Yesaya 6 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 6:1-13

Masomphenya a Yesaya

1Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova. 2Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira. 3Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti

“Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse.

Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”

4Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.

5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”

6Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe. 7Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”

8Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?”

Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”

9Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa:

“ ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;

kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’

10Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;

uwagonthetse makutu,

ndipo uwatseke mʼmaso.

Mwina angaone ndi maso awo,

angamve ndi makutu awo,

angamvetse ndi mitima yawo,

kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”

11Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?”

Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti,

“Mpaka mizinda itasanduka mabwinja

nʼkusowa wokhalamo,

mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo,

mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,

12mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali,

dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.

13Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko,

nachonso chidzawonongedwa.

Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu

imasiyira chitsa pamene ayidula,

chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”

New International Version – UK

Isaiah 6:1-13

Isaiah’s commission

1In the year that King Uzziah died, I saw the Lord, high and exalted, seated on a throne; and the train of his robe filled the temple. 2Above him were seraphim, each with six wings: with two wings they covered their faces, with two they covered their feet, and with two they were flying. 3And they were calling to one another:

‘Holy, holy, holy is the Lord Almighty;

the whole earth is full of his glory.’

4At the sound of their voices the doorposts and thresholds shook and the temple was filled with smoke.

5‘Woe to me!’ I cried. ‘I am ruined! For I am a man of unclean lips, and I live among a people of unclean lips, and my eyes have seen the King, the Lord Almighty.’

6Then one of the seraphim flew to me with a live coal in his hand, which he had taken with tongs from the altar. 7With it he touched my mouth and said, ‘See, this has touched your lips; your guilt is taken away and your sin atoned for.’

8Then I heard the voice of the Lord saying, ‘Whom shall I send? And who will go for us?’

And I said, ‘Here am I. Send me!’

9He said, ‘Go and tell this people:

‘ “Be ever hearing, but never understanding;

be ever seeing, but never perceiving.”

10Make the heart of this people calloused;

make their ears dull

and close their eyes.6:9,10 Hebrew; Septuagint “You will be ever hearing, but never understanding; / you will be ever seeing, but never perceiving.” / 10 This people’s heart has become calloused; / they hardly hear with their ears, / and they have closed their eyes

Otherwise they might see with their eyes,

hear with their ears,

understand with their hearts,

and turn and be healed.’

11Then I said, ‘For how long, Lord?’

And he answered:

‘Until the cities lie ruined

and without inhabitant,

until the houses are left deserted

and the fields ruined and ravaged,

12until the Lord has sent everyone far away

and the land is utterly forsaken.

13And though a tenth remains in the land,

it will again be laid waste.

But as the terebinth and oak

leave stumps when they are cut down,

so the holy seed will be the stump in the land.’