Yesaya 58 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 58:1-14

Kusala Kwenikweni

1“Fuwula kwambiri, usaleke.

Mawu ako amveke ngati lipenga.

Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;

uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.

2Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;

amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,

kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola

ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.

Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo

ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.

3Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala

kudya pamene Inu simukulabadirapo?

Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa

pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,

ndipo mumazunza antchito anu onse.

4Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,

mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.

Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.

5Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,

kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?

Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango

ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?

Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,

tsiku lokondweretsa Yehova?

6“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:

Kumasula maunyolo ozunzizira anthu

ndi kumasula zingwe za goli,

kupereka ufulu kwa oponderezedwa

ndi kuphwanya goli lililonse?

7Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?

Osowa ndi ongoyendayenda,

kodi mwawapatsa malo ogona?

Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?

8Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,

ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;

chilungamo chanu chidzakutsogolerani

ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.

9Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;

mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,

ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.

10Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,

ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,

pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,

ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.

11Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;

adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa

ndipo adzalimbitsa matupi anu.

Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,

ngati kasupe amene madzi ake saphwa.

12Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,

ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;

inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.

Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

13“Muzisunga osaphwanya Sabata;

musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,

tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.

Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza

posayenda mʼnjira zanu,

kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,

14mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,

ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.

Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”

Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.