Yesaya 54 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 54:1-17

Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni

1“Sangalala, iwe mayi wosabala,

iwe amene sunabalepo mwana;

imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,

iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;

chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri

kuposa mkazi wokwatiwa,”

akutero Yehova.

2Kulitsa malo omangapo tenti yako,

tambasula kwambiri nsalu zake,

usaleke;

talikitsa zingwe zako,

limbitsa zikhomo zako.

3Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;

ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina

ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.

4“Usachite mantha; sadzakunyozanso.

Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.

Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako

ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.

5Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;

dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.

6Yehova wakuyitananso,

uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,

mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”

akutero Mulungu wako.

7“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,

koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.

8Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa

ndili wokwiya kwambiri.

Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,

ndidzakuchitira chifundo,”

akutero Yehova Mpulumutsi wako.

9“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.

Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.

Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,

sindidzakudzudzulaninso.

10Ngakhale mapiri atagwedezeka

ndi zitunda kusunthidwa,

koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.

Pangano langa lamtendere silidzasintha,”

akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.

11“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza,

Ine ndidzakongoletsa miyala yako.

Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.

12Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi.

Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto,

ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.

13Yehova adzaphunzitsa ana ako onse,

ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.

14Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni:

Sudzakhalanso wopanikizika,

chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse.

Sudzakhalanso ndi mantha

chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.

15Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa;

aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.

16“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo

amene amakoleza moto wamakala

ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito.

Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;

17palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,

ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.

Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.

Chipambano chawo chichokera kwa Ine,”

akutero Yehova.

New International Version – UK

Isaiah 54:1-17

The future glory of Zion

1‘Sing, barren woman,

you who never bore a child;

burst into song, shout for joy,

you who were never in labour;

because more are the children of the desolate woman

than of her who has a husband,’

says the Lord.

2‘Enlarge the place of your tent,

stretch your tent curtains wide,

do not hold back;

lengthen your cords,

strengthen your stakes.

3For you will spread out to the right and to the left;

your descendants will dispossess nations

and settle in their desolate cities.

4‘Do not be afraid; you will not be put to shame.

Do not fear disgrace; you will not be humiliated.

You will forget the shame of your youth

and remember no more the reproach of your widowhood.

5For your Maker is your husband –

the Lord Almighty is his name –

the Holy One of Israel is your Redeemer;

he is called the God of all the earth.

6The Lord will call you back

as if you were a wife deserted and distressed in spirit –

a wife who married young,

only to be rejected,’ says your God.

7‘For a brief moment I abandoned you,

but with deep compassion I will bring you back.

8In a surge of anger

I hid my face from you for a moment,

but with everlasting kindness

I will have compassion on you,’

says the Lord your Redeemer.

9‘To me this is like the days of Noah,

when I swore that the waters of Noah would never again cover the earth.

So now I have sworn not to be angry with you,

never to rebuke you again.

10Though the mountains be shaken

and the hills be removed,

yet my unfailing love for you will not be shaken

nor my covenant of peace be removed,’

says the Lord, who has compassion on you.

11‘Afflicted city, lashed by storms and not comforted,

I will rebuild you with stones of turquoise,54:11 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.

your foundations with lapis lazuli.

12I will make your battlements of rubies,

your gates of sparkling jewels,

and all your walls of precious stones.

13All your children will be taught by the Lord,

and great will be their peace.

14In righteousness you will be established:

tyranny will be far from you;

you will have nothing to fear.

Terror will be far removed;

it will not come near you.

15If anyone does attack you, it will not be my doing;

whoever attacks you will surrender to you.

16‘See, it is I who created the blacksmith

who fans the coals into flame

and forges a weapon fit for its work.

And it is I who have created the destroyer to wreak havoc;

17no weapon forged against you will prevail,

and you will refute every tongue that accuses you.

This is the heritage of the servants of the Lord,

and this is their vindication from me,’

declares the Lord.