Yesaya 59 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 59:1-21

Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso

1Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,

kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.

2Koma zoyipa zanu zakulekanitsani

ndi Mulungu wanu;

ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,

kotero Iye sadzamva.

3Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.

Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.

Pakamwa panu payankhula zabodza,

ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.

4Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,

palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.

Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;

amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.

5Iwo amayikira mazira a mamba

ndipo amaluka ukonde wakangawude.

Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,

ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.

6Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;

ndipo chimene apangacho sangachifunde.

Ntchito zawo ndi zoyipa,

ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.

7Amathamangira kukachita zoyipa;

sachedwa kupha anthu osalakwa.

Maganizo awo ndi maganizo oyipa;

kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.

8Iwo sadziwa kuchita za mtendere;

zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.

Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;

aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.

9Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;

ndipo chipulumutso sichitifikira.

Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;

tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.

10Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,

kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.

Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;

timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.

11Tonse timabangula ngati zimbalangondo:

Timalira modandaula ngati nkhunda.

Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.

Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”

12Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,

ndipo machimo athu akutsutsana nafe.

Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse

ndipo tikuvomereza machimo athu:

13Tawukira ndi kumukana Yehova.

Tafulatira Mulungu wathu,

pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,

ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.

14Motero kuweruza kolungama kwalekeka

ndipo choonadi chili kutali ndi ife;

kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,

ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.

15Choonadi sichikupezeka kumeneko,

ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.

Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa

kuti panalibe chiweruzo cholungama.

16Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,

Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;

Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,

ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;

17Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,

ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;

anavala kulipsira ngati chovala

ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.

18Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake

molingana ndi zimene anachita,

adzaonetsa ukali kwa adani ake

ndi kubwezera chilango odana naye.

Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.

19Choncho akadzabwera ngati madzi

oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.

Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa

adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.

20“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni

kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,”

akutero Yehova.

21Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,”

akutero Yehova.

La Bible du Semeur

Esaïe 59:1-21

De l’injustice à la justice

Ce qui sépare de Dieu

1Mais non : la main de l’Eternel ╵n’est pas trop courte pour sauver,

et son oreille n’est pas sourde ╵au point de ne plus vous entendre !

2Ce sont vos fautes ╵qui vous séparent

de votre Dieu.

C’est à cause de vos péchés ╵qu’il s’est détourné loin de vous

pour ne plus vous entendre.

3Car vos mains sont souillées de sang

et vos doigts de péchés,

vos lèvres disent des mensonges,

votre langue susurre ╵des paroles perfides.

4Personne n’invoque le droit,

et nul ne plaide ╵selon la vérité.

On s’appuie sur de vains raisonnements

et l’on allègue des mensonges.

Ils conçoivent le mal

et enfantent l’iniquité.

5Ils couvent des œufs de vipère,

tissent des toiles d’araignée.

Qui mange de ces œufs mourra ;

de chaque œuf couvé qui éclôt

sortira un serpent.

6Leurs toiles d’araignée ╵ne servent pas de vêtement,

et l’on ne peut pas se couvrir ╵de ce qu’ils ont confectionné.

Les œuvres qu’ils produisent ╵sont des œuvres mauvaises ;

de leurs mains, ils commettent ╵des actes de violence.

7Leurs pieds courent au mal,

et ils ont hâte ╵de verser le sang innocent.

Leurs pensées sont sans cesse ╵orientées vers le mal,

dévastation et destruction ╵jalonnent leur parcours59.7 Pour les v. 7-8, voir Rm 3.15-17..

8Ils ne connaissent pas ╵le chemin de la paix,

et le droit est absent ╵des routes qu’ils empruntent.

Les sentiers qu’ils se tracent ╵sont des voies tortueuses :

quiconque s’y engage ╵ne connaît pas la paix.

Les péchés du peuple

9Voilà pourquoi le droit ╵demeure loin de nous,

et l’on ne nous rend pas justice.

Nous espérions de la lumière,

et c’est l’obscurité.

Oui, nous espérions la clarté

et nous marchons dans les ténèbres.

10Nous allons à tâtons ╵comme des aveugles ╵le long d’un mur ;

comme ceux qui n’ont plus leurs yeux,

nous allons à tâtons,

nous trébuchons en plein midi ╵comme à la nuit tombante ;

tout en étant pleins de vigueur,

nous sommes comme morts.

11Nous grondons tous comme des ours

et nous ne cessons de gémir ╵tout comme des colombes.

Nous espérons le droit, ╵mais il n’y en a pas ;

et le salut, ╵mais il est loin de nous !

12Car nos révoltes ╵contre toi sont nombreuses

nos transgressions ╵témoignent contre nous.

Nos péchés restent attachés à nous,

et nos fautes, nous les connaissons bien.

13Nous sommes des rebelles

et nous avons trompé ╵l’Eternel, notre Dieu, ╵en lui tournant le dos.

Nous ne parlons que d’oppression ╵et de révolte,

et nous avons conçu, ╵nous avons projeté ╵des propos mensongers ╵dans notre cœur.

14Aussi, le droit recule

et la justice est loin de nous.

La vérité trébuche ╵sur la place publique,

et la droiture ╵ne peut y accéder.

15La vérité a disparu

et celui qui se détourne du mal ╵se fait piller.

Dieu intervient

Mais l’Eternel a vu ╵avec indignation

qu’il n’y a plus de droit.

16Il n’a trouvé personne ╵qui intercède,

il s’en est étonné.

Alors son propre bras ╵lui est venu en aide,

et sa justice ╵a été son soutien59.16 Voir 63.5..

17Il se revêt de la justice ╵comme d’une cuirasse,

il s’est mis sur la tête ╵le casque du salut.

En guise de tunique, ╵il s’est drapé ╵de la rétribution,

il s’est enveloppé ╵comme dans un manteau59.17 Allusion en Ep 6.14-17 ; 1 Th 5.8. ╵d’une ardeur passionnée ╵pour la relation exclusive ╵qui le lie à son peuple.

18Il rendra à chacun ╵ce que lui vaut ses actes :

la fureur à ses adversaires,

et leur dû à ses ennemis ;

il paiera leur salaire ╵aux habitants des îles, ╵et des régions côtières.

19Ainsi, l’on craindra l’Eternel ╵et l’on révérera sa gloire

de l’occident jusqu’au levant.

Car il viendra ╵comme un fleuve en furie

agité par un vent ╵venu de l’Eternel59.19 Verset difficile, interprété de diverses manières..

20Car le libérateur ╵va venir pour Sion,

pour ceux qui, en Jacob, ╵renonceront à leurs révoltes.

L’Eternel le déclare.

21Quant à moi, déclare l’Eternel, voici quelle est l’alliance que je fais avec eux59.21 Les v. 20-21 sont cités en Rm 11.26. : Mon Esprit qui repose sur toi et mes paroles que je mets dans ta bouche59.21 Voir 51.16., ne s’écarteront ni de ta bouche, ni de la bouche de tes enfants, ni de la bouche de leurs enfants. Voilà ce que dit l’Eternel, dès maintenant et pour l’éternité.