Yesaya 55 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 55:1-13

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

1“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,

bwerani madzi alipo;

ndipo inu amene mulibe ndalama

bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!

Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka

osalipira ndalama, osalipira chilichonse.

2Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,

ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?

Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;

ndipo mudzisangalatse.

3Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;

mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.

Ndidzachita nanu pangano losatha,

chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.

4Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,

kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.

5Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,

ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.

Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,

Woyerayo wa Israeli,

wakuvekani ulemerero.”

6Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.

Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.

7Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,

ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.

Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,

ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

8“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,

ngakhale njira zanu si njira zanga,”

akutero Yehova.

9“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,

momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,

ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

10Monga mvula ndi chisanu chowundana

zimatsika kuchokera kumwamba,

ndipo sizibwerera komweko

koma zimathirira dziko lapansi.

Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera

kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.

11Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.

Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,

koma adzachita zonse zimene ndifuna,

ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.

12Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe

ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;

mapiri ndi zitunda

zidzakuyimbirani nyimbo,

ndipo mitengo yonse yamʼthengo

idzakuwombereni mʼmanja.

13Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,

ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.

Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,

ngati chizindikiro chamuyaya,

chimene sichidzafafanizika konse.”

Nova Versão Internacional

Isaías 55:1-13

Convite aos Sedentos

1“Venham, todos vocês que estão com sede,

venham às águas;

e vocês que não possuem dinheiro algum,

venham, comprem e comam!

Venham, comprem vinho e leite

sem dinheiro e sem custo.

2Por que gastar dinheiro naquilo que não é pão,

e o seu trabalho árduo naquilo que não satisfaz?

Escutem, escutem-me, e comam o que é bom,

e a alma de vocês se deliciará com a mais fina refeição.

3Deem-me ouvidos e venham a mim;

ouçam-me, para que sua alma viva.

Farei uma aliança eterna com vocês,

minha fidelidade prometida a Davi.

4Vejam, eu o fiz uma testemunha aos povos,

um líder e governante dos povos.

5Com certeza você convocará nações que você não conhece,

e nações que não o conhecem se apressarão até você,

por causa do Senhor, o seu Deus,

o Santo de Israel,

pois ele concedeu a você esplendor.”

6Busquem o Senhor enquanto é possível achá-lo;

clamem por ele enquanto está perto.

7Que o ímpio abandone o seu caminho;

e o homem mau, os seus pensamentos.

Volte-se ele para o Senhor,

que terá misericórdia dele;

volte-se para o nosso Deus,

pois ele dá de bom grado o seu perdão.

8“Pois os meus pensamentos não são os pensamentos de vocês,

nem os seus caminhos são os meus caminhos”,

declara o Senhor.

9“Assim como os céus são mais altos do que a terra,

também os meus caminhos são mais altos do que os seus caminhos;

e os meus pensamentos, mais altos do que os seus pensamentos.

10Assim como a chuva e a neve descem dos céus

e não voltam para eles sem regarem a terra

e fazerem-na brotar e florescer,

para ela produzir semente para o semeador

e pão para o que come,

11assim também ocorre com a palavra que sai da minha boca:

ela não voltará para mim vazia,

mas fará o que desejo

e atingirá o propósito para o qual a enviei.

12Vocês sairão em júbilo

e serão conduzidos em paz;

os montes e colinas

irromperão em canto diante de vocês,

e todas as árvores do campo

baterão palmas.

13No lugar do espinheiro crescerá o pinheiro,

e em vez de roseiras bravas crescerá a murta.

Isso resultará em renome para o Senhor,

para sinal eterno,

que não será destruído.”