Yesaya 55 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 55:1-13

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

1“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,

bwerani madzi alipo;

ndipo inu amene mulibe ndalama

bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!

Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka

osalipira ndalama, osalipira chilichonse.

2Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,

ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?

Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;

ndipo mudzisangalatse.

3Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;

mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.

Ndidzachita nanu pangano losatha,

chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.

4Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,

kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.

5Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,

ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.

Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,

Woyerayo wa Israeli,

wakuvekani ulemerero.”

6Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.

Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.

7Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,

ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.

Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,

ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

8“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,

ngakhale njira zanu si njira zanga,”

akutero Yehova.

9“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,

momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,

ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

10Monga mvula ndi chisanu chowundana

zimatsika kuchokera kumwamba,

ndipo sizibwerera komweko

koma zimathirira dziko lapansi.

Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera

kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.

11Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.

Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,

koma adzachita zonse zimene ndifuna,

ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.

12Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe

ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;

mapiri ndi zitunda

zidzakuyimbirani nyimbo,

ndipo mitengo yonse yamʼthengo

idzakuwombereni mʼmanja.

13Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,

ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.

Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,

ngati chizindikiro chamuyaya,

chimene sichidzafafanizika konse.”

Hoffnung für Alle

Jesaja 55:1-13

Kommt, es kostet nichts!

1Der Herr ruft: »Ihr habt Durst? Kommt her, hier gibt es Wasser! Auch wer kein Geld hat, kann kommen. Nehmt euch Brot und esst! Hierher! Hier gibt es Wein und Milch. Bedient euch, es kostet nichts! 2Warum gebt ihr euer sauer verdientes Geld aus für Brot, das nichts taugt, und für Nahrung, die euch nicht sättigt? Hört doch auf mich und tut, was ich sage, dann habt ihr es gut! Ihr dürft köstliche Speisen genießen und euch daran satt essen. 3Hört mir zu und kommt her! Ja, nehmt meine Worte an, dann werdet ihr leben!

Ich will einen Bund für alle Zeiten mit euch schließen und euch die Gnade erweisen, die ich David versprochen habe. 4Ich habe ihn dazu bestimmt, vielen Völkern meine Wahrheit zu bezeugen, und habe ihn als Herrscher über sie eingesetzt. 5Auch ihr sollt Menschen aus anderen Völkern zu euch rufen, die ihr nicht kennt und die euch nicht kennen. Sie werden zu euch eilen, weil ich, der Herr, euer Gott bin. Ja, sie kommen, um mich kennen zu lernen, den heiligen Gott Israels. Denn ich bin es, der euch Israeliten zu Ehren bringt.«

Mein Wort bleibt nicht ohne Wirkung

6Sucht den Herrn, solange er sich finden lässt! Betet zu ihm, solange er euch nahe ist! 7Hast du dich gegen Gott aufgelehnt? Bist du eigene Wege gegangen und eigenen Plänen gefolgt? Dann hör auf damit! Kehr deinem alten Leben den Rücken und komm zum Herrn! Er wird sich über dich erbarmen, denn unser Gott ist gern zum Vergeben bereit.

8Er sagt: »Meine Gedanken sind nicht eure Gedanken, und meine Wege sind nicht eure Wege. 9Denn wie der Himmel die Erde überragt, so sind auch meine Wege viel höher als eure Wege und meine Gedanken als eure Gedanken.

10Denkt an den Regen und den Schnee! Sie fallen vom Himmel und bleiben nicht ohne Wirkung: Sie tränken die Erde und machen sie fruchtbar; alles sprießt und wächst. So bekommt der Bauer wieder Samen für die nächste Aussaat, und er hat genügend Brot zu essen. 11Genauso ist mein Wort: Es bleibt nicht ohne Wirkung, sondern erreicht, was ich will, und führt das aus, was ich ihm aufgetragen habe.

12Ihr werdet voller Freude in die Freiheit hinausziehen und wohlbehütet euren Weg gehen. Berge und Hügel brechen in Jubel aus, und die Bäume am Weg klatschen in die Hände. 13Anstelle der Dornenbüsche wachsen Zypressen, und wo heute Brennnesseln wuchern, schießen Myrtensträucher empor. Dadurch wird mein Name überall bekannt. Mit eurer Erlösung setze ich für immer ein Zeichen, das nicht mehr aus der Welt zu schaffen ist.«