îles ╵et des régions côtières ╵mettront leur espérance en moi,

les vaisseaux au long cours60.9 Autre traduction : de Tarsis, port situé probablement en Espagne. ╵viendront les tout premiers

pour ramener tes fils de loin

avec leur argent et leur or

pour faire honneur ╵à l’Eternel, ton Dieu,

et au Saint d’Israël ╵qui te fait resplendir.

10Les étrangers ╵rebâtiront tes murs,

leurs rois te serviront.

Car je t’avais frappée ╵dans mon indignation,

mais maintenant dans ma faveur ╵je te témoigne ma tendresse.

11Tes portes, jour et nuit, ╵seront toujours ouvertes,

on ne les fermera jamais

pour laisser affluer vers toi

les trésors des nations,

et leurs rois en cortège60.11 Cité en Ap 21.25-26..

12Car la nation ou le royaume

qui ne te seront pas assujettis ╵disparaîtront ;

oui, en effet ces nations-là ╵seront complètement ruinées.

13Le cyprès, le platane ╵et le genévrier

qui font la gloire du Liban ╵te seront apportés

pour embellir le lieu ╵où est mon sanctuaire,

et je rendrai glorieux ╵le lieu où reposent mes pieds.

14Les descendants de ceux ╵qui t’humiliaient

viendront se courber devant toi,

et ceux qui t’insultaient

se prosterneront à tes pieds60.14 Réminiscence en Ap 3.9..

Et l’on t’appellera : ╵« Cité de l’Eternel,

la Sion du Saint d’Israël ».

15Tu étais délaissée, haïe,

nul ne passait chez toi.

Mais je ferai de toi ╵un sujet de fierté ╵à tout jamais,

et un sujet de joie ╵pour toutes les générations.

16Tu téteras le lait au sein

des nations et des rois

et tu sauras que je suis l’Eternel, ╵que c’est moi qui te sauve,

que je suis ton libérateur, ╵le Puissant de Jacob.

17Au lieu du bronze, ╵j’apporterai de l’or,

et de l’argent ╵au lieu du fer,

du bronze au lieu du bois,

du fer au lieu de pierres.

J’établirai sur toi

la paix comme inspecteur,

et la justice

comme dominateur.

18Et l’on n’entendra plus ╵parler de violence ╵dans ton pays,

de dévastation et de destruction ╵dans tes frontières,

et tu appelleras ╵tes murailles « Salut »,

et tes portes « Louange ».

19Ce ne sera plus le soleil ╵qui, désormais, te donnera ╵la lumière du jour ;

la clarté de la lune ╵ne luira plus sur toi la nuit.

Car l’Eternel sera ╵ta lumière à toujours,

oui, ton Dieu sera ta splendeur60.19 Les v. 19-20 sont repris en Ap 21.23..

20Désormais, ton soleil ╵ne se couchera plus

et, jamais plus, ta lune ╵ne se retirera,

car l’Eternel sera ╵ta lumière à toujours,

et les jours de ton deuil ╵auront pris fin pour toi.

21Ton peuple sera tout entier ╵composé d’hommes justes

et ils posséderont ╵le pays pour toujours.

Ils sont les rejetons ╵que j’ai plantés moi-même,

l’ouvrage de mes mains

pour manifester ma splendeur.

22Le plus petit d’entre eux ╵deviendra un millier,

le plus insignifiant, ╵une nation puissante.

C’est moi, moi l’Eternel, ╵qui hâterai ╵en leur temps, ces événements.