Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse
1Yehova akuti,
“Chitani chilungamo
ndi zinthu zabwino,
chifukwa chipulumutso changa chili pafupi
ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,
munthu amene amalimbika kuzichita,
amene amasunga Sabata osaliyipitsa,
ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,
“Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”
Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,
“Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4Popeza Yehova akuti,
“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,
nachita zokomera Ine
ndi kusunga pangano langa,
5ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino
mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,
kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.
Ndidzawapatsa dzina labwino,
losatha ndi losayiwalika.”
6Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,
motero kuti amamutumikira Iye,
amakonda dzina la Yehova,
amamugwirira ntchito,
komanso kusunga Sabata osaliyipitsa
ndi kusunga bwino pangano langa,
7amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,
ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.
Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo
ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.
Paja nyumba yanga idzatchedwa
nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa
Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,
“Ndidzasonkhanitsano anthu ena
kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
Mulungu Adzazula Anthu Oyipa
9Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,
inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,
onse ndi opanda nzeru;
onse ndi agalu opanda mawu,
samatha kuwuwa:
amagona pansi nʼkumalota
amakonda kugona tulo.
11Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;
sakhuta konse.
Abusa nawonso samvetsa zinthu;
onse amachita monga akufunira,
aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!
Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!
Mawa lidzakhala ngati leroli,
kapena kuposa lero lino.”
Tous les peuples acceptés
1Voici ce que dit l’Eternel :
Faites ce qui est juste
et respectez le droit,
car je vais bientôt vous sauver,
je vais faire justice.
2Bienheureux sera l’homme ╵qui agira ainsi,
heureux sera celui ╵qui s’y appliquera :
qui respectera le sabbat,
et ne le profanera pas,
et qui s’efforcera ╵de ne faire aucun mal !
3L’étranger qui s’attache ╵à l’Eternel ╵ne devra pas se dire :
« L’Eternel m’exclura ╵sûrement de son peuple »,
et l’eunuque non plus ╵n’aura pas à penser :
« Je suis un arbre sec ! »
4Car voici ce que l’Eternel déclare :
A ceux qui sont eunuques, ╵qui respecteront les sabbats ╵que j’ai prescrits,
qui choisiront de faire ╵ce qui m’est agréable,
et qui s’attacheront ╵à mon alliance,
5je réserverai ╵dans ma Maison
et dans mes murs ╵une stèle et un nom
qui vaudront mieux pour eux ╵que des fils et des filles ;
je leur accorderai ╵un nom impérissable
qui ne sera jamais rayé.
6Et les étrangers qui s’attacheront
à l’Eternel pour le servir,
et pour l’aimer
et pour être ses serviteurs,
qui respecteront le sabbat
et ne le profaneront pas,
et qui s’attacheront ╵à mon alliance,
7je les ferai venir ╵à ma montagne sainte
et je les réjouirai ╵au Temple où l’on me prie,
et j’agréerai leurs holocaustes ╵et autres sacrifices
offerts sur mon autel.
Car on appellera mon temple : ╵« La Maison de prière ╵pour tous les peuples56.7 Cité par Jésus en Mt 21.13 ; Mc 11.17 ; Lc 19.46.. »
8Voici ce que déclare l’Eternel,
lui qui rassemble ╵les bannis d’Israël :
A ceux qui seront déjà rassemblés
j’en joindrai d’autres ╵que je rassemblerai aussi.
Le changement nécessaire
Les conducteurs indignes
9Vous tous les animaux sauvages,
venez, repaissez-vous,
tous les animaux des forêts56.9 Ces bêtes représentent les ennemis d’Israël invités à venir dévorer le troupeau (le peuple) mal gardé par ses conducteurs infidèles. !
10Les sentinelles d’Israël ╵sont toutes des aveugles :
ce sont des ignorants,
tous sont des chiens muets
qui ne peuvent pas aboyer.
Rêvassant, allongés,
ils aiment somnoler…
11Mais ces chiens sont avides
et jamais rassasiés,
et ce sont des bergers
qui ne comprennent rien.
Ils suivent chacun son chemin
à la poursuite de ses gains.
12« Venez, je vais chercher du vin,
et nous boirons jusqu’à l’ivresse ╵des boissons fortes, disent-ils.
Demain, la fête continue ╵comme aujourd’hui :
il reste du surplus ╵en abondance. »