Ulemerero Wamʼtsogolo wa Ziyoni
1“Sangalala, iwe mayi wosabala,
iwe amene sunabalepo mwana;
imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe,
iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka;
chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri
kuposa mkazi wokwatiwa,”
akutero Yehova.
2Kulitsa malo omangapo tenti yako,
tambasula kwambiri nsalu zake,
usaleke;
talikitsa zingwe zako,
limbitsa zikhomo zako.
3Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere;
ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina
ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4“Usachite mantha; sadzakunyozanso.
Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso.
Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako
ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako,
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu;
dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6Yehova wakuyitananso,
uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima,
mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,”
akutero Mulungu wako.
7“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya,
koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa
ndili wokwiya kwambiri.
Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya,
ndidzakuchitira chifundo,”
akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa.
Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi.
Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima,
sindidzakudzudzulaninso.
10Ngakhale mapiri atagwedezeka
ndi zitunda kusunthidwa,
koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha.
Pangano langa lamtendere silidzasintha,”
akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza,
Ine ndidzakongoletsa miyala yako.
Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi.
Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto,
ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13Yehova adzaphunzitsa ana ako onse,
ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni:
Sudzakhalanso wopanikizika,
chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse.
Sudzakhalanso ndi mantha
chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa;
aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo
amene amakoleza moto wamakala
ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito.
Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke,
ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa.
Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova.
Chipambano chawo chichokera kwa Ine,”
akutero Yehova.
Ekitiibwa Kya Sayuuni eky’Oluvannyuma
154:1 a Is 49:20 b 1Sa 2:5; Bag 4:27*“Yimba ggwe omugumba
atazaalanga;
tandika okuyimbira mu ddoboozi ery’omwanguka osanyukire ddala
ggwe atalumwanga kuzaala.
Kubanga ggwe eyalekebwa
ojja kuba n’abaana bangi okusinga oyo akyalina bba,”
bw’ayogera Mukama.
254:2 a Is 49:19-20 b Kuv 35:18; 39:40“Gaziya weema yo, owanvuye emiguwa gyayo,
tokwata mpola;
nyweza enkondo zo.
354:3 Is 49:19Kubanga olisaasaanira
ku mukono gwo ogwa ddyo
era n’ogwa kkono,
n’ezzadde lyo lirirya amawanga,
era abantu bo balituula mu bibuga ebyalekebwa awo ebyereere.
454:4 Is 51:7“Totya kubanga toliddayo kukwatibwa nsonyi.
Toggwaamu maanyi kubanga togenda kuswazibwa.
Olyerabira ensonyi z’obuvubuka bwo,
n’ekivume ky’obwannamwandu bwo tolikijjukira nate.
554:5 a Yer 3:14 b Is 48:17 c Is 6:3Kubanga Omutonzi wo ye balo,
Mukama Katonda ow’Eggye lye linnya lye.
Omutukuvu wa Isirayiri ye Mununuzi wo,
Katonda ow’ensi yonna, bw’ayitibwa.
654:6 a Is 49:14-21 b Is 50:1-2; 62:4, 12Kubanga Mukama Katonda yakuyita okomewo,
ng’omukazi eyali alekeddwawo ng’alina ennaku ku mutima;
omukazi eyafumbirwa ng’akyali muto, n’alekebwawo,”
bw’ayogera Katonda wo.
754:7 a Is 26:20 b Is 49:18“Nakulekako akaseera katono nnyo;
naye ndikukuŋŋaanya n’okusaasira okungi.
854:8 a Is 60:10 b nny 10Obusungu obubuubuuka bwe bwankwata
nakweka amaaso gange okumala ekiseera,
naye ndikukwatirwa ekisa n’okwagala okutaliggwaawo,”
bw’ayogera Mukama Katonda,
Omununuzi wo.
954:9 a Lub 8:21 b Is 12:1“Kubanga gye ndi,
bino biri nga bwe byali mu biseera bya Nuuwa.
Nga bwe nalayira nti amazzi ga Nuuwa tegagenda kuddamu kulabikako ku nsi,
bwe ntyo ndayira nti siriddayo kukusunguwalira wadde okukunenya.
1054:10 a Zab 46:2 b Is 51:6 c Zab 89:34 d nny 8Kubanga ensozi ziyinza okuvaawo n’obusozi okuggyibwawo
naye okwagala kwange okutaggwaawo tekulisagaasagana
so n’endagaano yange ey’emirembe
teriggyibwawo,”
bw’ayogera Mukama Katonda akusaasira.
Yerusaalemi eky’Ebiro Ebijja
1154:11 a Is 14:32 b Is 28:2; 29:6 c Is 51:19 d 1By 29:2; Kub 21:18 e Is 28:16; Kub 21:19-20Mukama agamba nti,
“Ggwe Yerusaalemi ekibuga ekibonyaabonyezebwa, ekisuukundibwa emiyaga awatali kulaba ku mirembe;
laba ndikuzimba buto n’amayinja ag’amabala amalungi,
emisingi gyo ne gizimbibwa ne safiro.
12Ebitikkiro byo ndibikola n’amayinja amatwakaavu,
n’emiryango gyo ne ngikola ne kabunkulo,
ne bbugwe yenna ne mwetoolooza amayinja ag’omuwendo.
1354:13 a Yk 6:45* b Is 48:18N’abaana bo bonna baliyigirizibwa Mukama;
n’emirembe gy’abaana bo giriba mingi.
1454:14 Is 9:4Olinywezebwa mu butuukirivu
era toojoogebwenga,
kubanga tolitya,
onoobanga wala n’entiisa kubanga terikusemberera.
1554:15 Is 41:11-16Omuntu yenna bwakulumbanga kiriba tekivudde gye ndi.
Buli anaakulumbanga anaawangulwanga ku lulwo.
16Laba nze natonda omuweesi,
awujja amanda agaliko omuliro
n’aweesa ekyokulwanyisa olw’omugaso gwakyo.
Era nze natonda abazikiriza abakozesa ekyokulwanyisa okumalawo obulamu.
1754:17 a Is 29:8 b Is 45:24-25Naye teri kyakulwanyisa kye baliweesa ekirikwolekera ne kikusobola,
era oliwangula buli lulimi olulikuvunaana era oluwoza naawe.
Guno gwe mugabo gw’abaddu ba Mukama,
n’obutuukirivu bwabwe obuva gye ndi,”
bw’ayogera Mukama.