Yesaya 55 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 55:1-13

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

1“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,

bwerani madzi alipo;

ndipo inu amene mulibe ndalama

bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!

Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka

osalipira ndalama, osalipira chilichonse.

2Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,

ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?

Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;

ndipo mudzisangalatse.

3Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;

mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.

Ndidzachita nanu pangano losatha,

chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.

4Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,

kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.

5Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,

ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.

Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,

Woyerayo wa Israeli,

wakuvekani ulemerero.”

6Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.

Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.

7Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,

ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.

Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,

ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

8“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,

ngakhale njira zanu si njira zanga,”

akutero Yehova.

9“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,

momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,

ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

10Monga mvula ndi chisanu chowundana

zimatsika kuchokera kumwamba,

ndipo sizibwerera komweko

koma zimathirira dziko lapansi.

Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera

kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.

11Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.

Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,

koma adzachita zonse zimene ndifuna,

ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.

12Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe

ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;

mapiri ndi zitunda

zidzakuyimbirani nyimbo,

ndipo mitengo yonse yamʼthengo

idzakuwombereni mʼmanja.

13Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,

ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.

Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,

ngati chizindikiro chamuyaya,

chimene sichidzafafanizika konse.”

New Russian Translation

Исаия 55:1-13

Вечный завет

1– Эй, все, кто жаждет,

придите к водам;

и те, у кого нет денег,

приходите, получайте еду и ешьте!

Приходите, получайте вино и молоко

без денег, бесплатно!

2Зачем тратить деньги на то, что не хлеб,

свои трудовые – на то, что не насыщает?

Слушайте Меня внимательно и ешьте хорошее;

пусть душа ваша порадуется сытной пище.

3Внимайте и приходите ко Мне;

слушайте, чтобы жива была душа ваша.

Я заключу с вами вечный завет,

нетленную милость55:3 Или: «любовь»., обещанную Давиду.

4Вот, Я сделал его свидетелем для народов,

вождем и повелителем народов.

5Вот, ты призовешь народы, которых не знаешь,

и народы, не знающие тебя, устремятся к тебе

из-за Господа, твоего Бога,

Святого Израиля,

потому что Он прославил тебя.

6Ищите Господа, пока Его можно найти,

призывайте Его, пока Он близко.

7Пусть нечестивый оставит свой путь

и злой человек – свои помыслы.

Пусть обратится к Господу,

и Он его помилует,

к нашему Богу,

потому что Он щедр на прощение.

8– Мои мысли – не ваши мысли,

а пути ваши – не Мои пути, –

возвещает Господь. –

9Как небо выше земли,

так Мои пути выше ваших путей,

и Мои мысли выше ваших мыслей.

10Как дождь и снег нисходят с небес

и не возвращаются, не напоив землю,

но делают ее способной рождать и произращать,

чтобы она дала сеятелю зерно

и едоку хлеб,

11так и слово Мое,

что исходит из Моих уст:

оно не вернется ко Мне напрасным,

но совершит то, чего Я хочу,

и достигнет того,

для чего Я его посылал.

12Вы выйдете в радости,

проводят вас с миром.

Горы и холмы запоют перед вами песню,

а все деревья в поле будут рукоплескать.

13Вместо терновника вырастет кипарис,

а вместо колючек – мирт55:13 Мирт – южное вечнозеленое дерево или кустарник с белыми душистыми цветками..

И будет это для славы Господа,

знамением вечным, неистребимым.