Yesaya 57 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 57:1-21

1Anthu olungama amafa,

ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;

anthu odzipereka amatengedwa,

ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.

Anthu olungama amatengedwa

kuti tsoka lisawagwere.

2Iwo amene amakhala moyo wolungama

amafa mwamtendere;

amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.

3“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,

inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!

4Kodi inu mukuseka yani?

Kodi mukumunena ndani

ndi kupotoza pakamwa panu?

Kodi inu si ana owukira,

zidzukulu za anthu abodza?

5Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,

ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.

Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa

ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.

6Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.

Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,

ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.

Kodi zimenezi

zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?

7Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.

Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.

8Mʼnyumba mwanu mwayika

mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.

Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.

Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,

ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.

Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.

9Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta

ndi zonunkhira zochuluka.

Munachita kutumiza akazembe anu kutali;

inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!

10Inu mumatopa ndi maulendo anu,

koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’

Munapezako kumeneko zokhumba zanu

nʼchifukwa chake simunalefuke.

11“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,

kotero kuti mwakhala mukundinamiza,

ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,

kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?

Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti

ndakhala chete nthawi yayitali?

12Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,

ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.

13Pamene mufuwula kupempha thandizo,

mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!

Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,

mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.

Koma munthu amene amadalira ine

adzalandira dziko lokhalamo.

Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”

Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima

14Ndipo panamveka mawu akuti,

“Undani, undani, konzani msewu!

Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”

15Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,

amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,

akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,

koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima

kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse

ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.

16Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya

kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,

popeza kuti ndinalenga anthu anga

ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.

17Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;

ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,

koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.

18Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;

kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,

19anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.

Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”

“Ndipo ndidzawachiritsa.”

Akutero Yehova.

20Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,

yosatha kukhala bata,

mafunde ake amaponya matope ndi ndere.

21“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

New International Version

Isaiah 57:1-21

1The righteous perish,

and no one takes it to heart;

the devout are taken away,

and no one understands

that the righteous are taken away

to be spared from evil.

2Those who walk uprightly

enter into peace;

they find rest as they lie in death.

3“But you—come here, you children of a sorceress,

you offspring of adulterers and prostitutes!

4Who are you mocking?

At whom do you sneer

and stick out your tongue?

Are you not a brood of rebels,

the offspring of liars?

5You burn with lust among the oaks

and under every spreading tree;

you sacrifice your children in the ravines

and under the overhanging crags.

6The idols among the smooth stones of the ravines are your portion;

indeed, they are your lot.

Yes, to them you have poured out drink offerings

and offered grain offerings.

In view of all this, should I relent?

7You have made your bed on a high and lofty hill;

there you went up to offer your sacrifices.

8Behind your doors and your doorposts

you have put your pagan symbols.

Forsaking me, you uncovered your bed,

you climbed into it and opened it wide;

you made a pact with those whose beds you love,

and you looked with lust on their naked bodies.

9You went to Molek57:9 Or to the king with olive oil

and increased your perfumes.

You sent your ambassadors57:9 Or idols far away;

you descended to the very realm of the dead!

10You wearied yourself by such going about,

but you would not say, ‘It is hopeless.’

You found renewal of your strength,

and so you did not faint.

11“Whom have you so dreaded and feared

that you have not been true to me,

and have neither remembered me

nor taken this to heart?

Is it not because I have long been silent

that you do not fear me?

12I will expose your righteousness and your works,

and they will not benefit you.

13When you cry out for help,

let your collection of idols save you!

The wind will carry all of them off,

a mere breath will blow them away.

But whoever takes refuge in me

will inherit the land

and possess my holy mountain.”

Comfort for the Contrite

14And it will be said:

“Build up, build up, prepare the road!

Remove the obstacles out of the way of my people.”

15For this is what the high and exalted One says—

he who lives forever, whose name is holy:

“I live in a high and holy place,

but also with the one who is contrite and lowly in spirit,

to revive the spirit of the lowly

and to revive the heart of the contrite.

16I will not accuse them forever,

nor will I always be angry,

for then they would faint away because of me—

the very people I have created.

17I was enraged by their sinful greed;

I punished them, and hid my face in anger,

yet they kept on in their willful ways.

18I have seen their ways, but I will heal them;

I will guide them and restore comfort to Israel’s mourners,

19creating praise on their lips.

Peace, peace, to those far and near,”

says the Lord. “And I will heal them.”

20But the wicked are like the tossing sea,

which cannot rest,

whose waves cast up mire and mud.

21“There is no peace,” says my God, “for the wicked.”