Yesaya 52 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 52:1-15

1Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni,

vala zilimbe.

Vala zovala zako zokongola,

iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika.

Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa

sadzalowanso pa zipata zako.

2Sasa fumbi lako;

imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu.

Inu omangidwa a ku Ziyoni,

masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.

3Pakuti Yehova akuti,

“Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani,

choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”

4Pakuti Ambuye Yehova akuti,

“Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto;

nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”

5Tsopano Ine Yehova ndikuti,

“Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu,

amene amawalamulira amawanyoza,”

akutero Yehova.

“Ndipo tsiku lonse, akungokhalira

kuchita chipongwe dzina langa.

6Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa;

kotero adzadziwa

kuti ndi Ine amene ndikuyankhula,

Indedi, ndine.”

7Ngokongoladi mapazi a

amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.

Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,

chisangalalo ndi chipulumutso.

Iwo akubwera kudzawuza anthu

a ku Ziyoni kuti,

“Mulungu wako ndi mfumu!”

8Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;

akuyimba pamodzi mwachimwemwe.

Popeza akuona chamaso

kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.

9Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,

inu mabwinja a Yerusalemu,

pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,

wapulumutsa Yerusalemu.

10Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika

pamaso pa anthu a mitundu yonse,

ndipo anthu onse a dziko lapansi

adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

11Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko!

Musakhudze kanthu kodetsedwa!

Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova

tulukanimo ndipo mudziyeretse.

12Koma simudzachoka mofulumira

kapena kuchita chothawa;

pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu,

Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.

Kuzunzika ndi Ulemerero wa Mtumiki

13Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake

adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.

14Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,

chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.

Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.

15Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,

ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.

Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,

ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 52:1-15

錫安必獲救

1錫安啊,醒來吧,醒來吧,展示你的能力!

聖城耶路撒冷啊,

穿上你華美的衣服!

從今以後,

未受割禮和不潔淨的人必不得進入你的城門。

2耶路撒冷啊,抖掉身上的灰塵,

起來坐到寶座上!

被擄的錫安城啊,

卸去你頸上的鎖鏈!

3耶和華說:「你們被賣未得分文,你們被贖回也不需分文。」 4主耶和華說:「起先我的子民到埃及寄居,後來亞述人無緣無故地欺壓他們。」 5耶和華說:「我這裡還有什麼呢?我的子民白白地被擄去,轄制他們的人咆哮大叫,我的名整天被褻瀆。 6然而,我的子民終會認識我的名。到那日,他們就會知道是我對他們說,『我在這裡。』」

7那穿山越嶺之人的腳蹤是何等佳美!

他帶來佳音,報告平安,

傳遞喜訊,宣佈救恩,

錫安說:「你的上帝做王了。」

8聽啊,你的守望者都一同高聲歡呼,

因為耶和華回到錫安的時候,

他們必親眼看見。

9耶路撒冷的荒場啊,

你們要一同歡呼歌唱,

因為耶和華安慰了祂的子民,

救贖了耶路撒冷

10耶和華要向萬國展現祂神聖的大能,

普天下將看見我們上帝的救恩。

11離開吧,離開吧,

離開巴比倫吧!

不要碰不潔淨的東西。

你們抬耶和華器具的人啊,

要從那裡出來,要潔淨自己。

12你們不必匆忙離開,

也不用奔逃,

因為耶和華必走在你們前面,

以色列的上帝必作你們的後盾。

13看啊,我的僕人必成功,

受到擁戴、仰慕和尊崇。

14許多人看見祂就詫異,

祂的面容被毀、身體被殘害得不成人樣。

15祂必洗淨許多國家,

君王必因祂而閉口無言。

因為他們將看見未曾聽過的事,

明白聞所未聞的事。